< Danieli 11 >

1 Ndipo chaka choyamba cha Dariyo Mmedi ine Mikayeli ndinabwera kumuthandiza ndi kumuteteza Gabrieli.
ایستاده بودم تا او را استوار سازم وقوت دهم.۱
2 “Ndipo tsopano ndikuwuza zoona: Mafumu ena atatu adzalamulira ku Peresiya, ndipo kenaka padzadzuka mfumu yachinayi imene idzakhala yolemera kwambiri kuposa onsewo. Popeza kuti idzakhala ndi mphamvu chifukwa cha chuma chake, idzadzutsa onse kuti alimbane ndi ufumu wa Grisi.
«و الان تو را به راستی اعلام می‌نمایم. اینک سه پادشاه بعد از این در فارس خواهند برخاست و چهارمین از همه دولتمندتر خواهد بود و چون به‌سبب توانگری خویش قوی گردد همه را به ضد مملکت یونان برخواهد انگیخت.۲
3 Kenaka mfumu yamphamvu idzafika imene idzalamulira ndi ufumu waukulu ndi kuchita zimene ifuna.
وپادشاهی جبار خواهد برخاست و بر مملکت عظیمی سلطنت خواهد نمود و برحسب اراده خود عمل خواهد کرد.۳
4 Koma ufumu wake ukadzafika pachimake, udzawonongedwa ndi kugawidwa mʼzigawo zinayi. Ufumuwo sudzaperekedwa kwa zidzukulu zake, ndipo olowa mʼmalo mwake sadzakhala ndi mphamvu monga anali nazo, chifukwa ufumu wake udzazulidwa ndi kuperekedwa kwa ena.
و چون برخیزد سلطنت او شکسته خواهد شد و بسوی بادهای اربعه آسمان تقسیم خواهد گردید. اما نه به ذریت او ونه موافق استقلالی که او می‌داشت، زیرا که سلطنت او از ریشه‌کنده شده و به دیگران غیر ازایشان داده خواهد شد.۴
5 “Mfumu ya kummwera idzakhala yamphamvu, koma mmodzi mwa akalonga ake adzakhala ndi mphamvu kuposa iyo; adzalamulira ufumu wake waukulu kwambiri.
و پادشاه جنوب با یکی از سرداران خود قوی شده، بر او غلبه خواهدیافت و سلطنت خواهد نمود و سلطنت اوسلطنت عظیمی خواهد بود.۵
6 Patapita zaka zingapo, mfumu ya kummwera ndi mfumu ya kumpoto adzachita pangano. Mwana wamkazi wa mfumu ya kummwera adzapita nakakwatiwa ndi mfumu ya kumpoto pokhazikitsa pangano la mtendere, koma ulamuliro wake pamodzi ndi wa mwana wake sudzakhalitsa. Mʼmasiku amenewo iye, mwamuna wake, mwana wake ndi atumiki ake, onse adzaperekedwa kwa adani.
و بعد از انقضای سالها ایشان همداستان خواهند شد و دختر پادشاه جنوب نزد پادشاه شمال آمده، با اومصالحه خواهد نمود. لیکن قوت بازوی خود رانگاه نخواهد داشت و او و بازویش برقرار نخواهدماند و آن دختر و آنانی که او را خواهند‌آورد وپدرش و آنکه او را تقویت خواهد نمود در آن زمان تسلیم خواهند شد.۶
7 “Mmodzi wochokera ku banja la mkaziyo adzadzuka nadzalamulira mʼmalo mwake. Iye adzamenyana ndi ankhondo a mfumu ya kumpoto ndi kulowa mʼmalo ake otetezedwa; adzachita nawo nkhondo ndi kupambana.
«و کسی از رمونه های ریشه هایش در جای او خواهد برخاست و با لشکری آمده، به قلعه پادشاه شمال داخل خواهد شد و با ایشان (جنگ ) نموده، غلبه خواهد یافت.۷
8 Iye adzalandanso milungu yawo, mafano awo achitsulo, ndi ziwiya zawo zamtengowapatali zasiliva ndi golide ndi kubwerera nazo ku Igupto. Adzaleka osayithira nkhondo mfumu ya kumpoto kwa zaka zingapo.
