< Danieli 12 >
1 “Pa nthawi imeneyo Mikayeli, mngelo wamkulu amene amateteza anthu a mtundu wako, adzabwera. Imeneyi idzakhala nthawi ya mavuto aakulu omwe sanaonekepo kuyambira pachiyambi cha mitundu ya anthu mpaka nthawi ikudzayo. Komatu pa nthawiyi anthu a mtundu wako, aliyense amene dzina lake lidzapezeke lolembedwa mʼbuku adzapulumutsidwa.
“Ngalesosikhathi uMikhayeli, umbusi omkhulu olinda abantu bakini, uzavela. Kuzakuba khona isikhathi sokuhlukumezeka okungazange kube khona kulokhu kwadabuka izizwe kuze kube yiso. Kodwa kulesosikhathi abantu bakini bonke labo abalamabizo azafunyanwa elotshiwe encwadini bazahlengwa.
2 Ambiri mwa amene akugona mʼnthaka adzadzuka: ena adzapita ku moyo wosatha, ena ku malo amanyazi ndi chilango chosatha.
Izixuku lezixuku zabaleleyo othulini lomhlaba bazavuka; abanye baye ekuphileni okungapheliyo, abanye baye ehlazweni lokunengeka okungapheliyo.
3 Amene ali anzeru mʼnjira ya chilungamo adzawala ngati kuwala kwa mlengalenga, ndipo amene alondolera ambiri ku njira yolungama, adzawala ngati nyenyezi ku nthawi zosatha.
Labo abahlakaniphileyo bazakhazimula njengokubenyezela kwamazulu, lalabo abaholela abanengi ekulungeni, bazakhazimula njengezinkanyezi okwanini lanini.
4 Koma iweyo, Danieli, sungitsa mawuwa, umate bukuli kufikira nthawi ya chimaliziro. Anthu ambiri adzapita uku ndi uko ndipo nzeru zidzanka zikukulirakulira.”
Kodwa wena Danyeli, vala ungcine amazwi omgoqwancwadi kuze kube yisikhathi sokucina. Abanengi bazakuya lapha lale ukwandisa ulwazi.”
5 Kenaka ine Danieli poyangʼana ndinaona anthu ena awiri atayima, wina tsidya lino la mtsinje, wina tsidya linalo.
Kwathi mina, Danyeli, ngakhangela, ngabona khonapho phambi kwami kumi abanye ababili, omunye ngakuleli ikhumbi lomfula lomunye ngakuleliyana ikhumbi.
6 Mmodzi mwa awiriwo anafunsa munthu wovala chovala chosalala amene anali mʼmbali mwa madzi a mu mtsinje uja kuti, “Kodi padzapita nthawi yayitali bwanji kuti zodabwitsazi zidzakwaniritsidwe?”
Omunye wabo wathi emuntwini owayegqoke ilineni owayengaphezulu kwamanzi omfula, “Kuzakuba yisikhathi esingakanani zingakenzakali izinto lezi eziyisimanga na?”
7 Munthu wovala chovala chosalala, amene anali mʼmbali mwa madzi a mu mtsinje uja, anakweza dzanja lake lamanja ndi lamanzere kumwamba, ndipo ndinamumva akulumbira mʼdzina la Wamoyo ku nthawi zonse uja kuti, “Zidzachitika patapita zaka zitatu ndi theka. Zinthu zonsezi zidzachitika akadzatha masautso amene agwera anthu olungama.”
Indoda eyayigqoke ilineni, eyayiphezulu kwamanzi omfula yaphakamisela isandla sayo sokunene lesandla sayo sokhohlo ezulwini, ngayizwa ifunga ngaye ohleziyo laphakade, isithi, “Kuzakuba ngokwesikhathi, izikhathi lengxenye yesikhathi. Lapho amandla abantu abangcwele eseze afohlozwa, zonke lezi izinto zizapheleliswa.”
8 Ndinamva, koma sindinamvetsetse. Choncho ndinafunsa kuti, “Mbuye wanga, nanga matsiriziro a zonsezi adzakhala chiyani?”
Ngezwa, kodwa kangizwisisanga. Yikho ngabuza ngathi, “Nkosi yami, pho sizaba yini isiphetho sakho konke lokhu na?”
9 Ndipo anandiyankha kuti, “Pita iwe Danieli, pakuti mawuwa ndi osungidwa ndi omatidwa kufikira nthawi ya chimaliziro.
Waphendula wathi, “Zihambele, Danyeli, ngoba amazwi asevaliwe ananyekwa kuze kube sekucineni kwesikhathi.
10 Anthu ambiri adzayeretsedwa nakhala olungama wopanda chodetsa, koma oyipa adzakhala chiyipire. Palibe mmodzi wa anthu oyipa amene adzamvetsetsa koma okhawo amene ali anzeru adzamvetsetsa.
Abanengi bazahlanjululwa, bangabi latshatha njalo bacolisiswe, kodwa abagangileyo bazaqhubeka begangile. Kakho kwababi ozazwisisa, kodwa labo abahlakaniphileyo bazazwisisa.”
11 “Kuyambira pamene nsembe ya tsiku ndi tsiku idzathetsedwa ndi kukhazikitsa kwa chonyansa chobweretsa chisokonezo chija, padzapita masiku 1,290.
Kusukela ngesikhathi kusaliswa umhlatshelo wansuku zonke, sekumiswe amanyala abanga incithakalo, kuzakuba lensuku eziyinkulungwane lamakhulu amabili lamatshumi ayisificamunwemunye.
12 Wodala munthu amene adikirabe nadzafika pa mapeto a masiku 1,335.
Ubusisiwe lowo okulindelayo njalo akufice ukucina kwensuku eziyinkulungwane lamakhulu amathathu alamatshumi amathathu lanhlanu.
13 “Koma iweyo Danieli, pitiriza ndipo ulimbikire mpaka matsiriziro. Kenaka udzamwalira. Koma mʼmasiku otsiriza udzauka kuti ulandire gawo lako.”
“Kodwa wena, zihambele nje kuze kube sekucineni. Uzaphumula, besekusithi ekucineni kwensuku uzavuka ukuba wamukele elakho ilifa olabelweyo.”