< Danieli 11 >
1 Ndipo chaka choyamba cha Dariyo Mmedi ine Mikayeli ndinabwera kumuthandiza ndi kumuteteza Gabrieli.
Ja tedy roku pierwszego za Daryjusza Medskiego stanąłem, abym go posilił i zmocnił.
2 “Ndipo tsopano ndikuwuza zoona: Mafumu ena atatu adzalamulira ku Peresiya, ndipo kenaka padzadzuka mfumu yachinayi imene idzakhala yolemera kwambiri kuposa onsewo. Popeza kuti idzakhala ndi mphamvu chifukwa cha chuma chake, idzadzutsa onse kuti alimbane ndi ufumu wa Grisi.
A teraz ci prawdę oznajmię: Oto jeszcze trzej królowie królować będą w Perskiej ziemi; potem czwarty zbogaci się bogactwy wielkimi nade wszystkich, a gdy się zmocni w bogactwach swoich, pobudzi wszystkich przeciw królestwu Greckiemu.
3 Kenaka mfumu yamphamvu idzafika imene idzalamulira ndi ufumu waukulu ndi kuchita zimene ifuna.
I powstanie król mocny, a będzie panował mocą wielką, a będzie czynił według woli swojej.
4 Koma ufumu wake ukadzafika pachimake, udzawonongedwa ndi kugawidwa mʼzigawo zinayi. Ufumuwo sudzaperekedwa kwa zidzukulu zake, ndipo olowa mʼmalo mwake sadzakhala ndi mphamvu monga anali nazo, chifukwa ufumu wake udzazulidwa ndi kuperekedwa kwa ena.
A gdy się on zmocni, będzie skruszone królestwo jego, i będzie rozdzielone na cztery strony świata, wszakże nie między potomków jego, ani będzie państwo jego takie, jakie było; bo wykorzenione będzie królestwo jego, a innym mimo onych dostanie się.
5 “Mfumu ya kummwera idzakhala yamphamvu, koma mmodzi mwa akalonga ake adzakhala ndi mphamvu kuposa iyo; adzalamulira ufumu wake waukulu kwambiri.
Tedy się zmocni król z południa i jeden z książąt jego; ten mocniejszy będzie nadeń, i panować będzie, a państwo jego będzie państwo szerokie.
6 Patapita zaka zingapo, mfumu ya kummwera ndi mfumu ya kumpoto adzachita pangano. Mwana wamkazi wa mfumu ya kummwera adzapita nakakwatiwa ndi mfumu ya kumpoto pokhazikitsa pangano la mtendere, koma ulamuliro wake pamodzi ndi wa mwana wake sudzakhalitsa. Mʼmasiku amenewo iye, mwamuna wake, mwana wake ndi atumiki ake, onse adzaperekedwa kwa adani.
Lecz po wyjściu kilku lat złączą się; bo córka króla od południa pójdzie za króla północnego, aby uczyniła przymierze; wszakże nie otrzyma siły ramienia, ani się ostoi z ramieniem swojem, ale wydana będzie ona, i ci, którzy ją przyprowadzą, i syn jej, i ten, co ją zmacniał za onych czasów.
7 “Mmodzi wochokera ku banja la mkaziyo adzadzuka nadzalamulira mʼmalo mwake. Iye adzamenyana ndi ankhondo a mfumu ya kumpoto ndi kulowa mʼmalo ake otetezedwa; adzachita nawo nkhondo ndi kupambana.
Potem powstanie z latorośli korzenia jej na miejsce jego, który przyciągnie z wojskiem swem, a uderzy na miejsce obronne króla północnego, i przewiedzie nad nimi i zmocni się.
8 Iye adzalandanso milungu yawo, mafano awo achitsulo, ndi ziwiya zawo zamtengowapatali zasiliva ndi golide ndi kubwerera nazo ku Igupto. Adzaleka osayithira nkhondo mfumu ya kumpoto kwa zaka zingapo.
