< Danieli 11 >
1 Ndipo chaka choyamba cha Dariyo Mmedi ine Mikayeli ndinabwera kumuthandiza ndi kumuteteza Gabrieli.
And I also, in the first year of Darius the Mede, stood up to confirm and strengthen him.
2 “Ndipo tsopano ndikuwuza zoona: Mafumu ena atatu adzalamulira ku Peresiya, ndipo kenaka padzadzuka mfumu yachinayi imene idzakhala yolemera kwambiri kuposa onsewo. Popeza kuti idzakhala ndi mphamvu chifukwa cha chuma chake, idzadzutsa onse kuti alimbane ndi ufumu wa Grisi.
And now I will tell thee what is true. Behold, there shall arise yet three kings in Persia, and the fourth shall be far richer than they all; and, relying upon his riches, he shall stir up all against the realm of Greece.
3 Kenaka mfumu yamphamvu idzafika imene idzalamulira ndi ufumu waukulu ndi kuchita zimene ifuna.
But a mighty king shall arise, and rule with great dominion, and do according to his will.
4 Koma ufumu wake ukadzafika pachimake, udzawonongedwa ndi kugawidwa mʼzigawo zinayi. Ufumuwo sudzaperekedwa kwa zidzukulu zake, ndipo olowa mʼmalo mwake sadzakhala ndi mphamvu monga anali nazo, chifukwa ufumu wake udzazulidwa ndi kuperekedwa kwa ena.
But when he shall have arisen, his kingdom shall be broken in pieces, and shall be divided toward the four winds of heaven; and not to his posterity, nor with the dominion with which he ruled; for his kingdom shall be plucked up, and divided amongst others besides those.
5 “Mfumu ya kummwera idzakhala yamphamvu, koma mmodzi mwa akalonga ake adzakhala ndi mphamvu kuposa iyo; adzalamulira ufumu wake waukulu kwambiri.
And the king of the South shall become strong; but one of his princes shall become stronger than he, and have dominion; his dominion shall be a great dominion.
6 Patapita zaka zingapo, mfumu ya kummwera ndi mfumu ya kumpoto adzachita pangano. Mwana wamkazi wa mfumu ya kummwera adzapita nakakwatiwa ndi mfumu ya kumpoto pokhazikitsa pangano la mtendere, koma ulamuliro wake pamodzi ndi wa mwana wake sudzakhalitsa. Mʼmasiku amenewo iye, mwamuna wake, mwana wake ndi atumiki ake, onse adzaperekedwa kwa adani.
And after some years they shall ally themselves with each other; and the daughter of the king of the South shall come to the king of the North, to make peace; but she shall not retain the power of giving aid; neither shall he stand, nor his aid; but she shall be given up, and they that caused her to go, and he that begat her, and he that received her in those times.
7 “Mmodzi wochokera ku banja la mkaziyo adzadzuka nadzalamulira mʼmalo mwake. Iye adzamenyana ndi ankhondo a mfumu ya kumpoto ndi kulowa mʼmalo ake otetezedwa; adzachita nawo nkhondo ndi kupambana.
But from a shoot of her roots shall one arise in his place, who shall come to an army, and shall come against the fortresses of the king of the North, and shall deal with them according to his pleasure, and prevail against them.
8 Iye adzalandanso milungu yawo, mafano awo achitsulo, ndi ziwiya zawo zamtengowapatali zasiliva ndi golide ndi kubwerera nazo ku Igupto. Adzaleka osayithira nkhondo mfumu ya kumpoto kwa zaka zingapo.
And their gods, with their molten images, and their precious vessels of silver and of gold, shall he carry into captivity into Egypt; then shall he stand away for many years from the king of the North;
9 Kenaka mfumu ya kumpoto idzathira nkhondo dziko la mfumu ya kummwera koma idzalephera ndi kubwerera kwawo.
and he shall come against the kingdom of the king of the South, but he shall return into his own land.
10 Ana ake adzakonzekera nkhondo ndi kusonkhanitsa gulu lankhondo lalikulu, limene lidzathira nkhondo mfumu yakummwera ngati chigumula mpaka kumalo ake otetezedwa.
But his sons shall be stirred up, and shall assemble a multitude of large forces; and one of them shall move onward, and overflow, and pass through, and shall again stir himself up to carry on the war even to his stronghold.
