< Danieli 12 >

1 “Pa nthawi imeneyo Mikayeli, mngelo wamkulu amene amateteza anthu a mtundu wako, adzabwera. Imeneyi idzakhala nthawi ya mavuto aakulu omwe sanaonekepo kuyambira pachiyambi cha mitundu ya anthu mpaka nthawi ikudzayo. Komatu pa nthawiyi anthu a mtundu wako, aliyense amene dzina lake lidzapezeke lolembedwa mʼbuku adzapulumutsidwa.
Or, en ce temps-là Michaël, ce grand Chef qui tient ferme pour les enfants de ton peuple, tiendra ferme; et ce sera un temps de détresse, tel qu'il n'y en a point eu depuis qu'il y a eu des nations, jusqu'à ce temps-là; et en ce temps-là ton peuple, [c'est à savoir], quiconque sera trouvé écrit dans le Livre, échappera.
2 Ambiri mwa amene akugona mʼnthaka adzadzuka: ena adzapita ku moyo wosatha, ena ku malo amanyazi ndi chilango chosatha.
Et plusieurs de ceux qui dorment dans la poussière de la terre se réveilleront, les uns pour la vie éternelle, et les autres pour les opprobres et pour l'infamie éternelle.
3 Amene ali anzeru mʼnjira ya chilungamo adzawala ngati kuwala kwa mlengalenga, ndipo amene alondolera ambiri ku njira yolungama, adzawala ngati nyenyezi ku nthawi zosatha.
Et ceux qui auront été intelligents, luiront comme la splendeur de l'étendue; et ceux qui en auront amené plusieurs à la justice [luiront] comme des étoiles, à toujours et à perpétuité.
4 Koma iweyo, Danieli, sungitsa mawuwa, umate bukuli kufikira nthawi ya chimaliziro. Anthu ambiri adzapita uku ndi uko ndipo nzeru zidzanka zikukulirakulira.”
Mais toi, Daniel, ferme ces paroles, et cachette ce Livre jusqu'au temps déterminé, [auquel] plusieurs courront, et la science sera augmentée.
5 Kenaka ine Danieli poyangʼana ndinaona anthu ena awiri atayima, wina tsidya lino la mtsinje, wina tsidya linalo.
Alors moi Daniel je regardai; et voici, deux autres se tenaient debout, l'un en deçà, sur le bord du fleuve, et l'autre au delà, sur le bord du fleuve.
6 Mmodzi mwa awiriwo anafunsa munthu wovala chovala chosalala amene anali mʼmbali mwa madzi a mu mtsinje uja kuti, “Kodi padzapita nthawi yayitali bwanji kuti zodabwitsazi zidzakwaniritsidwe?”
Et on dit à l'homme vêtu de lin qui était au-dessus des eaux du fleuve: Quand est-ce que sera la fin de [ces] merveilles?
7 Munthu wovala chovala chosalala, amene anali mʼmbali mwa madzi a mu mtsinje uja, anakweza dzanja lake lamanja ndi lamanzere kumwamba, ndipo ndinamumva akulumbira mʼdzina la Wamoyo ku nthawi zonse uja kuti, “Zidzachitika patapita zaka zitatu ndi theka. Zinthu zonsezi zidzachitika akadzatha masautso amene agwera anthu olungama.”
Et j'entendis l'homme vêtu de lin, qui était au-dessus des eaux du fleuve, lequel ayant élevé sa main droite et sa main gauche vers les cieux, jura par celui qui vit éternellement, que ce sera jusqu'à un temps, à des temps, et une moitié [de temps]; et quand il aura achevé de disperser la force du peuple saint, toutes ces choses-là seront accomplies.
8 Ndinamva, koma sindinamvetsetse. Choncho ndinafunsa kuti, “Mbuye wanga, nanga matsiriziro a zonsezi adzakhala chiyani?”
Ce que j'ouïs bien, mais je ne l'entendis point; et je dis: Mon Seigneur, quelle sera l'issue de ces choses?
9 Ndipo anandiyankha kuti, “Pita iwe Danieli, pakuti mawuwa ndi osungidwa ndi omatidwa kufikira nthawi ya chimaliziro.
Et il dit: Va, Daniel, car ces paroles sont closes et cachetées jusqu'au temps déterminé.
10 Anthu ambiri adzayeretsedwa nakhala olungama wopanda chodetsa, koma oyipa adzakhala chiyipire. Palibe mmodzi wa anthu oyipa amene adzamvetsetsa koma okhawo amene ali anzeru adzamvetsetsa.
Il y en aura plusieurs qui seront nettoyés et blanchis, et rendus éprouvés; mais les méchants agiront méchamment, et pas un des méchants n'aura de l'intelligence, mais les intelligents comprendront.
11 “Kuyambira pamene nsembe ya tsiku ndi tsiku idzathetsedwa ndi kukhazikitsa kwa chonyansa chobweretsa chisokonezo chija, padzapita masiku 1,290.
Or depuis le temps que le sacrifice continuel aura été ôté, et qu'on aura mis l'abomination de la désolation, il y aura mille deux cent quatre-vingt-dix jours.
12 Wodala munthu amene adikirabe nadzafika pa mapeto a masiku 1,335.
Heureux celui qui attendra, et qui parviendra jusques à mille trois cent trente-cinq jours.
13 “Koma iweyo Danieli, pitiriza ndipo ulimbikire mpaka matsiriziro. Kenaka udzamwalira. Koma mʼmasiku otsiriza udzauka kuti ulandire gawo lako.”
Mais toi, va à [ta] fin; néanmoins tu te reposeras, et demeureras dans ton état jusqu'à la fin de [tes] jours.

< Danieli 12 >