Nadto i bogów ich z książętami ich, z naczyniem ich drogiem, srebrnem i złotem w niewolę zawiedzie do Egiptu; a ten będzie bezpieczen przez wiele lat od króla północnego.
9 Kenaka mfumu ya kumpoto idzathira nkhondo dziko la mfumu ya kummwera koma idzalephera ndi kubwerera kwawo.
A tak wtargnie w królestwo król od południa, i wróci się do ziemi swojej.
10 Ana ake adzakonzekera nkhondo ndi kusonkhanitsa gulu lankhondo lalikulu, limene lidzathira nkhondo mfumu yakummwera ngati chigumula mpaka kumalo ake otetezedwa.
Ale synowie jego walczyć będą, i zbiorą mnóstwo wojsk wielkich; a z nagła następując jako powódź przechodzić będzie, potem wracając się, wojskiem nacierać będzie aż na twierdze jego.
11 “Kenaka mfumu yakummwera idzatuluka mokwiya ndi kumenya nkhondo ndi mfumu yakumpoto, imene idzasonkhanitsa gulu lalikulu la nkhondo, koma idzayigonjetsa.
Skąd rozdrażniony będąc król z południa wyciągnie, i będzie walczył z nim, to jest, z królem północnym; a uszykuje mnóstwo wielkie, ale ono mnóstwo będzie podane w rękę jego.
12 Gulu la nkhondoli likadzagwidwa, mfumu yakummwera idzayamba kudzikuza ndipo idzapha anthu miyandamiyanda, koma kupambanaku sikudzapitirira.
A gdy zniesione będzie ono mnóstwo, podniesie się serce jego; a choć porazi wiele tysięcy, przecie się nie zmocni.
13 Popeza mfumu ya kumpoto idzasonkhanitsa gulu lina lankhondo, lochulukirapo kuposa loyamba; ndipo patapita zaka zingapo idzabwera ndi chigulu chachikulu cha nkhondo chokonzekeratu ndi zida.
Bo się wróci król północny, i uszykuje większe mnóstwo niż pierwsze; lecz po wyjściu czasu kilku lat z nagła przyjdzie z wielkiem wojskiem i z wielkim dostatkiem.
14 “Nthawi imeneyo ambiri adzawukira mfumu ya kummwera. Anthu achisokonezo pakati panu nawonso adzawukira pokwaniritsa masomphenya, koma sadzapambana.
Onychże czasów wiele ich powstanie przeciwko królowi z południa; ale synowie przestępników z ludu twego będą zniesieni dla utwierdzenia tego widzenia, i upadną.
15 Kenaka mfumu ya kumpoto idzafika ndikuzinga mzinda powunda nthumbira za nkhondo ndipo idzagonjetsa mzinda wotetezedwa. Gulu lankhondo la kummwera lidzasowa mphamvu; ngakhale akatswiri awo ankhondo sadzakhala ndi mphamvu zogonjetsera ankhondo a kumpoto.
Bo przyciągnie król z północy, i usypie wały, i weźmie miasto obronne, a ramiona południowe nie oprą się, ani lud jego wybrany, i nie stanie im siły, aby dali odpór.
16 Mfumu ya kumpoto idzachita zofuna zake; palibe aliyense adzayigonjetse. Idzakhazikitsa ulamuliro wake mu Dziko Lokongola. Zonse zidzakhala mu ulamuliro wa mfumu yakumpoto ija.
I uczyni on, który przyciągnie przeciwko niemu, według woli swojej, i nie będzie nikogo, coby się stawił przeciwko niemu; stawi się też w ziemi ozdobnej, która zniszczeje przez rękę jego.
17 Idzafika ndi mphamvu za ufumu wake wonse ndipo idzayesa kuchita pangano la mtendere ndi mfumu ya kummwera. Ndipo idzamupatsa mwana wake wamkazi kuti amukwatire ndi cholinga cholanda ufumu, koma zolinga zake sizidzatheka kapena kumuthandiza.
Potem obróci twarz swoję, aby przyszedł z mocą wszystkiego królestwa swego, i okazał się, jakoby zgody szukał, i uczyni coś; bo mu da córkę piękną, aby go zgubił przez nią; ale ona w tem nie będzie stateczna, i nie będzie z nim przestawała.
