< Akolose 1 >

1 Paulo, mtumwi wa Khristu Yesu mwachifuniro cha Mulungu, ndi Timoteyo mʼbale wathu.
Paul, apôtre de Jésus-Christ par la volonté de Dieu, et Timothée, notre frère,
2 Kulembera abale oyera mtima ndi okhulupirira a ku Kolose mwa Khristu. Chisomo ndi mtendere kwa inu zochokera kwa Mulungu Atate athu.
aux saints et fidèles frères en Christ qui sont à Colosses: Grâce et paix à vous de la part de Dieu notre Père et du Seigneur Jésus-Christ.
3 Timayamika Mulungu Atate wa Ambuye athu Yesu Khristu, nthawi zonse pamene tikukupemphererani.
Nous rendons grâces à Dieu, le Père de notre Seigneur Jésus-Christ, en priant toujours pour vous,
4 Timayamika chifukwa tinamva za chikhulupiriro chanu mwa Khristu Yesu ndi za chikondi chanu pa oyera mtima onse.
ayant entendu parler de votre foi en Jésus-Christ et de l'amour que vous avez pour tous les saints,
5 Chikhulupiriro ndi chikondi, gwero lake ndi chiyembekezo chomwe muli nacho chodzalandira zimene anakusungirani kumwamba. Munamva kale za zimenezi kudzera mʼmawu a choonadi, Uthenga Wabwino
à cause de l'espérance qui vous est réservée dans les cieux, et dont vous avez entendu parler auparavant dans la parole de vérité de la Bonne Nouvelle
6 umene unafika kwa inu. Pa dziko lonse lapansi Uthenga Wabwino ukubereka chipatso ndi kukula monga momwe zakhala zikuchitikira pakati panu kuyambira tsiku limene munawumva ndi kuzindikira chisomo cha Mulungu mu choonadi chonse.
qui vous est parvenue, comme elle est dans le monde entier, et qu'elle porte du fruit et croît, comme elle croît aussi en vous, depuis le jour où vous avez entendu et connu la grâce de Dieu dans la vérité,
7 Inu munaphunzira zimenezi kuchokera kwa Epafra, mtumiki mnzathu wokondedwa, amene ndi mtumiki wokhulupirika wa Khristu mʼmalo mwathu.
ainsi que vous l'avez appris d'Épaphras, notre bien-aimé compagnon de service, fidèle serviteur de Christ en votre faveur,
8 Iye anatiwuza za chikondi chanu chimene Mzimu anakupatsani.
qui nous a aussi déclaré votre amour dans l'Esprit.
9 Chifukwa cha ichi, kuyambira tsiku limene tinamva za inu, sitinasiye kukupemphererani ndi kumupempha Mulungu kuti akudzazeni ndi chidziwitso cha chifuniro chake kudzera mu nzeru yonse yauzimu ndi kumvetsetsa.
C'est pourquoi, nous aussi, depuis le jour où nous l'avons appris, nous ne cessons de prier et de demander pour vous, afin que vous soyez remplis de la connaissance de sa volonté en toute sagesse et intelligence spirituelles,
10 Ndipo tikupempherera zimenezi ndi cholinga chakuti inu mukhale moyo oyenera Ambuye ndi kumukondweretsa mʼnjira zonse. Kubereka chipatso pa ntchito iliyonse yabwino, ndi kukula mʼchidziwitso cha Mulungu.
afin que vous marchiez d'une manière digne du Seigneur, pour lui plaire à tous égards, portant du fruit en toute bonne œuvre et croissant dans la connaissance de Dieu,
11 Timapempheranso kuti Mulungu akulimbikitseni ndi mphamvu yake yonse ya ulemerero wake, kuti muzipirira zonse ndi mitima yofatsa ndi ya chimwemwe
fortifiés de toute puissance, selon la puissance de sa gloire, pour toute endurance et persévérance dans la joie,
12 ndi kuyamika Atate nthawi zonse, amene wakuyenerezani kuti mulandire nawo chuma cha oyera mtima mu ufumu wa kuwunika.
en rendant grâces au Père, qui nous a rendus aptes à participer à l'héritage des saints dans la lumière,
13 Pakuti Iye anatipulumutsa ku ulamuliro wa mdima ndi kutibweretsa mu ufumu wa Mwana wake wokondedwa.
qui nous a délivrés de la puissance des ténèbres et nous a transportés dans le royaume du Fils de son amour,
14 Mwa Iyeyu ife tinawomboledwa ndi kukhululukidwa machimo.
en qui nous avons notre rédemption, le pardon de nos péchés.
15 Mwanayu ndiye chithunzi cha Mulungu wosaonekayo. Iye ndiye Mwana wake woyamba kubadwa ndi wolamulira zolengedwa zonse.
Il est l'image du Dieu invisible, le premier-né de toute la création.