و خدایان وبتهای ریخته شده ایشان را نیز با ظروف گرانبهای ایشان از طلا و نقره به مصر به اسیری خواهد برد وسالهایی چند از پادشاه شمال دست خواهدبرداشت.۸
9 Kenaka mfumu ya kumpoto idzathira nkhondo dziko la mfumu ya kummwera koma idzalephera ndi kubwerera kwawo.
و به مملکت پادشاه جنوب داخل شده، باز به ولایت خود مراجعت خواهد نمود.۹
10 Ana ake adzakonzekera nkhondo ndi kusonkhanitsa gulu lankhondo lalikulu, limene lidzathira nkhondo mfumu yakummwera ngati chigumula mpaka kumalo ake otetezedwa.
و پسرانش محاربه خواهند نمود و گروهی ازلشکرهای عظیم را جمع خواهند کرد و ایشان داخل شده، مثل سیل خواهند آمد و عبورخواهند نمود و برگشته، تا به قلعه او جنگ خواهند کرد.۱۰
11 “Kenaka mfumu yakummwera idzatuluka mokwiya ndi kumenya nkhondo ndi mfumu yakumpoto, imene idzasonkhanitsa gulu lalikulu la nkhondo, koma idzayigonjetsa.
و پادشاه جنوب خشمناک شده، بیرون خواهد آمد و با وی یعنی با پادشاه شمال جنگ خواهد نمود و وی گروه عظیمی برپاخواهد کرد و آن گروه به‌دست وی تسلیم خواهند شد.۱۱
12 Gulu la nkhondoli likadzagwidwa, mfumu yakummwera idzayamba kudzikuza ndipo idzapha anthu miyandamiyanda, koma kupambanaku sikudzapitirira.
و چون آن گروه برداشته شود، دلش مغرور خواهد شد و کرورها را هلاک خواهد ساخت اما قوت نخواهد یافت.۱۲
13 Popeza mfumu ya kumpoto idzasonkhanitsa gulu lina lankhondo, lochulukirapo kuposa loyamba; ndipo patapita zaka zingapo idzabwera ndi chigulu chachikulu cha nkhondo chokonzekeratu ndi zida.
پس پادشاه شمال مراجعت کرده، لشکری عظیم تر ازاول برپا خواهد نمود و بعد از انقضای مدت سالهابا لشکر عظیمی و دولت فراوانی خواهد آمد.۱۳
14 “Nthawi imeneyo ambiri adzawukira mfumu ya kummwera. Anthu achisokonezo pakati panu nawonso adzawukira pokwaniritsa masomphenya, koma sadzapambana.
و در آنوقت بسیاری با پادشاه جنوب مقاومت خواهند نمود و بعضی از ستمکیشان قوم توخویشتن را خواهند برافراشت تا رویا را ثابت نمایند اما ایشان خواهند افتاد.۱۴
15 Kenaka mfumu ya kumpoto idzafika ndikuzinga mzinda powunda nthumbira za nkhondo ndipo idzagonjetsa mzinda wotetezedwa. Gulu lankhondo la kummwera lidzasowa mphamvu; ngakhale akatswiri awo ankhondo sadzakhala ndi mphamvu zogonjetsera ankhondo a kumpoto.
«پس پادشاه شمال خواهد آمد و سنگرهابرپا نموده، شهر حصاردار را خواهد گرفت و نه افواج جنوب و نه برگزیدگان او یارای مقاومت خواهند داشت بلکه وی را هیچ یارای مقاومت نخواهد بود.۱۵
16 Mfumu ya kumpoto idzachita zofuna zake; palibe aliyense adzayigonjetse. Idzakhazikitsa ulamuliro wake mu Dziko Lokongola. Zonse zidzakhala mu ulamuliro wa mfumu yakumpoto ija.
و آنکس که به ضد وی می‌آیدبرحسب رضامندی خود عمل خواهد نمود وکسی نخواهد بود که با وی مقاومت تواند نمودپس در فخر زمینها توقف خواهد نمود و آن به‌دست وی تلف خواهد شد.۱۶
17 Idzafika ndi mphamvu za ufumu wake wonse ndipo idzayesa kuchita pangano la mtendere ndi mfumu ya kummwera. Ndipo idzamupatsa mwana wake wamkazi kuti amukwatire ndi cholinga cholanda ufumu, koma zolinga zake sizidzatheka kapena kumuthandiza.