18 Kenaka idzatembenukira ku mayiko a mʼmbali mwa nyanja ndi kulanda mizinda yambiri, koma mtsogoleri wina wa nkhondo adzathetsa kudzikuza kwakeko ndipo adzabwezera chipongwecho kwa iye.
Zatem obróci twarz swoję do wysep, i wiele ich pobierze; ale wódz wstręt uczyni hańbieniu jego, owszem, ono hańbienie jego nań obróci.
19 Zikadzatha izi, mfumu idzabwerera ku malo otetezedwa a dziko la kwawo koma idzapunthwa ndi kugwa osapezekanso.
Dlaczego obróci twarz swoję ku twierdzom ziemi swej; lecz się potknie i upadnie, i nie będzie więcej znaleziony.
20 “Mfumu imene idzatenga malo ake idzatumiza wokhometsa msonkho kuti chuma cha ufumu wake chichuluke. Komabe mʼzaka zochepa mfumuyo idzawonongedwa osati mu mkwiyo kapena ku nkhondo.
I powstanie na miejsce jego taki, który roześle poborców w sławie królewskiej; ale ten po niewielu dniach starty będzie, a to nie w gniewie ani przez wojnę.
21 “Mʼmalo mwake mudzalowa munthu wonyozeka amene si wa banja laufumu. Iye adzabwera pamene anthu akuganiza kuti ali pa mtendere, ndipo adzalanda ufumuwo mwa chinyengo.
Potem powstanie wzgardzony na jego miejsce, acz nie włożą nań ozdoby królewskiej; wszakże przyszedłszy w pokoju, otrzyma królestwo pochlebstwem.
22 Kenaka adzagonetsa gulu lalikulu lankhondo kuphatikizapo Mkulu wa Ansembe wapangano.
A ramionami jako powodzią wiele ich zachwyceni będą przed obliczem jego, i skruszeni będą, także też i sam wódz, który z nimi przymierze uczynił.
23 Atatha kuchita naye pangano, iye adzachita monyenga, ndipo ngakhale adzakhale ndi anthu ochepa adzakhalabe ndi mphamvu.
Bo wszedłszy z nimi w przyjaźń, uczyni zdradę, a przyciągnąwszy zmocni się w małym poczcie ludu.
24 Mwadzidzidzi, iye adzazithira nkhondo zigawo zolemera kwambiri ndipo adzachita zimene makolo ake ngakhale agogo ake sanachitepo. Iye adzagawira zolanda, zofunkha ndi chuma kwa omutsatira. Adzachita chiwembu cholanda mizinda yotetezedwa koma kwa kanthawi kochepa.
Bezpiecznie i do najobfitszych miejsc onej krainy wpadnie, a uczyni to, czego nie czynili ojcowie jego, ani ojcowie ojców jego; łup i korzyść i majętności rozdzieli im, nawet i o miejscach obronnych chytrze przemyśliwać będzie, a to aż do czasu.
25 “Mfumu ya kumpoto idzalimba mtima, ndipo idzasonkhanitsa gulu lalikulu la ankhondo kuti lithire nkhondo mfumu yakummwera. Mfumu yakummwera ndi gulu lake lankhondo lalikulu ndi lamphamvu idzathirana nkhondo ndi mfumu yakumpoto koma sidzapambana chifukwa cha ziwembu zimene adzamukonzera.
Potem wzbudzi moc swoję, i serce swoje przeciw królowi z południa z wojskiem wielkiem, z którem król z południa walecznie się potykać będzie z wojskiem wielkiem i bardzo mocnem; ale się nie oprze, przeto, że wymyśli przeciwko niemu zdradę.
26 Amene amadya chakudya ndi mfumu adzamuukira; gulu lake lankhondo lidzagonjetsedwa, ndipo ambiri adzafera ku nkhondo.
Bo ci, którzy jedzą chleb jego, zniszczą go, gdy wojsko onego jako powódź przypadnie, a pobitych wiele polęże.