11 “Kenaka mfumu yakummwera idzatuluka mokwiya ndi kumenya nkhondo ndi mfumu yakumpoto, imene idzasonkhanitsa gulu lalikulu la nkhondo, koma idzayigonjetsa.
Then shall the king of the South be enraged, and shall come forth and fight with him, even with the king of the North; and shall lead forth a great multitude, and the multitude shall be given into his hand.
12 Gulu la nkhondoli likadzagwidwa, mfumu yakummwera idzayamba kudzikuza ndipo idzapha anthu miyandamiyanda, koma kupambanaku sikudzapitirira.
And the multitude shall be elated, and his heart shall be lifted up, and he shall cast down tens of thousands; but he shall not be strong.
13 Popeza mfumu ya kumpoto idzasonkhanitsa gulu lina lankhondo, lochulukirapo kuposa loyamba; ndipo patapita zaka zingapo idzabwera ndi chigulu chachikulu cha nkhondo chokonzekeratu ndi zida.
For the king of the North shall return and raise up against him a multitude greater than the former, and shall steadily come after certain years with a great army and with great riches.
14 “Nthawi imeneyo ambiri adzawukira mfumu ya kummwera. Anthu achisokonezo pakati panu nawonso adzawukira pokwaniritsa masomphenya, koma sadzapambana.
And in those times many will stand up against the king of the South; and violent men of thy people shall exalt themselves, so as to establish the vision, and shall fall.
15 Kenaka mfumu ya kumpoto idzafika ndikuzinga mzinda powunda nthumbira za nkhondo ndipo idzagonjetsa mzinda wotetezedwa. Gulu lankhondo la kummwera lidzasowa mphamvu; ngakhale akatswiri awo ankhondo sadzakhala ndi mphamvu zogonjetsera ankhondo a kumpoto.
And the king of the North shall come, and cast up a mound, and take a fortified city; and the arms of the South shall not withstand, neither his chosen men, neither shall there be any strength to withstand.
16 Mfumu ya kumpoto idzachita zofuna zake; palibe aliyense adzayigonjetse. Idzakhazikitsa ulamuliro wake mu Dziko Lokongola. Zonse zidzakhala mu ulamuliro wa mfumu yakumpoto ija.
And he that cometh against him shall do according to his will, and none shall stand before him; and he shall stand in the beautiful land, and destruction shall be in his hand.
17 Idzafika ndi mphamvu za ufumu wake wonse ndipo idzayesa kuchita pangano la mtendere ndi mfumu ya kummwera. Ndipo idzamupatsa mwana wake wamkazi kuti amukwatire ndi cholinga cholanda ufumu, koma zolinga zake sizidzatheka kapena kumuthandiza.
And he shall set his face to come with the strength of his whole kingdom, and shall make pacification with him; and he shall give him his daughter in marriage, to ruin his dominion. But it shall not succeed, neither shall it be for him.
18 Kenaka idzatembenukira ku mayiko a mʼmbali mwa nyanja ndi kulanda mizinda yambiri, koma mtsogoleri wina wa nkhondo adzathetsa kudzikuza kwakeko ndipo adzabwezera chipongwecho kwa iye.
After this he shall turn his face to the isles, and shall take many; but a commander shall put an end to his scorn; nay, shall cause his scorn to return upon himself.
19 Zikadzatha izi, mfumu idzabwerera ku malo otetezedwa a dziko la kwawo koma idzapunthwa ndi kugwa osapezekanso.
Then shall he turn his face to the strongholds of his own land; and he shall stumble, and fall, and shall not be found.
20 “Mfumu imene idzatenga malo ake idzatumiza wokhometsa msonkho kuti chuma cha ufumu wake chichuluke. Komabe mʼzaka zochepa mfumuyo idzawonongedwa osati mu mkwiyo kapena ku nkhondo.
Then shall arise in his place one who shall send an exacter of tribute through the glory of his kingdom; but within few days shall he be destroyed, neither by anger nor by battle.
21 “Mʼmalo mwake mudzalowa munthu wonyozeka amene si wa banja laufumu. Iye adzabwera pamene anthu akuganiza kuti ali pa mtendere, ndipo adzalanda ufumuwo mwa chinyengo.
And in his place shall arise a despised person, to whom they shall not give the honor of the kingdom; but in the midst of peace he shall come in and obtain the kingdom by flatteries.
