< Danieli 12 >

1 “Pa nthawi imeneyo Mikayeli, mngelo wamkulu amene amateteza anthu a mtundu wako, adzabwera. Imeneyi idzakhala nthawi ya mavuto aakulu omwe sanaonekepo kuyambira pachiyambi cha mitundu ya anthu mpaka nthawi ikudzayo. Komatu pa nthawiyi anthu a mtundu wako, aliyense amene dzina lake lidzapezeke lolembedwa mʼbuku adzapulumutsidwa.
Mais en ce temps-là s’élèvera Michel le grand prince, qui est pour les fils de ton peuple; et viendra un temps, tel qu’il n’y en a pas eu depuis que les nations ont commencé d’être jusqu’alors. Et en ce temps-là, sera sauvé quiconque de ton peuple sera trouvé écrit dans le livre.
2 Ambiri mwa amene akugona mʼnthaka adzadzuka: ena adzapita ku moyo wosatha, ena ku malo amanyazi ndi chilango chosatha.
Et beaucoup de ceux qui dorment dans la poussière de la terre s’éveilleront: les uns pour la vie éternelle, et les autres pour l’opprobre, afin qu’ils le voient toujours.
3 Amene ali anzeru mʼnjira ya chilungamo adzawala ngati kuwala kwa mlengalenga, ndipo amene alondolera ambiri ku njira yolungama, adzawala ngati nyenyezi ku nthawi zosatha.
Or ceux qui auront été savants brilleront comme la splendeur du firmament, et ceux qui enseignent la justice à un grand nombre, seront comme les étoiles dans les perpétuelles éternités.
4 Koma iweyo, Danieli, sungitsa mawuwa, umate bukuli kufikira nthawi ya chimaliziro. Anthu ambiri adzapita uku ndi uko ndipo nzeru zidzanka zikukulirakulira.”
Mais toi, Daniel, ferme les paroles, et scelle le livre jusqu’au temps déterminé; beaucoup le parcourront et la science sera multipliée.
5 Kenaka ine Danieli poyangʼana ndinaona anthu ena awiri atayima, wina tsidya lino la mtsinje, wina tsidya linalo.
Et je vis, moi Daniel, et voilà comme deux autres hommes qui se tenaient debout: l’un en deçà, sur la rive du fleuve, et l’autre au-delà, sur la rive du fleuve.
6 Mmodzi mwa awiriwo anafunsa munthu wovala chovala chosalala amene anali mʼmbali mwa madzi a mu mtsinje uja kuti, “Kodi padzapita nthawi yayitali bwanji kuti zodabwitsazi zidzakwaniritsidwe?”
Et je dis à l’homme qui était vêtu de lin, qui se tenait sur les eaux du fleuve: Quand sera la fin de ces prodiges?
7 Munthu wovala chovala chosalala, amene anali mʼmbali mwa madzi a mu mtsinje uja, anakweza dzanja lake lamanja ndi lamanzere kumwamba, ndipo ndinamumva akulumbira mʼdzina la Wamoyo ku nthawi zonse uja kuti, “Zidzachitika patapita zaka zitatu ndi theka. Zinthu zonsezi zidzachitika akadzatha masautso amene agwera anthu olungama.”
Et j’entendis l’homme qui était vêtu de lin, qui se tenait debout sur les eaux du fleuve, lorsqu’il eut élevé sa main droite et sa main gauche au ciel, et qu’il eut juré par celui qui vit éternellement, en disant: Dans un temps, et deux temps, et la moitié d’un temps. Et quand la dispersion de l’assemblée du peuple saint sera accomplie, toutes ces choses seront accomplies.
8 Ndinamva, koma sindinamvetsetse. Choncho ndinafunsa kuti, “Mbuye wanga, nanga matsiriziro a zonsezi adzakhala chiyani?”
Et moi j’entendis et ne compris pas. Et je dis: Mon Seigneur, qu’est-ce qui sera après ceci?
9 Ndipo anandiyankha kuti, “Pita iwe Danieli, pakuti mawuwa ndi osungidwa ndi omatidwa kufikira nthawi ya chimaliziro.
Et il dit: Va, Daniel; car les paroles sont fermées et scellées jusqu’au temps fixé.
10 Anthu ambiri adzayeretsedwa nakhala olungama wopanda chodetsa, koma oyipa adzakhala chiyipire. Palibe mmodzi wa anthu oyipa amene adzamvetsetsa koma okhawo amene ali anzeru adzamvetsetsa.
Beaucoup seront purifiés, et deviendront blancs et éprouvés comme le feu, et les impies agiront avec impiété, et aucun des impies ne comprendra; mais les savants comprendront.
11 “Kuyambira pamene nsembe ya tsiku ndi tsiku idzathetsedwa ndi kukhazikitsa kwa chonyansa chobweretsa chisokonezo chija, padzapita masiku 1,290.
Et depuis le temps qu’aura été aboli le sacrifice perpétuel, et qu’aura été établie l’abomination de la désolation, il s’écoulera mille deux cent quatre-vingt-dix jours.
12 Wodala munthu amene adikirabe nadzafika pa mapeto a masiku 1,335.
Bien heureux celui qui attend et qui parvient jusqu’à mille trois cent trente-cinq jours.
13 “Koma iweyo Danieli, pitiriza ndipo ulimbikire mpaka matsiriziro. Kenaka udzamwalira. Koma mʼmasiku otsiriza udzauka kuti ulandire gawo lako.”
Mais toi, va jusqu’au terme fixé, et tu seras en repos, et tu demeureras dans ton état jusqu’à la fin des jours.

< Danieli 12 >