27 Mafumu awiriwa mitima yawo idzalinga ku zoyipa. Azidzanamizana ali pa tebulo limodzi, koma zolinga zawo sizidzatheka chifukwa nthawi idzakhala isanakwane.
Natenczas obaj królowie w sercu swem myślić będą, jakoby jeden drugiemu szkodzić mógł, a przy jednymże stole kłamstwo mówić będą; ale się im nie nada, gdyż jeszcze koniec na inszy czas odłożony jest.
28 Mfumu ya kumpoto idzabwerera ku dziko la kwawo ndi chuma chambiri, koma mtima wake udzafunitsitsa pangano lopatulika. Idzawononga panganolo ndipo kenaka idzabwerera ku dziko lake.
Przetoż się wróci do ziemi swojej z bogactwy wielkiemi, a serce jego obróci się przeciwko przymierzu świętemu; co uczyniwszy wróci się do ziemi swojej.
29 “Patapita nthawi mfumu ya kumpoto idzabwereranso kummwera koma sidzapambana monga inachitira kale.
A czasu zamierzonego wróci się i pociągnie na południe; ale mu się nie tak powiedzie, jako za pierwszym i za ostatnim razem.
30 Sitima zapamadzi zochokera ku mayiko a ku madzulo zidzalimbana naye, ndipo adzataya mtima. Kenaka idzabwerera mopsa mtima ndi kudzalimbana ndi chipembedzo cha anthu opatulika. Idzabwerera ndi kuchitira chifundo amene sadzasunga pangano loyera.
Bo przyjdą przeciwko niemu okręty z Cytym, skąd on nad tem bolejąc znowu się rozgniewa przeciwko przymierzu świętemu; co uczyniwszy wróci się, a będzie miał porozumienie z onymi, którzy opuścili przymierze święte;
31 “Ankhondo ake adzayipitsa linga la Nyumba ya Mulungu ndipo adzathetsa nsembe za tsiku ndi tsiku. Kenaka adzakhazikitsa chonyansa chimene chabweretsa chiwonongeko.
A wojska wielkie przy nim stać będą, które splugawią świątnicę, i twierdze zniosą; odejmą też ustawiczną ofiarę, a postawią obrzydliwość spustoszenia.
32 Ndi mawu oshashalika mfumuyo idzakopa amene anaphwanya pangano, koma anthu amene amadziwa Mulungu wawo adzalimbika ndipo adzayikana mfumuyo kwathunthu.
Tak aby tych, którzy niezbożnie przeciwko przymierzu postępować będą, w obłudzie pochlebstwem utwierdził, a żeby lud znający Boga swego imali, co też uczynią.
33 “Amene ndi anzeru adzalangiza ambiri. Koma patapita kanthawi adzaphedwa ndi lupanga kapena kutenthedwa, kapena kugwidwa kapena kulandidwa katundu.
Zaczem ci, którzy nauczają lud, którzy nauczają wielu, padać będą od miecza i od ognia, od pojmania i od łupu przez wiele dni.
34 Pa nthawi yozunzikayi ena adzawathandiza pangʼono, koma ambiri othandizawo adzakhala achinyengo.
A gdy padać będą, małą pomoc mieć będą; bo się do nich wiele pochlebców przyłączy.
35 Ena mwa anzeruwo adzaphedwa ndi cholinga chakuti ayengedwe, otsala mwa iwo ayeretsedwe ndi kukhala wopanda banga kufikira nthawi yomaliza, popeza idzafika ndithu nthawi imene Mulungu wayika.
A z tych, którzy innych nauczają, padać będą, aby doświadczeni i oczyszczeni, i wybieleni byli aż do czasu zamierzonego; bo to jeszcze potrwa aż do czasu zamierzonego.
36 “Mfumu ya kumpoto idzachita zimene ikufuna. Idzadzikweza ndi kudziyesa yopambana mulungu aliyense ndipo idzanenera za mwano Mulungu wa milungu. Iyo idzapambana mpaka nthawi yoti Mulungu ayilange mwa mkwiyo itakwana popeza chimene chatsimikizika chiyenera kuchitika.
