< Akolose 1 >

1 Paulo, mtumwi wa Khristu Yesu mwachifuniro cha Mulungu, ndi Timoteyo mʼbale wathu.
Paul, an Apostle of Christ Jesus by the will of God--and Timothy our brother:
2 Kulembera abale oyera mtima ndi okhulupirira a ku Kolose mwa Khristu. Chisomo ndi mtendere kwa inu zochokera kwa Mulungu Atate athu.
To the people of God and the believing brethren at Colossae who are in Christ. May grace and peace be granted to you from God our Father.
3 Timayamika Mulungu Atate wa Ambuye athu Yesu Khristu, nthawi zonse pamene tikukupemphererani.
We give thanks to God, the Father of our Lord Jesus Christ, constantly praying for you as we do,
4 Timayamika chifukwa tinamva za chikhulupiriro chanu mwa Khristu Yesu ndi za chikondi chanu pa oyera mtima onse.
because we have heard of your faith in Christ Jesus and of the love which you cherish towards all God's people,
5 Chikhulupiriro ndi chikondi, gwero lake ndi chiyembekezo chomwe muli nacho chodzalandira zimene anakusungirani kumwamba. Munamva kale za zimenezi kudzera mʼmawu a choonadi, Uthenga Wabwino
on account of the hope treasured up for you in Heaven. Of this hope you have already heard in the Message of the truth of the Good News.
6 umene unafika kwa inu. Pa dziko lonse lapansi Uthenga Wabwino ukubereka chipatso ndi kukula monga momwe zakhala zikuchitikira pakati panu kuyambira tsiku limene munawumva ndi kuzindikira chisomo cha Mulungu mu choonadi chonse.
For it has reached you, and remains with you, just as it has also spread through the whole world, yielding fruit there and increasing, as it has done among you from the day when first you heard it and came really to know the grace of God,
7 Inu munaphunzira zimenezi kuchokera kwa Epafra, mtumiki mnzathu wokondedwa, amene ndi mtumiki wokhulupirika wa Khristu mʼmalo mwathu.
as you learned it from Epaphras our dearly-loved fellow servant. He is to you a faithful minister of Christ in our stead,
8 Iye anatiwuza za chikondi chanu chimene Mzimu anakupatsani.
and moreover he has informed us of your love, which is inspired by the Spirit.
9 Chifukwa cha ichi, kuyambira tsiku limene tinamva za inu, sitinasiye kukupemphererani ndi kumupempha Mulungu kuti akudzazeni ndi chidziwitso cha chifuniro chake kudzera mu nzeru yonse yauzimu ndi kumvetsetsa.
For this reason we also, from the day we first received these tidings, have never ceased to pray for you and to entreat that you may be filled with a clear knowledge of His will accompanied by thorough wisdom and discernment in spiritual things;
10 Ndipo tikupempherera zimenezi ndi cholinga chakuti inu mukhale moyo oyenera Ambuye ndi kumukondweretsa mʼnjira zonse. Kubereka chipatso pa ntchito iliyonse yabwino, ndi kukula mʼchidziwitso cha Mulungu.
so that your lives may be worthy of the Lord and perfectly pleasing to Him, while you exhibit the results of right action of every sort and grow into a fuller knowledge of God.
11 Timapempheranso kuti Mulungu akulimbikitseni ndi mphamvu yake yonse ya ulemerero wake, kuti muzipirira zonse ndi mitima yofatsa ndi ya chimwemwe
Since His power is so glorious, may you be strengthened with strength of every kind, and be prepared for cheerfully enduring all things with patience and long-suffering;
12 ndi kuyamika Atate nthawi zonse, amene wakuyenerezani kuti mulandire nawo chuma cha oyera mtima mu ufumu wa kuwunika.
and give thanks to the Father who has made us fit to receive our share of the inheritance of God's people in Light.
13 Pakuti Iye anatipulumutsa ku ulamuliro wa mdima ndi kutibweretsa mu ufumu wa Mwana wake wokondedwa.
It is God who has delivered us out of the dominion of darkness, and has transferred us into the Kingdom of His dearly-loved Son,
14 Mwa Iyeyu ife tinawomboledwa ndi kukhululukidwa machimo.
in whom we have our redemption--the forgiveness of our sins.
15 Mwanayu ndiye chithunzi cha Mulungu wosaonekayo. Iye ndiye Mwana wake woyamba kubadwa ndi wolamulira zolengedwa zonse.
Christ is the visible representation of the invisible God, the Firstborn and Lord of all creation.