و عزیمت خواهدنمود که با قوت تمامی مملکت خویش داخل بشود و با وی مصالحه خواهد کرد و او دختر زنان را به وی خواهد داد تا آن را هلاک کند. اما او ثابت نخواهد ماند و از آن او نخواهد بود.۱۷
18 Kenaka idzatembenukira ku mayiko a mʼmbali mwa nyanja ndi kulanda mizinda yambiri, koma mtsogoleri wina wa nkhondo adzathetsa kudzikuza kwakeko ndipo adzabwezera chipongwecho kwa iye.
پس بسوی جزیره‌ها توجه خواهد نمود و بسیاری ازآنها را خواهد گرفت. لیکن سرداری سرزنش او راباطل خواهد کرد، بلکه انتقام سرزنش او را از اوخواهد گرفت.۱۸
19 Zikadzatha izi, mfumu idzabwerera ku malo otetezedwa a dziko la kwawo koma idzapunthwa ndi kugwa osapezekanso.
پس بسوی قلعه های زمین خویش توجه خواهد نمود اما لغزش خواهدخورد و افتاده، ناپدید خواهد شد.۱۹
20 “Mfumu imene idzatenga malo ake idzatumiza wokhometsa msonkho kuti chuma cha ufumu wake chichuluke. Komabe mʼzaka zochepa mfumuyo idzawonongedwa osati mu mkwiyo kapena ku nkhondo.
«پس در جای او عاملی خواهد برخاست که جلال سلطنت را از میان خواهد برداشت لیکن در اندک ایامی او نیز هلاک خواهد شد نه به غضب و نه به جنگ.۲۰
21 “Mʼmalo mwake mudzalowa munthu wonyozeka amene si wa banja laufumu. Iye adzabwera pamene anthu akuganiza kuti ali pa mtendere, ndipo adzalanda ufumuwo mwa chinyengo.
و در جای او حقیری خواهدبرخاست اما جلال سلطنت را به وی نخواهند دادو او ناگهان داخل شده، سلطنت را با حیله هاخواهد گرفت.۲۱
22 Kenaka adzagonetsa gulu lalikulu lankhondo kuphatikizapo Mkulu wa Ansembe wapangano.
و سیل افواج و رئیس عهد نیزاز حضور او رفته و شکسته خواهند شد.۲۲
23 Atatha kuchita naye pangano, iye adzachita monyenga, ndipo ngakhale adzakhale ndi anthu ochepa adzakhalabe ndi mphamvu.
و ازوقتی که ایشان با وی همداستان شده باشند او به حیله رفتار خواهد کرد و با جمعی قلیل افراشته وبزرگ خواهد شد.۲۳
24 Mwadzidzidzi, iye adzazithira nkhondo zigawo zolemera kwambiri ndipo adzachita zimene makolo ake ngakhale agogo ake sanachitepo. Iye adzagawira zolanda, zofunkha ndi chuma kwa omutsatira. Adzachita chiwembu cholanda mizinda yotetezedwa koma kwa kanthawi kochepa.
و ناگهان به برومندترین بلادوارد شده، کارهایی را که نه پدرانش و نه پدران پدرانش کرده باشند بجا خواهد آورد و غارت وغنیمت و اموال را به ایشان بذل خواهد نمود و به ضد شهرهای حصاردار تدبیرها خواهد نمود، لیکن اندک زمانی خواهد بود.۲۴
25 “Mfumu ya kumpoto idzalimba mtima, ndipo idzasonkhanitsa gulu lalikulu la ankhondo kuti lithire nkhondo mfumu yakummwera. Mfumu yakummwera ndi gulu lake lankhondo lalikulu ndi lamphamvu idzathirana nkhondo ndi mfumu yakumpoto koma sidzapambana chifukwa cha ziwembu zimene adzamukonzera.
و قوت و دل خود را با لشکر عظیمی به ضد پادشاه جنوب برخواهد انگیخت و پادشاه جنوب با فوجی بسیار عظیم و قوی تهیه جنگ خواهد دید امایارای مقاومت نخواهد داشت زیرا که به ضد اوتدبیرها خواهند نمود.۲۵
26 Amene amadya chakudya ndi mfumu adzamuukira; gulu lake lankhondo lidzagonjetsedwa, ndipo ambiri adzafera ku nkhondo.
و آنانی که خوراک او رامی خورند او را شکست خواهند داد و لشکر اوتلف خواهد شد و بسیاری کشته خواهند افتاد.۲۶
27 Mafumu awiriwa mitima yawo idzalinga ku zoyipa. Azidzanamizana ali pa tebulo limodzi, koma zolinga zawo sizidzatheka chifukwa nthawi idzakhala isanakwane.
