< Danieli 10 >

1 Chaka chachitatu cha Koresi mfumu ya Aperezi, Danieli amene ankatchedwa Belitesezara analandira mawu a vumbulutso. Uthenga wake unali woona ndipo anawumvetsa movutikira. Uthengawu anawumva kudzera mʼmasomphenya.
Ngomnyaka wesithathu kaKoresi inkosi yePerisiya ulutho lwembulelwa uDaniyeli, obizo lakhe labizwa ngokuthi nguBeliteshazari. Njalo lolulutho lwaluliqiniso mayelana lokulwisana okukhulu. Njalo waluqedisisa lolulutho, waba lokuqedisisa ngombono.
2 Pa nthawi imeneyi, ine Danieli ndinalira kwa masabata atatu.
Ngalezonsuku, mina Daniyeli ngangilila okwamaviki amathathu agcweleyo.
3 Sindinadye chakudya chokoma; nyama ndi vinyo sizinakhudze milomo yanga ndi pangʼono pomwe; ndipo sindinadzole mafuta aliwonse mpaka patatha masabata atatu.
Kangidlanga sinkwa esiloyisekayo, njalo kakuzanga nyama kumbe iwayini emlonyeni wami, futhi kangizigcobanga ngitsho, kwaze kwagcwaliseka amaviki amathathu ezinsuku.
4 Pa tsiku la 24 la mwezi woyamba, nditayima mʼmbali mwa mtsinje waukulu wa Tigirisi,
Kwathi ngosuku lwamatshumi amabili lane lwenyanga yokuqala, mina ngiseceleni komfula omkhulu, oyiHidekeli;
5 ndinakweza maso ndipo ndinaona kuti pafupi ndi ine panali munthu wochokera ku Ufazi atavala zovala zosalala ndi lamba wa golide woyengeka bwino mʼchiwuno mwake.
ngasengiphakamisa amehlo ami, ngabona, khangela-ke umuntu othile egqoke ilembu elicolekileyo, okhalo lwakhe lwalubhincwe ngegolide elicwengekileyo leUfazi.
6 Thupi lake linali ngati mwala wonyezimira, nkhope yake ngati chiphaliwali, maso ake ngati muni wowala, manja ndi miyendo yake ngati mkuwa wowala, ndipo mawu ake ngati liwu la chikhamu cha anthu.
Lomzimba wakhe wawunjengebherule, lobuso bakhe babunjengesimo sombane, lamehlo akhe njengezibane zomlilo, lengalo zakhe lenyawo zakhe njengombala wethusi elikhazimulayo, lelizwi lamazwi akhe njengomsindo wexuku.
7 Ine Danieli ndinali ndekha pamene ndinaona masomphenyawa; anthu amene anali ndi ine sanawaone, koma anadzazidwa ndi mantha kotero kuti anathawa ndi kukabisala.
Yimi ngedwa uDaniyeli engabona lowombono, ngoba abantu ababelami kabawubonanga umbono. Kodwa ukuqhuqha okukhulu kwabehlela, baze babaleka ukuze bacatshe.
8 Choncho ndinatsala ndekha, ndikuonetsetsa masomphenya a ulemererowa. Ndiye nkhope yanga inasinthika, ndinalefuka, ndipo ndinalibenso mphamvu.
Ngakho mina ngasala ngedwa, ngabona lumbono omkhulu, futhi kakusalanga mandla kimi, lobuhle bami baguquka kimi baba yikonakala, kangisalelwanga ngamandla.
9 Kenaka ndinamva iye akuyankhula, ndipo pamene ndinkamvetsera, ndinagwa chafufumimba ndi kugona tulo tofa nato.
Ngasengisizwa ilizwi lamazwi akhe; njalo lapho ngisizwa ilizwi lamazwi akhe, mina ngehlelwa yibuthongo obukhulu ebusweni bami, lobuso bami bungasemhlabathini.
10 Dzanja linandikhudza ndi kundinyamula ndipo ndinachita ngati kuwerama pa mawondo manja atagwira pansi.
Khangela-ke, isandla sangithinta, sangimisa ngithuthumela ngamadolo ami lempama zezandla zami.
11 Iye anati, “Danieli, iwe wokondedwa kwambiri, imirira ndipo uganizire mosamala mawu ndiyankhule kwa iwe, popeza tsopano ndatumidwa kwa iwe.” Atanena izi kwa ine ndinayimirira monjenjemera.
Wasesithi kimi: Daniyeli, umuntu othandwe kakhulu, zwisisa amazwi engiwakhuluma kuwe, ume ngokuma kwakho, ngoba khathesi ngithunywe kuwe. Esekhulume lelilizwi kimi, ngema ngithuthumela.
