< Akolose 3 >

1 Tsono popeza munaukitsidwa pamodzi ndi Khristu, ikani mitima yanu pa zinthu za kumwamba, kumene Khristu akukhala ku dzanja lamanja la Mulungu.
Si donc vous avez été ressuscités avec le Christ, cherchez les choses d'en haut, où est le Christ, assis à la droite de Dieu.
2 Muzifunafuna zinthu za kumwamba, osati zinthu za pa dziko lapansi.
Fixez vos pensées sur les choses d'en haut, et non sur celles qui sont sur la terre.
3 Pakuti munafa, ndipo moyo wanu tsopano wabisika pamodzi ndi Khristu mwa Mulungu.
Car vous êtes morts, et votre vie est cachée avec le Christ en Dieu.
4 Khristu, amene ndiye moyo wanu, akadzaonekanso, pamenepo inunso mudzaoneka naye pamodzi mu ulemerero.
Quand le Christ, notre vie, paraîtra, vous paraîtrez aussi avec lui dans la gloire.
5 Choncho, iphani zilakolako za dziko lapansi mwa inu, monga: dama, zodetsa, kulakalaka zosayenera, kukhumba zoyipa ndi umbombo, pakuti umbombo ndiko kupembedza mafano.
Faites donc mourir vos membres qui sont sur la terre: l'immoralité sexuelle, l'impureté, la passion dépravée, le mauvais désir, la cupidité, qui est une idolâtrie.
6 Chifukwa cha zimenezi, mkwiyo wa Mulungu ukubwera pa ana osamvera.
C'est à cause de ces choses que la colère de Dieu vient sur les enfants de la désobéissance.
7 Inunso kale munkachita zomwezi, mʼmoyo wanu wakale uja.
Vous aussi, vous avez marché autrefois dans ces choses, quand vous viviez dans ces choses-là,
8 Koma tsopano mukuyenera kuzichotsa zinthu zonsezi monga: mkwiyo, ukali, dumbo, chipongwe ndi mawu onyansa.
mais maintenant il faut les rejeter toutes: la colère, l'emportement, la malice, la calomnie, et les paroles honteuses qui sortent de votre bouche.
9 Musanamizane wina ndi mnzake, popeza munavula munthu wakale pamodzi ndi zochita zake
Ne vous mentez pas les uns aux autres, puisque vous avez dépouillé le vieil homme et ses actions,
10 ndipo mwavala munthu watsopano, amene nzeru zake zikukonzedwanso kuti afanane ndi Mlengi wake.
et que vous avez revêtu l'homme nouveau, qui se renouvelle dans la connaissance, à l'image de son Créateur,
11 Pano palibe kusiyana pakati pa Mgriki ndi Myuda, wochita mdulidwe ndi wosachita, wosaphunzira kapena wosachangamuka, kapolo kapena mfulu, koma Khristu yekha basi ndipo amakhala mwa onse.
où il n'y a ni Grec ni Juif, ni circoncis ni incirconcis, ni barbare ni Scythe, ni esclave ni homme libre, mais où Christ est tout et en tous.
12 Choncho, ngati anthu osankhidwa ndi Mulungu, oyera mtima ndi okondedwa kwambiri, muvale chifundo, kukoma mtima, kudzichepetsa, kufatsa ndi kupirira.
Revêtez-vous donc, comme des élus de Dieu, saints et bien-aimés, d'un cœur de compassion, de bonté, de modestie, d'humilité et de persévérance;
13 Mulezerane mtima ndipo muzikhululukirana ngati wina ali ndi chifukwa ndi mnzake. Muzikhululukirana monga Ambuye anakhululukira inu.
supportez-vous les uns les autres, et pardonnez-vous mutuellement, si quelqu'un a quelque chose à se reprocher; comme Christ vous a pardonné, faites-le vous aussi.
14 Ndipo kuwonjezera pa zonsezi valani chikondi, chimene chimangirira zonsezi pamodzi mu mgwirizano wangwiro.
Par-dessus toutes ces choses, marchez dans l'amour, qui est le lien de la perfection.
15 Mtendere wa Khristu ulamulire mʼmitima mwanu, popeza monga ziwalo za thupi limodzi, munayitanidwa kuti mukhale ndi mtendere. Ndipo muziyamika.
Et que la paix de Dieu règne dans vos cœurs, à laquelle vous avez aussi été appelés en un seul corps, et soyez reconnaissants.
16 Mawu a Khristu akhazikike kwathunthu mʼmitima mwanu. Muziphunzitsana ndi kulangizana wina ndi mnzake ndi nzeru zonse pamene mukuyimba Masalimo, nyimbo zotamanda ndi nyimbo zauzimu, kuyimbira Mulungu ndi mitima yoyamika.
Que la parole de Christ habite richement en vous; en toute sagesse, enseignez-vous et exhortez-vous les uns les autres par des psaumes, des hymnes et des chants spirituels, en chantant au Seigneur avec grâce dans votre cœur.
17 Ndipo chilichonse chimene mungachite, kaya nʼkuyankhula, kaya nʼkugwira ntchito, muchite zonse mʼdzina la Ambuye Yesu, kuyamika kwa Mulungu Atate kudzera mwa Iye.
Quoi que vous fassiez, en paroles ou en actes, faites tout au nom du Seigneur Jésus, en rendant par lui des actions de grâces à Dieu le Père.
18 Inu akazi, gonjerani amuna anu, monga kuyenera mwa Ambuye.
Femmes, soyez soumises à vos maris, comme il convient dans le Seigneur.
19 Inu amuna, kondani akazi anu ndipo musawapsere mtima.
Maris, aimez vos femmes, et ne vous aigrissez pas contre elles.
20 Inu ana, mverani makolo anu mu zonse pakuti izi zimakondweretsa Ambuye.
Enfants, obéissez en toutes choses à vos parents, car cela plaît au Seigneur.
21 Inu abambo, musakwiyitse ana anu, kuti angataye mtima.
Pères, ne provoquez pas vos enfants, afin qu'ils ne se découragent pas.
22 Inu antchito, mverani mabwana anu mu zonse, ndipo muzichita zimenezi osati nthawi yokhayo imene akukuonani kuti akukondeni, koma muzichite moona mtima ndi mopereka ulemu kwa Ambuye.
Serviteurs, obéissez en toutes choses à ceux qui sont vos maîtres selon la chair, non pas seulement quand ils regardent, comme pour plaire aux hommes, mais dans la simplicité du cœur, en craignant Dieu.
23 Chilichonse mungachite, muchite ndi mtima wanu onse, monga mmene mungagwirire ntchito ya Ambuye osati ya anthu.
Et quoi que vous fassiez, travaillez de bon cœur, comme pour le Seigneur et non pour des hommes,
24 Inu mukudziwa kuti mudzalandira mphotho monga cholowa kuchokera kwa Ambuye. Ndi Ambuye Khristu amene mukumutumikira.
sachant que vous recevrez du Seigneur la récompense de l'héritage; car vous servez le Seigneur Christ.
25 Aliyense amene amachita zolakwa adzalandira malipiro molingana ndi kulakwa kwake, ndipo palibe tsankho.
Mais celui qui fait le mal recevra de nouveau pour le mal qu'il a fait, et il n'y a pas de partialité.

< Akolose 3 >