< Amosi 1 >

1 Mawu a Amosi, mmodzi mwa anthu oweta nkhosa ku Tekowa. Zimene iye anaona mʼmasomphenya zokhudza Israeli patatsala zaka ziwiri kuti chivomerezi chichitike, nthawi imene Uziya anali mfumu ya Yuda ndipo Yeroboamu mwana wa Yowasi anali mfumu ya Israeli.
Słowa Amosa, który był [jednym] spośród pasterzy z Tekoa, które widział o Izraelu za dni Uzjasza, króla Judy, i za dni Jeroboama, syna Joasza, króla Izraela, dwa lata przed trzęsieniem ziemi.
2 Amosi anati: “Yehova akubangula mu Ziyoni ndipo akumveka ngati bingu mu Yerusalemu; msipu wa abusa ukulira, ndipo pamwamba pa Karimeli pakuwuma.”
I powiedział: PAN zagrzmi z Syjonu, z Jerozolimy wyda swój głos; mieszkania pasterzy będą lamentować, a wyschnie szczyt Karmelu.
3 Yehova akuti, “Chifukwa anthu a ku Damasiko akunka nachimwirachimwira, Ine sindileka kuwalanga. Popeza anapuntha Giliyadi ndi zopunthira za mano achitsulo,
Tak mówi PAN: Z powodu trzech występków Damaszku i z powodu czterech nie przepuszczę mu, ponieważ młócili Gilead narzędziami z żelaza.
4 Ine ndidzatumiza moto pa nyumba ya Hazaeli umene udzanyeketsa nyumba zaufumu za Beni-Hadadi.
Ale ześlę ogień na dom Chazaela, który strawi pałace Ben-Hadada.
5 Ndidzathyola chipata cha Damasiko; ndidzawononga mfumu yokhala ku Chigwa cha Aveni, ndiponso iye amene akugwira ndodo yaufumu mu Beti-Edeni. Anthu a ku Aramu adzapita ku ukapolo ku Kiri,” akutero Yehova.
Połamię też rygiel Damaszku i wykorzenię mieszkańca z doliny Awen i tego, który trzyma berło z domu Eden. I lud Syrii pójdzie do niewoli do Kir, mówi PAN.
6 Yehova akuti, “Chifukwa anthu a ku Gaza akunka nachimwirachimwira, Ine sindileka kuwalanga. Popeza anatenga ukapolo mtundu wathunthu ndi kuwugulitsa ku Edomu,
Tak mówi PAN: Z powodu trzech występków Gazy i z powodu czterech nie przepuszczę im, ponieważ uprowadzili wszystkich jeńców, aby ich wydać Edomowi.
7 ndidzatumiza moto pa makoma a Gaza umene udzanyeketsa nyumba zake zaufumu.
Ale ześlę ogień na mur Gazy, który strawi jej pałace.
8 Ndidzawononga mfumu ya ku Asidodi komanso amene akugwira ndodo yaufumu ku Asikeloni. Ndidzalanga Ekroni, mpaka wotsala mwa Afilisti atafa,” akutero Ambuye Yehova.
Wykorzenię też mieszkańca z Aszdodu i tego, który trzyma berło z Aszkelonu, i zwrócę swoją rękę przeciwko Ekronowi, i zginie resztka Filistynów, mówi Pan BÓG.
9 Yehova akuti, “Chifukwa anthu a ku Turo akunka nachimwirachimwira, Ine sindileka kuwalanga. Popeza iwo anagulitsa mtundu wathunthu ku ukapolo ku Edomu, osasunga pangano laubale lija,
Tak mówi PAN: Z powodu trzech występków Tyru i z powodu czterech nie przepuszczę mu, ponieważ wydali wszystkich jeńców Edomowi, a nie pamiętali o braterskim przymierzu;
10 Ine ndidzatumiza moto pa makoma a Turo umene udzanyeketsa nyumba zake zaufumu.”
Ale ześlę ogień na mur Tyru, który strawi jego pałace.
11 Yehova akuti, “Chifukwa anthu a ku Edomu akunka nachimwirachimwira, Ine sindileka kuwalanga. Popeza anathamangitsa mʼbale wake ndi lupanga, popanda nʼchifundo chomwe. Popeza mkwiyo wake unakulabe ndipo ukali wake sunatonthozeke,
Tak mówi PAN: Z powodu trzech występków Edomu i z powodu czterech nie przepuszczę mu, ponieważ prześladował mieczem swego brata, tłumiąc w sobie wszelaką litość, a nieustannie pałał gniewem, swoją zapalczywość chował na zawsze.
12 Ine ndidzatumiza moto pa Temani umene udzanyeketsa nyumba zaufumu za Bozira.”
Ale ześlę ogień na Teman i strawi pałace Bosry.
13 Yehova akuti, “Chifukwa anthu a ku Amoni akunka nachimwirachimwira, Ine sindileka kuwalanga. Popeza anatumbula akazi oyembekezera a ku Giliyadi nʼcholinga choti akuze malire awo,
Tak mówi PAN: Z powodu trzech występków synów Ammona i z powodu czterech nie przepuszczę im, ponieważ rozcinali brzemienne w Gileadzie tylko po to, by rozszerzyć swoje granice.
14 Ine ndidzayatsa moto pa makoma a ku Raba umene udzanyeketsa nyumba zake zaufumu. Padzakhala kulira kwakukulu pa tsiku la nkhondoyo, kumenyana kudzakhala kwafumbi ngati mkuntho wa kamvuluvulu.
Ale rozniecę ogień na murze Rabby, który strawi jego pałace wśród krzyku w dzień bitwy, podczas wichru w dzień burzy.
15 Mfumu yawo idzatengedwa kupita ku ukapolo, iyo pamodzi ndi akuluakulu ake,” akutero Yehova.
I pójdzie ich król do niewoli, on i jego książęta razem z nim, mówi PAN.

< Amosi 1 >