< Akolose 1 >

1 Paulo, mtumwi wa Khristu Yesu mwachifuniro cha Mulungu, ndi Timoteyo mʼbale wathu.
NA Paulo aku, na ka lunaolelo a Iesu Kristo ma ka manao mai o ke Akua, na Timoteo hoi ka hoahanau,
2 Kulembera abale oyera mtima ndi okhulupirira a ku Kolose mwa Khristu. Chisomo ndi mtendere kwa inu zochokera kwa Mulungu Atate athu.
I ka poe haipule a me na hoahanau manaoio iloko o Kristo, ma Kolosa; no oukou ke aloha a me ka malu mai ke Akua mai, o ko kakou Makua, a me ka Haku o Iesu Kristo.
3 Timayamika Mulungu Atate wa Ambuye athu Yesu Khristu, nthawi zonse pamene tikukupemphererani.
Ke hoomaikai aku nei maua i ke Akua, i ka Makua o ko kakou Haku o Iesu Kristo, e pule mau ana no oukou,
4 Timayamika chifukwa tinamva za chikhulupiriro chanu mwa Khristu Yesu ndi za chikondi chanu pa oyera mtima onse.
Ua lohe maua i ko oukou manaoio ana ia Kristo Iesu, a me ko oukou aloha ana i na haipule a pau,
5 Chikhulupiriro ndi chikondi, gwero lake ndi chiyembekezo chomwe muli nacho chodzalandira zimene anakusungirani kumwamba. Munamva kale za zimenezi kudzera mʼmawu a choonadi, Uthenga Wabwino
No ka pono e manaolanaia'i, e waiho ana no oukou ma ka lani: o ka mea a oukou i lohe mua ai maloko o ka olelo oiaio o ka eua nelio;
6 umene unafika kwa inu. Pa dziko lonse lapansi Uthenga Wabwino ukubereka chipatso ndi kukula monga momwe zakhala zikuchitikira pakati panu kuyambira tsiku limene munawumva ndi kuzindikira chisomo cha Mulungu mu choonadi chonse.
I hiki mai io oukou la e like me ia ma ka honua a pau; a ua hua mai hoi i ka hua, me ia hoi iwaena o oukou, mai ka la i lohe ai oukou, a i ike ai hoi i ke aloha o ke Akua, ma ka oiaio.
7 Inu munaphunzira zimenezi kuchokera kwa Epafra, mtumiki mnzathu wokondedwa, amene ndi mtumiki wokhulupirika wa Khristu mʼmalo mwathu.
E like mo ka oukou hoolohe ana ia Epapera i ko maua hoakauwa aloha, i ko Kristo kahunapule hoopono no oukou;
8 Iye anatiwuza za chikondi chanu chimene Mzimu anakupatsani.
Nana no i hoike mai ia maua i ko oukou aloha ma ka naau.
9 Chifukwa cha ichi, kuyambira tsiku limene tinamva za inu, sitinasiye kukupemphererani ndi kumupempha Mulungu kuti akudzazeni ndi chidziwitso cha chifuniro chake kudzera mu nzeru yonse yauzimu ndi kumvetsetsa.
Nolaila hoi, mai ka manawa mai i lohe ai maua, aole maua i hooki i ka pule no oukou, me ka noi aku i hoopihaia mai oukou me ka ike i kona makemake, a me ka naanao io ma ka Uhane;
10 Ndipo tikupempherera zimenezi ndi cholinga chakuti inu mukhale moyo oyenera Ambuye ndi kumukondweretsa mʼnjira zonse. Kubereka chipatso pa ntchito iliyonse yabwino, ndi kukula mʼchidziwitso cha Mulungu.
I hele oukou ma ka pono o ka Haku, i na mea a pau i oluoluia mai ai, e hua mai ana i ka hua ma na hana maikai a pau, me ka mahuahua ana ae o ka ike ana i ke Akua.
11 Timapempheranso kuti Mulungu akulimbikitseni ndi mphamvu yake yonse ya ulemerero wake, kuti muzipirira zonse ndi mitima yofatsa ndi ya chimwemwe
E hooikaika nui ia mai oukou e kona mana nani, i ke kupaa ana, a me ke ahonui a me ka olioli;
12 ndi kuyamika Atate nthawi zonse, amene wakuyenerezani kuti mulandire nawo chuma cha oyera mtima mu ufumu wa kuwunika.
Me ka hoomaikai aku i ka Makua nana kakou i hoopono mai, i loaa mai ai ia kakou ka pono e ili mai ana i ka poe haipule i ke ao.
13 Pakuti Iye anatipulumutsa ku ulamuliro wa mdima ndi kutibweretsa mu ufumu wa Mwana wake wokondedwa.
Nana hoi kakou i hoola, mai ka mana mai o ka pouli, a ua lawe hoi oia ia kakou iloko o ke aupuni o kana Keiki punahele;
14 Mwa Iyeyu ife tinawomboledwa ndi kukhululukidwa machimo.
Iloko ona ke ola no kakou i kona koko, o ke kala ana'e o ka hewa.
15 Mwanayu ndiye chithunzi cha Mulungu wosaonekayo. Iye ndiye Mwana wake woyamba kubadwa ndi wolamulira zolengedwa zonse.
Oia hoi ka like me ke Akua i nana ole ia, oia hoi ka mua o na mea a pau i hanaia'i.
16 Pakuti zinthu zonse zinalengedwa kudzera mwa Iye. Zinthu zakumwamba ndi za pa dziko lapansi, zooneka ndi zosaoneka, maufumu, akuluakulu, aulamuliro ndi amphamvu. Zinthu zonse zinalengedwa kudzera mwa Iye ndipo anazilengera Iyeyo.