12 Ndipo iye anapitiriza nati, “Usachite mantha Danieli. Kuyambira tsiku loyamba pamene unatsimikiza mtima kuti umvetse zinthuzi ndi kudzichepetsa pamaso pa Mulungu wako, pempho lako linamveka ndipo ndabwera kudzayankha mapemphero akowo.
Wasesithi kimi: Ungesabi, Daniyeli, ngoba kusukela osukwini lokuqala owabeka ngalo inhliziyo yakho ukuqedisisa lokuzithoba phambi kukaNkulunkulu wakho, amazwi akho ezwakala, ngizile-ke mina ngenxa yamazwi akho.
13 Koma mtsogoleri wa ufumu wa Peresiya ananditchingira pa masiku 21, kenaka Mikayeli, mmodzi mwa angelo akuluakulu anadza kudzandithandiza chifukwa ndinakhala komweko ndi mafumu a ku Peresiya.
Kodwa isiphathamandla sombuso wamaPerisiya samelana lami okwensuku ezingamatshumi amabili lanye; kodwa khangela, uMikayeli omunye weziphathamandla zakuqala weza ukuzangisiza; mina ngasengisala khona ngasemakhosini ePerisiya.
14 Tsopano ndafika kuti ndidzakufotokozere zimene zidzachitika kwa anthu a mtundu wako kutsogolo. Ndipo pali masomphenya enanso okhudza nthawi imene ikudza.”
Khathesi ngizile ukuthi ngikwenze uqedisise okuzakwehlela abantu bakho ekucineni kwezinsuku, ngoba umbono usengowezinsuku ezinengi.
15 Pa nthawi yomwe ankanena izi kwa ine, ndinazolika nkhope yanga pansi kusowa chonena.
Esekhulumile amazwi anje kimi, ngakhangelisa ubuso bami emhlabathini, ngaba yisimungulu.
16 Kenaka wina wa maonekedwe ngati munthu anakhudza milomo yanga, ndipo ndinatsekula pakamwa panga ndi kuyamba kuyankhula. Ndinati kwa amene anayima patsogolo panga, “Ine ndasweka mtima chifukwa cha masomphenyawa mbuye wanga, ndipo ndalefuka.
Khangela-ke, omunye ofanana lomfanekiso wamadodana abantu wathinta indebe zami; ngasengivula umlomo wami, ngakhuluma, ngathi kulowo owayemi phambi kwami: Nkosi yami, ngenxa yombono izinsizi zami seziphendukele phezu kwami, kangaba lamandla.
17 Kodi ine mtumiki wamba wa mbuye wanga ndingathe bwanji kuyankhula ndi inu mbuye wanga? Mphamvu zanga zatha, ndipo ndikulephera kupuma.”
Ngoba inceku yale inkosi yami ingaba lakho ukukhuluma njani lale inkosi yami? Mayelana lami, kusukela ngalesosikhathi kakusalanga mandla kimi, lokuphefumula kwakungasekho kimi.
18 Kenaka wooneka ngati munthu uja anandikhudzanso ndipo anandipatsa mphamvu.
Wasebuya wangithinta onjengomfanekiso womuntu, wangiqinisa.
19 Iye anati, “Usachite mantha, munthu wokondedwa kwambiriwe. Mtendere ukhale ndi Iwe ndipo ukhale wolimba.” Atayankhula nane, ndinalimbikitsidwa ndipo ndinati, “Yankhulani Mbuye wanga, popeza mwandipatsa mphamvu.”
Wasesithi: Ungesabi, muntu othandiweyo kakhulu; ukuthula kakube kuwe, qina, yebo, qina. Kwathi esekhulume lami, ngaqiniswa, ngathi: Kayikhulume inkosi yami, ngoba ungiqinisile.
20 Ndipo iye anati, “Kodi ukudziwa chifukwa chimene ndabwerera kwa iwe? Ndiyamba ndabwerera kukamenyana ndi mtsogoleri wa ufumu wa Peresiya, ndipo ndikakanthana naye, kenaka mtsogoleri wa ufumu wa Grisi adzabwera.
Wasesithi: Uyazi yini ukuthi ngizeleni kuwe? Khathesi-ke ngizabuyela ukuzakulwa lesiphathamandla sePerisiya; lalapho sengiphumile, khangela-ke, isiphathamandla seGirisi sizafika.
21 Koma ndikuwuza zimene zalembedwa mʼbuku la zoona koma palibe wondithandiza kulimbana nawo kupatula Mikayeli, kalonga wako.”
Kodwa ngizakutshela lokho okubhaliweyo embhalweni weqiniso; njalo kakho loyedwa obambisana lami kulezizinto, ngaphandle kukaMikayeli isiphathamandla senu.

< Danieli 10 >