16 Pakuti zinthu zonse zinalengedwa kudzera mwa Iye. Zinthu zakumwamba ndi za pa dziko lapansi, zooneka ndi zosaoneka, maufumu, akuluakulu, aulamuliro ndi amphamvu. Zinthu zonse zinalengedwa kudzera mwa Iye ndipo anazilengera Iyeyo.
For in Him was created the universe of things in heaven and on earth, things seen and things unseen, thrones, dominions, princedoms, powers--all were created, and exist through and for Him.
17 Iyeyo analipo zinthu zonse zisanalengedwe ndipo zinthu zonse zimamangika pamodzi mwa Iye.
And HE IS before all things and in and through Him the universe is a harmonious whole.
18 Iye ndiyenso mutu wa thupi, limene ndi mpingo. Iye ndiye chiyambi chake, woyamba kuuka kwa akufa, kuti Iyeyo akhale wopambana zonse.
Moreover He is the Head of His Body, the Church. He is the Beginning, the Firstborn from among the dead, in order that He Himself may in all things occupy the foremost place.
19 Pakuti kunamukomera Mulungu kuti umulungu wake wonse ukhalemo mwa Khristu.
For it was the Father's gracious will that the whole of the divine perfections should dwell in Him.
20 Ndipo kudzera mwa Iye Mulungu ayanjanitsenso zinthu zonse ndi Iye mwini, zinthu za pa dziko lapansi, kapena zinthu za kumwamba. Iye anachita mtendere kudzera mʼmagazi ake, wokhetsedwa pa mtanda.
And God purposed through Him to reconcile the universe to Himself, making peace through His blood, which was shed upon the Cross--to reconcile to Himself through Him, I say, things on earth and things in Heaven.
21 Kale inu munali kutali ndi Mulungu ndipo munali adani a Mulungu mʼmaganizo mwanu chifukwa cha khalidwe lanu loyipa.
And you, estranged as you once were and even hostile in your minds, amidst your evil deeds,
22 Koma tsopano Iye anakuyanjanitsani mʼthupi la Khristu kudzera mu imfa kuti akuperekeni pamaso pake oyera, opanda banga ndi opanda chotsutsidwa nacho
He has now, in His human body, reconciled to God by His death, to bring you, holy and faultless and irreproachable, into His presence;
23 ngati mupitirirabe kukhala mʼchikhulupiriro chanu, okhazikika ndi olimba, osasunthidwa kuchoka pa chiyembekezo chimene munachigwira mu Uthenga Wabwino. Uwu ndi Uthenga Wabwino umene munawumva, umene wakhala ukulalikidwa kwa olengedwa onse a pansi pa thambo, ndi umenenso, ine Paulo ndinakhala mtumiki wake.
if, indeed, you are still firmly holding to faith as your foundation, without ever shifting from your hope that rests on the Good News that you have heard, which has been proclaimed in the whole creation under Heaven, and in which I Paul have been appointed to serve.
24 Tsopano ine ndikukondwa kuti ndinavutika chifukwa cha inu, ndipo ndikukwaniritsa mʼthupi langa zimene zikuperewera pa masautso a Khristu, chifukwa cha thupi lake, limene ndi Mpingo.
Now I can find joy amid my sufferings for you, and I fill up in my own person whatever is lacking in Christ's afflictions on behalf of His Body, the Church.
25 Ine ndakhala mtumiki wake mwa lamulo limene Mulungu anandipatsa kuti ndipereke Mawu a Mulungu athunthu,
I have been appointed to serve the Church in the position of responsibility entrusted to me by God for your benefit, so that I may fully deliver God's Message--
26 chinsinsi chimene chakhala chikubisika kwa nthawi ndi mibado, koma tsopano chawululidwa kwa oyera mtima. (aiōn g165)
the truth which has been kept secret from all ages and generations, but has now been revealed to His people, (aiōn g165)
27 Kwa iwo amene Mulungu anawasankha kuti awadziwitse pakati pa a mitundu ina, ulemerero wa chuma cha chinsinsi ichi, amene ndi Khristu mwa inu, chiyembekezo cha ulemerero.
to whom it was His will to make known how vast a wealth of glory for the Gentile world is implied in this truth--the truth that 'Christ is in you, the hope of glory.'
28 Ife tikulalikira Khristu, kulangiza ndi kuphunzitsa aliyense mwa nzeru zonse kuti timupereke aliyense wangwiro mwa Khristu.
Him we preach, admonishing every one and instructing every one, with all possible wisdom, so that we may bring every one into God's presence, made perfect through Christ.
29 Ndi cholinga chimenechi, ine ndikugwira ntchito molimbika ndi mwamphamvu zonse zimene Iye anachita mwa ine.
To this end, like an earnest wrestler, I exert all my strength in reliance upon the power of Him who is mightily at work within me.

< Akolose 1 >