و دل این دو پادشاه به بدی مایل خواهد شد وبر یک سفره دروغ خواهند گفت، اما پیش نخواهد رفت زیرا که هنوز انتها برای وقت معین خواهد بود.۲۷
28 Mfumu ya kumpoto idzabwerera ku dziko la kwawo ndi chuma chambiri, koma mtima wake udzafunitsitsa pangano lopatulika. Idzawononga panganolo ndipo kenaka idzabwerera ku dziko lake.
پس با اموال بسیار به زمین خودمراجعت خواهد کرد ودلش به ضد عهد مقدس جازم خواهد بود پس (برحسب اراده خود) عمل نموده، به زمین خود خواهد برگشت.۲۸
29 “Patapita nthawi mfumu ya kumpoto idzabwereranso kummwera koma sidzapambana monga inachitira kale.
و دروقت معین مراجعت نموده، به زمین جنوب واردخواهد شد لیکن آخرش مثل اولش نخواهد بود.۲۹
30 Sitima zapamadzi zochokera ku mayiko a ku madzulo zidzalimbana naye, ndipo adzataya mtima. Kenaka idzabwerera mopsa mtima ndi kudzalimbana ndi chipembedzo cha anthu opatulika. Idzabwerera ndi kuchitira chifundo amene sadzasunga pangano loyera.
و کشتیها از کتیم به ضد او خواهند آمد لهذامایوس شده، رو خواهد تافت و به ضد عهدمقدس خشمناک شده، (برحسب اراده خود)عمل خواهد نمود و برگشته به آنانی که عهدمقدس را ترک می‌کنند توجه خواهد نمود.۳۰
31 “Ankhondo ake adzayipitsa linga la Nyumba ya Mulungu ndipo adzathetsa nsembe za tsiku ndi tsiku. Kenaka adzakhazikitsa chonyansa chimene chabweretsa chiwonongeko.
وافواج از جانب او برخاسته، مقدس حصین رانجس خواهند نمود و قربانی سوختنی دایمی راموقوف کرده، رجاست ویرانی را برپا خواهندداشت.۳۱
32 Ndi mawu oshashalika mfumuyo idzakopa amene anaphwanya pangano, koma anthu amene amadziwa Mulungu wawo adzalimbika ndipo adzayikana mfumuyo kwathunthu.
و آنانی را که به ضد عهد شرارت می‌ورزند با مکرها گمراه خواهد کرد. اما آنانی که خدای خویش را می‌شناسند قوی شده، (کارهای عظیم ) خواهند کرد.۳۲
33 “Amene ndi anzeru adzalangiza ambiri. Koma patapita kanthawi adzaphedwa ndi lupanga kapena kutenthedwa, kapena kugwidwa kapena kulandidwa katundu.
و حکیمان قوم بسیاری را تعلیم خواهند داد، لیکن ایامی چند به شمشیر و آتش و اسیری و تاراج خواهند افتاد.۳۳
34 Pa nthawi yozunzikayi ena adzawathandiza pangʼono, koma ambiri othandizawo adzakhala achinyengo.
و چون بیفتند نصرت کمی خواهند یافت وبسیاری با فریب به ایشان ملحق خواهند شد.۳۴
35 Ena mwa anzeruwo adzaphedwa ndi cholinga chakuti ayengedwe, otsala mwa iwo ayeretsedwe ndi kukhala wopanda banga kufikira nthawi yomaliza, popeza idzafika ndithu nthawi imene Mulungu wayika.
وبعضی از حکیمان به جهت امتحان ایشان لغزش خواهند خورد که تا وقت آخر طاهر و سفیدبشوند زیرا که زمان معین هنوز نیست.۳۵
36 “Mfumu ya kumpoto idzachita zimene ikufuna. Idzadzikweza ndi kudziyesa yopambana mulungu aliyense ndipo idzanenera za mwano Mulungu wa milungu. Iyo idzapambana mpaka nthawi yoti Mulungu ayilange mwa mkwiyo itakwana popeza chimene chatsimikizika chiyenera kuchitika.
