< Danieli 12 >

1 “Pa nthawi imeneyo Mikayeli, mngelo wamkulu amene amateteza anthu a mtundu wako, adzabwera. Imeneyi idzakhala nthawi ya mavuto aakulu omwe sanaonekepo kuyambira pachiyambi cha mitundu ya anthu mpaka nthawi ikudzayo. Komatu pa nthawiyi anthu a mtundu wako, aliyense amene dzina lake lidzapezeke lolembedwa mʼbuku adzapulumutsidwa.
És abban az időben támad Mikháél, a nagy vezér, a ki mellettük áll a te néped fiainak és lészen szorongatás ideje, milyen még nem volt, a mióta nemzet létezik, egészen addig az időig; és abban az időben meg fog menekülni a te néped, mindenki, a ki fölírva találtatik a könyvben.
2 Ambiri mwa amene akugona mʼnthaka adzadzuka: ena adzapita ku moyo wosatha, ena ku malo amanyazi ndi chilango chosatha.
És sokan a föld porában alvók közül föl fognak ébredni: ezek örök életre s amazok gyalázatra, örök undorodásra.
3 Amene ali anzeru mʼnjira ya chilungamo adzawala ngati kuwala kwa mlengalenga, ndipo amene alondolera ambiri ku njira yolungama, adzawala ngati nyenyezi ku nthawi zosatha.
De a belátók fényleni fognak, mint az égboltozat fénye, s azok, a kik sokakat igazságra visznek, mint a csillagok mind örökké.
4 Koma iweyo, Danieli, sungitsa mawuwa, umate bukuli kufikira nthawi ya chimaliziro. Anthu ambiri adzapita uku ndi uko ndipo nzeru zidzanka zikukulirakulira.”
Te pedig, Dániél, zárd el a szavakat s pecsételjed le a könyvet a vég idejéig: buzgólkodni fognak sokan és gyarapodik a tudás.
5 Kenaka ine Danieli poyangʼana ndinaona anthu ena awiri atayima, wina tsidya lino la mtsinje, wina tsidya linalo.
És láttam én, Dániél, s íme más ketten állnak, az egyik a folyó partján innen, a másik a folyó partján tulnan.
6 Mmodzi mwa awiriwo anafunsa munthu wovala chovala chosalala amene anali mʼmbali mwa madzi a mu mtsinje uja kuti, “Kodi padzapita nthawi yayitali bwanji kuti zodabwitsazi zidzakwaniritsidwe?”
És mondta a lenbe öltözött férfiúnak, a ki a folyó vizein fölül volt: Meddig a csodák vége?
7 Munthu wovala chovala chosalala, amene anali mʼmbali mwa madzi a mu mtsinje uja, anakweza dzanja lake lamanja ndi lamanzere kumwamba, ndipo ndinamumva akulumbira mʼdzina la Wamoyo ku nthawi zonse uja kuti, “Zidzachitika patapita zaka zitatu ndi theka. Zinthu zonsezi zidzachitika akadzatha masautso amene agwera anthu olungama.”
És hallottam a lenbe öltözött férfiút, ki a folyó vizein fölül volt s fölemelte jobbját s balját az ég felé s esküdött az örökké élőre: egy időszak, két időszak s egy félnek multáig; s midőn végkép szétzúzzák a szent nép hatalmát, bevégződnek mindezek.
8 Ndinamva, koma sindinamvetsetse. Choncho ndinafunsa kuti, “Mbuye wanga, nanga matsiriziro a zonsezi adzakhala chiyani?”
Én hallottam ugyan, de nem értettem meg; és mondtam: Uram, mi ezeknek utólja?
9 Ndipo anandiyankha kuti, “Pita iwe Danieli, pakuti mawuwa ndi osungidwa ndi omatidwa kufikira nthawi ya chimaliziro.
Mondta: Menj, Dániél, mert bezárva, lepecsételve vannak a szavak a végnek idejéig.
10 Anthu ambiri adzayeretsedwa nakhala olungama wopanda chodetsa, koma oyipa adzakhala chiyipire. Palibe mmodzi wa anthu oyipa amene adzamvetsetsa koma okhawo amene ali anzeru adzamvetsetsa.
Meg fognak válogattatni s fehérittetni s olvasztatni sokan és gonoszul cselekesznek; mind a gonoszok nem fognak érteni, de a belátók fognak érteni.
11 “Kuyambira pamene nsembe ya tsiku ndi tsiku idzathetsedwa ndi kukhazikitsa kwa chonyansa chobweretsa chisokonezo chija, padzapita masiku 1,290.
És attól az időtől kezdve, hogy elvitetik az állandó áldozat és hogy elhelyezik a pusztitó undokságot ezerkétszázkilenczven nap.
12 Wodala munthu amene adikirabe nadzafika pa mapeto a masiku 1,335.
Boldog az, a ki vár s megéri az ezerháromszázharminczöt napot.
13 “Koma iweyo Danieli, pitiriza ndipo ulimbikire mpaka matsiriziro. Kenaka udzamwalira. Koma mʼmasiku otsiriza udzauka kuti ulandire gawo lako.”
Te pedig menj a vég felé, s nyugodni fogsz és fel fogsz támadni sorsodra a napok végén!

< Danieli 12 >