22 Kenaka adzagonetsa gulu lalikulu lankhondo kuphatikizapo Mkulu wa Ansembe wapangano.
And the forces of a flood shall be overwhelmed before him, and shall be broken in pieces; and even the prince that is allied with him.
23 Atatha kuchita naye pangano, iye adzachita monyenga, ndipo ngakhale adzakhale ndi anthu ochepa adzakhalabe ndi mphamvu.
For after making a league with him, he will practise deceit; for he will come up, and prevail with a small people.
24 Mwadzidzidzi, iye adzazithira nkhondo zigawo zolemera kwambiri ndipo adzachita zimene makolo ake ngakhale agogo ake sanachitepo. Iye adzagawira zolanda, zofunkha ndi chuma kwa omutsatira. Adzachita chiwembu cholanda mizinda yotetezedwa koma kwa kanthawi kochepa.
In the midst of security shall he come into the fattest provinces of the land, and he shall do what his fathers never did, nor his fathers' fathers; he shall scatter among them prey, and spoil, and riches; and he shall form his devices against the strongholds, even to a set time.
25 “Mfumu ya kumpoto idzalimba mtima, ndipo idzasonkhanitsa gulu lalikulu la ankhondo kuti lithire nkhondo mfumu yakummwera. Mfumu yakummwera ndi gulu lake lankhondo lalikulu ndi lamphamvu idzathirana nkhondo ndi mfumu yakumpoto koma sidzapambana chifukwa cha ziwembu zimene adzamukonzera.
And he shall stir up his power and his courage against the king of the South, with a great army; and the king of the South shall be stirred up to battle with a very great and mighty army; but he shall not stand, for they shall form devices against him.
26 Amene amadya chakudya ndi mfumu adzamuukira; gulu lake lankhondo lidzagonjetsedwa, ndipo ambiri adzafera ku nkhondo.
Even they that eat of his own food shall destroy him; and his army shall overflow, and many shall fall down slain.
27 Mafumu awiriwa mitima yawo idzalinga ku zoyipa. Azidzanamizana ali pa tebulo limodzi, koma zolinga zawo sizidzatheka chifukwa nthawi idzakhala isanakwane.
And the hearts of both these kings shall be to do mischief; and at one table shall they speak lies; but it shall not prosper; for yet the end is for the appointed time.
28 Mfumu ya kumpoto idzabwerera ku dziko la kwawo ndi chuma chambiri, koma mtima wake udzafunitsitsa pangano lopatulika. Idzawononga panganolo ndipo kenaka idzabwerera ku dziko lake.
Then shall he return into his land with great riches; and he will set his heart against the holy covenant, and he will execute his purposes, and return to his own land.
29 “Patapita nthawi mfumu ya kumpoto idzabwereranso kummwera koma sidzapambana monga inachitira kale.
At the appointed time he shall again go against the South; but the second time it shall not be as at the first.
30 Sitima zapamadzi zochokera ku mayiko a ku madzulo zidzalimbana naye, ndipo adzataya mtima. Kenaka idzabwerera mopsa mtima ndi kudzalimbana ndi chipembedzo cha anthu opatulika. Idzabwerera ndi kuchitira chifundo amene sadzasunga pangano loyera.
For the Chittaean ships shall come against him, and he shall be discouraged, and return, and be enraged against the holy covenant, and execute his purposes; and he shall again have an understanding with them that forsake the holy covenant.
31 “Ankhondo ake adzayipitsa linga la Nyumba ya Mulungu ndipo adzathetsa nsembe za tsiku ndi tsiku. Kenaka adzakhazikitsa chonyansa chimene chabweretsa chiwonongeko.
And forces shall be raised by him, which shall pollute the sanctuary, the stronghold, and take away the daily sacrifice, and set up the abomination of the destroyer.
32 Ndi mawu oshashalika mfumuyo idzakopa amene anaphwanya pangano, koma anthu amene amadziwa Mulungu wawo adzalimbika ndipo adzayikana mfumuyo kwathunthu.
And such as do wickedly against the covenant will he lead to apostasy by flatteries; but the people that know their God shall be strong, and do exploits.
33 “Amene ndi anzeru adzalangiza ambiri. Koma patapita kanthawi adzaphedwa ndi lupanga kapena kutenthedwa, kapena kugwidwa kapena kulandidwa katundu.
And they that have understanding among the people shall instruct many; but they shall fall by the sword, and by flame, by captivity, and by spoil, many days.