«و آن پادشاه موافق اراده خود عمل نموده، خویشتن را بر همه خدایان افراشته و بزرگ خواهد نمود و به ضد خدای خدایان سخنان عجیب خواهد گفت و تا انتهای غضب کامیاب خواهد شد زیرا آنچه مقدر است به وقوع خواهدپیوست.۳۶
37 Mfumuyo idzanyoza milungu ya makolo ake ndiponso mulungu wokondedwa ndi akazi, sidzachitiranso ulemu mulungu aliyense, koma idzadzikweza yokha pamwamba pa onse.
و به خدای پدران خود و به فضیلت زنان اعتنا نخواهد نمود، بلکه بهیچ خدا اعتنانخواهد نمود زیرا خویشتن را از همه بلندترخواهد شمرد.۳۷
38 Mʼmalo mwa onsewo, idzachitira ulemu mulungu wachitetezo; mulungu wosadziwika ndi makolo ake. Iyo idzapereka kwa mulunguyo golide ndi siliva, ndi miyala yokongola, ndiponso mphatso za pamwamba kwambiri.
و در جای او خدای قلعه‌ها راتکریم خواهد نمود و خدایی را که پدرانش او رانشناختند با طلا و نقره و سنگهای گرانبها ونفایس تکریم خواهد نمود.۳۸
39 Anthu opembedza mulungu wachilendo adzakhala ngati linga lake. Idzalemekeza iwowa kwambiri, ndipo idzawayika kuti alamulire anthu ambiri. Idzawagawira dziko ngati malipiro awo.
و با قلعه های حصین مثل خدای بیگانه عمل خواهد نمود وآنانی را که بدو اعتراف نمایند در جلال ایشان خواهد افزود و ایشان را بر اشخاص بسیار تسلطخواهد داد و زمین را برای اجرت (ایشان ) تقسیم خواهد نمود.۳۹
40 “Pa nthawi yomaliza mfumu yakummwera idzachita nkhondo ndi mfumu yakumpoto. Koma mfumu yakumpotoyi idzayikantha ndi magaleta ndi akavalo ndi sitima zapamadzi zambiri ngati mphepo yamkokomo. Idzalowa mʼmayiko ambiri ndikuwakokolola onse ngati madzi osefukira.
«و در زمان آخر پادشاه جنوب با وی مقاتله خواهد نمود و پادشاه شمال با ارابه‌ها و سواران و کشتیهای بسیار مانند گردباد به ضد اوخواهد آمد و به زمینها سیلان کرده، از آنها عبورخواهد کرد.۴۰
41 Idzalowanso mʼDziko Lokongola ndipo anthu ambiri adzaphedwa. Koma Edomu, Mowabu ndi olamulira a Amoni adzapulumuka.
و به فخر زمینها وارد خواهد شدو بسیاری خواهند افتاد اما اینان یعنی ادوم وموآب و روسای بنی عمون از دست او خلاصی خواهند یافت.۴۱
42 Idzathira nkhondo mayiko ambiri ndipo ngakhale Igupto sadzapulumuka.
و دست خود را بر کشورهادراز خواهد کرد و زمین مصر رهایی نخواهدیافت.۴۲
43 Idzalanda chuma cha golide, siliva, ndi zonse za mtengowapatali za ku Igupto, ndiponso anthu a ku Libiya ndi Akusi adzagonja kwa iwo.
و بر خزانه های طلا و نقره و بر همه نفایس مصر استیلا خواهد یافت و لبیان وحبشیان در موکب او خواهند بود.۴۳
44 Koma uthenga wochokera kummawa ndi kumpoto udzayiopsa, ndipo idzapita ndi ukali kukawononga ndi kutheratu anthu ambiri.
لیکن اخباراز مشرق و شمال او را مضطرب خواهد ساخت، لهذا با خشم عظیمی بیرون رفته، اشخاص بسیاری را تباه کرده، بالکل هلاک خواهد ساخت.۴۴
45 Mfumuyo idzayimika matenti ake aufumu, pakati pa nyanja ndi phiri lokongola. Komabe mapeto ake mfumuyo idzaphedwa, ndipo palibe amene adzayithandize.”
و خیمه های ملوکانه خود را در کوه مجیدمقدس در میان دو دریا برپا خواهد نمود، لیکن به اجل خود خواهد رسید و معینی نخواهد داشت.۴۵

< Danieli 11 >