Tak uczyni król według woli swojej, i podniesie się i wielmożnym się uczyni nad każdego boga, i przeciwko Bogu nad bogami dziwne rzeczy mówić będzie, i poszczęści mu się, aż się dokona gniew, ażby się to, co jest postanowiono, wykonało.
37 Mfumuyo idzanyoza milungu ya makolo ake ndiponso mulungu wokondedwa ndi akazi, sidzachitiranso ulemu mulungu aliyense, koma idzadzikweza yokha pamwamba pa onse.
Ani na bogów ojców swych nie będzie dbał, ani o miłość niewiast, ani o żadnego boga dbać będzie, przeto, że się nade wszystko wyniesie.
38 Mʼmalo mwa onsewo, idzachitira ulemu mulungu wachitetezo; mulungu wosadziwika ndi makolo ake. Iyo idzapereka kwa mulunguyo golide ndi siliva, ndi miyala yokongola, ndiponso mphatso za pamwamba kwambiri.
A na miejscu Boga najmocniejszego czcić będzie boga, którego nie znali ojcowie jego; czcić będzie złotem i srebrem i kamieniem drogiem i rzeczami kosztownemi.
39 Anthu opembedza mulungu wachilendo adzakhala ngati linga lake. Idzalemekeza iwowa kwambiri, ndipo idzawayika kuti alamulire anthu ambiri. Idzawagawira dziko ngati malipiro awo.
A tak dowiedzie tego, że twierdze Najmocniejszego będą boga obcego; a których mu się będzie zdało, tych rozmnoży sławę, i uczyni, aby panowali nad wielą, a rozdzieli im ziemię miasto zapłaty.
40 “Pa nthawi yomaliza mfumu yakummwera idzachita nkhondo ndi mfumu yakumpoto. Koma mfumu yakumpotoyi idzayikantha ndi magaleta ndi akavalo ndi sitima zapamadzi zambiri ngati mphepo yamkokomo. Idzalowa mʼmayiko ambiri ndikuwakokolola onse ngati madzi osefukira.
A przy skończeniu tego czasu będzie się z nim potykał król z południa; ale król północny jako burza nań przyjdzie z wozami i z jezdnymi i z wielą okrętów, a wtargnie w ziemię, i jako powódź przejdzie.
41 Idzalowanso mʼDziko Lokongola ndipo anthu ambiri adzaphedwa. Koma Edomu, Mowabu ndi olamulira a Amoni adzapulumuka.
Potem przyciągnie do ziemi ozdobnej, i wiele krain upadnie; wszakże ci ujdą rąk jego, Edomczycy i Moabczycy, i pierwociny synów Ammonowych.
42 Idzathira nkhondo mayiko ambiri ndipo ngakhale Igupto sadzapulumuka.
A gdy rękę swą ściągnie na krainy, ani ziemia Egipska tego ujść nie będzie mogła.
43 Idzalanda chuma cha golide, siliva, ndi zonse za mtengowapatali za ku Igupto, ndiponso anthu a ku Libiya ndi Akusi adzagonja kwa iwo.
Bo opanuje skarby złota i srebra, i wszystkie rzeczy drogie Egipskie, a Libijczycy i Murzynowie za nim pójdą.
44 Koma uthenga wochokera kummawa ndi kumpoto udzayiopsa, ndipo idzapita ndi ukali kukawononga ndi kutheratu anthu ambiri.
W tem wieści od wschodu słońca i od północy przestraszą go; przetoż wyciągnie z popędliwością wielką, aby wygubił i zamordował wielu.
45 Mfumuyo idzayimika matenti ake aufumu, pakati pa nyanja ndi phiri lokongola. Komabe mapeto ake mfumuyo idzaphedwa, ndipo palibe amene adzayithandize.”
I rozbije namioty pałacu swego między morzami na górze ozdobnej świętobliwości; a gdy przyjdzie do końca swego, nie będzie miał nikogo na pomocy.