16 Pakuti zinthu zonse zinalengedwa kudzera mwa Iye. Zinthu zakumwamba ndi za pa dziko lapansi, zooneka ndi zosaoneka, maufumu, akuluakulu, aulamuliro ndi amphamvu. Zinthu zonse zinalengedwa kudzera mwa Iye ndipo anazilengera Iyeyo.
Car par lui tout a été créé dans les cieux et sur la terre, les choses visibles et les choses invisibles, qu'il s'agisse de trônes, de dominations, de principautés ou de pouvoirs. Toutes choses ont été créées par lui et pour lui.
17 Iyeyo analipo zinthu zonse zisanalengedwe ndipo zinthu zonse zimamangika pamodzi mwa Iye.
Il est avant toutes choses, et toutes choses subsistent en lui.
18 Iye ndiyenso mutu wa thupi, limene ndi mpingo. Iye ndiye chiyambi chake, woyamba kuuka kwa akufa, kuti Iyeyo akhale wopambana zonse.
Il est la tête du corps, de l'assemblée, lui qui est le commencement, le premier-né d'entre les morts, afin d'avoir en toutes choses la prééminence.
19 Pakuti kunamukomera Mulungu kuti umulungu wake wonse ukhalemo mwa Khristu.
Car il a plu à toute la plénitude d'habiter en lui,
20 Ndipo kudzera mwa Iye Mulungu ayanjanitsenso zinthu zonse ndi Iye mwini, zinthu za pa dziko lapansi, kapena zinthu za kumwamba. Iye anachita mtendere kudzera mʼmagazi ake, wokhetsedwa pa mtanda.
et de réconcilier par lui toutes choses avec lui-même, tant celles qui sont sur la terre que celles qui sont dans les cieux, ayant établi la paix par le sang de sa croix.
21 Kale inu munali kutali ndi Mulungu ndipo munali adani a Mulungu mʼmaganizo mwanu chifukwa cha khalidwe lanu loyipa.
Vous qui, autrefois, étiez aliénés et ennemis dans votre esprit par vos mauvaises actions,
22 Koma tsopano Iye anakuyanjanitsani mʼthupi la Khristu kudzera mu imfa kuti akuperekeni pamaso pake oyera, opanda banga ndi opanda chotsutsidwa nacho
il vous a maintenant réconciliés par la mort dans le corps de sa chair, afin de vous présenter saints, irréprochables et sans défaut devant lui,
23 ngati mupitirirabe kukhala mʼchikhulupiriro chanu, okhazikika ndi olimba, osasunthidwa kuchoka pa chiyembekezo chimene munachigwira mu Uthenga Wabwino. Uwu ndi Uthenga Wabwino umene munawumva, umene wakhala ukulalikidwa kwa olengedwa onse a pansi pa thambo, ndi umenenso, ine Paulo ndinakhala mtumiki wake.
si du moins vous persévérez dans la foi, fondés et inébranlables, sans vous détourner de l'espérance de la Bonne Nouvelle que vous avez entendue et qui est proclamée dans toute la création sous le ciel, dont moi, Paul, j'ai été fait serviteur.
24 Tsopano ine ndikukondwa kuti ndinavutika chifukwa cha inu, ndipo ndikukwaniritsa mʼthupi langa zimene zikuperewera pa masautso a Khristu, chifukwa cha thupi lake, limene ndi Mpingo.
Or, je me réjouis de mes souffrances à cause de vous, et je comble de mon côté ce qui manque aux souffrances de Christ dans ma chair, pour l'amour de son corps, qui est l'assemblée,
25 Ine ndakhala mtumiki wake mwa lamulo limene Mulungu anandipatsa kuti ndipereke Mawu a Mulungu athunthu,
dont j'ai été fait serviteur selon l'office de Dieu qui m'a été confié envers vous pour l'accomplissement de la parole de Dieu,
26 chinsinsi chimene chakhala chikubisika kwa nthawi ndi mibado, koma tsopano chawululidwa kwa oyera mtima. (aiōn g165)
mystère caché depuis des siècles et des générations. Mais maintenant il a été révélé à ses saints, (aiōn g165)
27 Kwa iwo amene Mulungu anawasankha kuti awadziwitse pakati pa a mitundu ina, ulemerero wa chuma cha chinsinsi ichi, amene ndi Khristu mwa inu, chiyembekezo cha ulemerero.
à qui Dieu a voulu faire connaître quelle est la richesse de la gloire de ce mystère parmi les païens, qui est le Christ en vous, l'espérance de la gloire.
28 Ife tikulalikira Khristu, kulangiza ndi kuphunzitsa aliyense mwa nzeru zonse kuti timupereke aliyense wangwiro mwa Khristu.
Nous l'annonçons, en exhortant tout homme et en l'instruisant en toute sagesse, afin de rendre tout homme parfait en Jésus-Christ.
29 Ndi cholinga chimenechi, ine ndikugwira ntchito molimbika ndi mwamphamvu zonse zimene Iye anachita mwa ine.
C'est à quoi je m'efforce, moi aussi, selon son opération qui agit puissamment en moi.

< Akolose 1 >