34 Pa nthawi yozunzikayi ena adzawathandiza pangʼono, koma ambiri othandizawo adzakhala achinyengo.
And whilst they fall they shall receive a little help, and many shall join themselves to them with flatteries.
35 Ena mwa anzeruwo adzaphedwa ndi cholinga chakuti ayengedwe, otsala mwa iwo ayeretsedwe ndi kukhala wopanda banga kufikira nthawi yomaliza, popeza idzafika ndithu nthawi imene Mulungu wayika.
And some of them of understanding shall fall, to try them, and to purify, and cleanse, even to the time of the end, for it is yet at the time appointed.
36 “Mfumu ya kumpoto idzachita zimene ikufuna. Idzadzikweza ndi kudziyesa yopambana mulungu aliyense ndipo idzanenera za mwano Mulungu wa milungu. Iyo idzapambana mpaka nthawi yoti Mulungu ayilange mwa mkwiyo itakwana popeza chimene chatsimikizika chiyenera kuchitika.
And the king shall do according to his will; and he will exalt himself and magnify himself against every god, and he will speak horrible things against the God of gods, and he will prosper until the indignation be accomplished; for that which is determined shall be done.
37 Mfumuyo idzanyoza milungu ya makolo ake ndiponso mulungu wokondedwa ndi akazi, sidzachitiranso ulemu mulungu aliyense, koma idzadzikweza yokha pamwamba pa onse.
Neither will he regard the god of his fathers, nor the desire of women; nor will he regard any god, but he will magnify himself against all.
38 Mʼmalo mwa onsewo, idzachitira ulemu mulungu wachitetezo; mulungu wosadziwika ndi makolo ake. Iyo idzapereka kwa mulunguyo golide ndi siliva, ndi miyala yokongola, ndiponso mphatso za pamwamba kwambiri.
But in their place will he honor the god of strongholds, even the god whom his fathers knew not shall he honor with gold, and with silver, and with precious stones, and with jewels.
39 Anthu opembedza mulungu wachilendo adzakhala ngati linga lake. Idzalemekeza iwowa kwambiri, ndipo idzawayika kuti alamulire anthu ambiri. Idzawagawira dziko ngati malipiro awo.
And he shall do his will against fenced strongholds with a strange god; whoever acknowledge him, to them he will give great honor, and give them dominion over many, and divide the land amongst them for a reward.
40 “Pa nthawi yomaliza mfumu yakummwera idzachita nkhondo ndi mfumu yakumpoto. Koma mfumu yakumpotoyi idzayikantha ndi magaleta ndi akavalo ndi sitima zapamadzi zambiri ngati mphepo yamkokomo. Idzalowa mʼmayiko ambiri ndikuwakokolola onse ngati madzi osefukira.
But at the time of the end shall the king of the South push at him, and the king of the North shall rush against him like a whirlwind with chariots, and with horsemen, and with many ships; and he shall enter into the countries, and overflow them, and pass over them.
41 Idzalowanso mʼDziko Lokongola ndipo anthu ambiri adzaphedwa. Koma Edomu, Mowabu ndi olamulira a Amoni adzapulumuka.
He shall also enter into the beautiful land, and multitudes shall be overthrown; but these shall escape out of his hand, Edom, and Moab, and the chief of the sons of Ammon.
42 Idzathira nkhondo mayiko ambiri ndipo ngakhale Igupto sadzapulumuka.
He shall stretch forth his hand also upon the countries, and the land of Egypt shall not escape.
43 Idzalanda chuma cha golide, siliva, ndi zonse za mtengowapatali za ku Igupto, ndiponso anthu a ku Libiya ndi Akusi adzagonja kwa iwo.
And he shall have power over the treasures of gold and of silver, and over all the precious things of Egypt; and the Lybians and Ethiopians shall be in his train.
44 Koma uthenga wochokera kummawa ndi kumpoto udzayiopsa, ndipo idzapita ndi ukali kukawononga ndi kutheratu anthu ambiri.
But tidings out of the East and out of the North shall trouble him, and he shall go forth with great fury to destroy and utterly to take away many.
45 Mfumuyo idzayimika matenti ake aufumu, pakati pa nyanja ndi phiri lokongola. Komabe mapeto ake mfumuyo idzaphedwa, ndipo palibe amene adzayithandize.”
And he shall pitch his palace-tents between the sea and the beautiful holy mountain; but he shall come to his end, and none shall help him.