No ka mea, ua hanaia e ia na mea a pau, o ko ka lani a me ko ka honua, i nanaia, a i nana ole ia, o na nohoalii, o na haku, o na luna, a me na'lii: ua hauaia na mea a pau ma ona la, a nona no hoi.
17 Iyeyo analipo zinthu zonse zisanalengedwe ndipo zinthu zonse zimamangika pamodzi mwa Iye.
Oia hoi ka mua o na mea a pau, a ma ona la no hoi i mau ai na mea a pau.
18 Iye ndiyenso mutu wa thupi, limene ndi mpingo. Iye ndiye chiyambi chake, woyamba kuuka kwa akufa, kuti Iyeyo akhale wopambana zonse.
Oia hoi ke poo o ke kino, o ka ekalesia: oia ka makamua, o ka hanau mua hoi mai ka make mai; i lilo ia i pookela iwaena o na mea a pau.
19 Pakuti kunamukomera Mulungu kuti umulungu wake wonse ukhalemo mwa Khristu.
No ka mea, o ka pono no ia i ka Makua e noho nui ka pono a pau iloko ona;
20 Ndipo kudzera mwa Iye Mulungu ayanjanitsenso zinthu zonse ndi Iye mwini, zinthu za pa dziko lapansi, kapena zinthu za kumwamba. Iye anachita mtendere kudzera mʼmagazi ake, wokhetsedwa pa mtanda.
A ma ona la e hoolaulea ai i na mea a pau ia ia iho, e hoomaiu ana ma ke koko o kona kea; ma ona la, i ko ka honua nei, a me ko ka lani.
21 Kale inu munali kutali ndi Mulungu ndipo munali adani a Mulungu mʼmaganizo mwanu chifukwa cha khalidwe lanu loyipa.
O oukou kekahi, ka poe i ku e i kekahi manawa, ka poe enemi i ko oukou manao ana ma na hana hewa, o kana ia i hoolaulea ae nei,
22 Koma tsopano Iye anakuyanjanitsani mʼthupi la Khristu kudzera mu imfa kuti akuperekeni pamaso pake oyera, opanda banga ndi opanda chotsutsidwa nacho
Ma kona kino kanaka, i ka make ana, e hoike oia ia oukou he hemolele, he hala ole, a me ka hoohewa ole ia, imua o kona alo;
23 ngati mupitirirabe kukhala mʼchikhulupiriro chanu, okhazikika ndi olimba, osasunthidwa kuchoka pa chiyembekezo chimene munachigwira mu Uthenga Wabwino. Uwu ndi Uthenga Wabwino umene munawumva, umene wakhala ukulalikidwa kwa olengedwa onse a pansi pa thambo, ndi umenenso, ine Paulo ndinakhala mtumiki wake.
Ke noho mau aku oukou ma ka manaoio, i hookumuia oukou me ka hoopaaia, ke hoonee ole ia ku hoi mai ka manaolana aku o ka euanelio a oukou i lohe ai, ka mea i haiia'ku i na mea a pau i hanaia malalo ae o ka lani, nona iho au o Paulo i hooliloia'e nei i lunalawehana.
24 Tsopano ine ndikukondwa kuti ndinavutika chifukwa cha inu, ndipo ndikukwaniritsa mʼthupi langa zimene zikuperewera pa masautso a Khristu, chifukwa cha thupi lake, limene ndi Mpingo.
ke hauoli nei au i ko'u ehaeha no oukou, e hoopau ana iloko o ko'u kino, i ke koena o ko Kristo ehaeha ana, no kona kino, oia no ka ekalesia.
25 Ine ndakhala mtumiki wake mwa lamulo limene Mulungu anandipatsa kuti ndipereke Mawu a Mulungu athunthu,
Nona wau i hooliloia'e nei i lunalawehana, e like me ke kauoha a ke Akua i haawi mai ai ia'u no oukou, e hoolaha ae i ka olelo a ke Akua;
26 chinsinsi chimene chakhala chikubisika kwa nthawi ndi mibado, koma tsopano chawululidwa kwa oyera mtima. (aiōn g165)
I ka mea pohihihi hunaia'e mai ka wa kahiko mai, a me na hanauna mai, aka i keia manawa, ua hoikeia mai nei i kana mau haipule; (aiōn g165)
27 Kwa iwo amene Mulungu anawasankha kuti awadziwitse pakati pa a mitundu ina, ulemerero wa chuma cha chinsinsi ichi, amene ndi Khristu mwa inu, chiyembekezo cha ulemerero.
I ka poe a ke Akua i hoomaopopo ai i ka waiwai nani o keia mea pohihihi iwaena o ko na aina e; oia no o Kristo iloko o oukou, ka manaolana no ka nani:
28 Ife tikulalikira Khristu, kulangiza ndi kuphunzitsa aliyense mwa nzeru zonse kuti timupereke aliyense wangwiro mwa Khristu.
Oia ka makou e hai aku nei, e ao ana i na kanaka a pau, a e hoonaauao ana i na kanaka a pau i ka naauao io, e hiki ia makou ke hoike i na kanaka a pau i hemolele iloko o Kristo Iesu.
29 Ndi cholinga chimenechi, ine ndikugwira ntchito molimbika ndi mwamphamvu zonse zimene Iye anachita mwa ine.
Nalaila hoi ka'u hana e hooikaika nui nei, e like me kana hana i hooikaika nui mai nei iloko o'u.

< Akolose 1 >