< Amosi 9 >

1 Ine ndinaona Ambuye atayima pambali pa guwa lansembe, ndipo anati: “Kantha mitu ya nsanamira kuti ziwundo za nyumba zigwedezeke. Muzigwetsere pa mitu ya anthu onse, onse amene atsalira ndidzawapha ndi lupanga. Palibe ndi mmodzi yemwe amene adzathawe, palibe amene adzapulumuke.
Mihuu Awurade sɛ ogyina afɔremuka no ho, na ɔkae se, “Bɔ Asɔredan no afadum no atifi na mma ne fapem no nwosow. Munnwiriw ngu nnipa no nyinaa so; wɔn a aka no mede afoa bekunkum wɔn. Ɔbaako mpo rentumi nguan, obiara rennya ne ho sɔnn.
2 Ngakhale atakumba pansi mpaka ku malo a anthu akufa, dzanja langa lidzawatulutsa kumeneko. Ngakhale atakwera kumwamba Ine ndidzawatsakamutsa kumeneko. (Sheol h7585)
Mpo sɛ wotu fam kɔ ɔda mu a, hɔ na me nsa bɛtwe wɔn afi aba. Mpo sɛ wɔforo kɔ ɔsoro a, hɔ na meyi wɔn afi aba fam. (Sheol h7585)
3 Ngakhale atakabisala pamwamba pa phiri la Karimeli, Ine ndidzawasaka kumeneko ndi kuwagwira. Ngakhale atakabisala pansi pa nyanja yayikulu, ndidzalamula njoka kuti iwalume kumeneko.
Mpo sɛ wɔkɔtetɛw bepɔw Karmel atifi a, hɔ na metiw wɔn akɔkyere wɔn aba. Mpo sɛ wɔde wɔn ho sie me wɔ po ase a, hɔ na mɛhyɛ ɔwɔ no ama wakɔkeka wɔn.
4 Ngakhale adani awo awakusire ku ukapolo, ndidzalamula lupanga kuti liwaphe kumeneko. Ndidzawayangʼanitsitsa kuti zoyipa ziwagwere; osati zabwino.”
Mpo sɛ wɔn atamfo de wɔn kɔ nnommum mu a, hɔ na mɛhyɛ afoa akunkum wɔn. “Megyen mʼani ahwɛ wɔn. Mede ɔsɛe bɛba wɔn so na meremmoa wɔn.”
5 Ambuye Yehova Wamphamvuzonse amene amakhudza dziko lapansi ndipo dzikolo limasungunuka, onse amene amakhala mʼmenemo amalira. Dziko lonse lidzadzaza ngati mtsinje wa Nailo, kenaka nʼkuphwera ngati mtsinje wa ku Igupto.
Awurade, Asafo Awurade, Ɔno na ɔde ne nsa ka asase ma ɛnan, ma wɔn a wɔte so nyinaa twa adwo. Asase no nyinaa ma ne ho so te sɛ Nil na ɛtwe te sɛ Misraim asubɔnten.
6 Iye amene amamanga malo ake okhalamo kumwamba, ndi kuyika maziko ake pa dziko lapansi, Iye amene amayitana madzi a ku nyanja ndikuwakhuthulira pa dziko lapansi, dzina lake ndiye Yehova.
Ɔno na osi nʼahemfi a ɛkorɔn wɔ ɔsoro na ɔto ne fapem wɔ asase so. Ɔno na ɔboaboa po mu nsu ano na ohwie gu asase so. Awurade ne ne din!
7 “Kodi kwa Ine, inu Aisraeli, simuli chimodzimodzi ndi Akusi?” Akutero Yehova. “Kodi sindine amene ndinatulutsa Israeli ku Igupto, Afilisti ku Kafitori ndi Aaramu ku Kiri?
“Mo Israelfo, mo ho hia me sen Etiopiafo?” Sɛnea Awurade se ni. Manyi Israelfo amfi Misraim, ne Filistifo amfi Kaftor, ne Aramfo nso amfi Kir ana?
8 “Taonani, maso a Ambuye Yehova ali pa ufumu wochimwawu. Ndidzawufafaniza pa dziko lapansi. Komabe sindidzawononga kotheratu nyumba ya Yakobo,” akutero Yehova.
“Ampa ara Otumfo Awurade ani wɔ nnebɔne ahenni no so. Mɛpepa no afi asase ani, nanso merensɛe Yakobfi korakora,” sɛnea Awurade se ni.
9 “Pakuti ndidzalamula, ndipo ndidzagwedeza nyumba ya Israeli pakati pa mitundu yonse ya anthu monga momwe amasefera ufa mʼsefa, koma palibe nʼkamwala kamodzi komwe kamene kadzagwe pansi.
“Na mɛhyɛ, na mɛwosow Israelfi, wɔ amanaman nyinaa mu, sɛnea wohuhuw atoko so wɔ huhuamoa mu na aba fua mpo ntɔ fam no.
10 Anthu onse ochimwa pakati pa anthu anga adzaphedwa ndi lupanga, onse amene amanena kuti, ‘Tsoka silidzatigwera ife kapena kutiwononga.’
Nnebɔneyɛfo a wɔwɔ me nkurɔfo mu nyinaa bɛtotɔ wɔ afoa ano, wɔn a wɔka se, ‘Amanehunu rento yɛn anaa ɛremma yɛn so da no.’
11 “Tsiku limenelo ndidzabwezeretsa nyumba ya Davide imene inagwa. Ndidzakonzanso malo amene anagumuka, ndi kuyimanganso monga inalili poyamba,
“Saa da no, mɛsan aba abesi “Dawid fi a abubu no bio. Mesiesie ne mmeae a asɛesɛe no, na masi no sɛnea na ɛte no,
12 kuti adzatengenso otsala a Edomu ndi mitundu yonse imene imatchedwa ndi dzina langa,” akutero Yehova amene adzachita zinthu izi.
na wɔafa Edom nkae no ne amanaman a me din da wɔn so.” Awurade a waka no, ɔno na ɔbɛyɛ eyinom nyinaa.
13 Yehova akunena kuti “Nthawi ikubwera pamene mlimi wotipula adzapyola wokolola ndipo woponda mphesa adzapyola wodzala mbewu. Mapiri adzachucha vinyo watsopano ndi kuyenderera pa zitunda zonse.
“Nna no reba,” sɛnea Awurade se ni, “A nnɔbae no bɛba ntɛm ama otwafo no, na bobe no abu so ama nea otiatia nsakyiamoa no so no. Nsa foforo bɛsosɔ afi mmepɔw no so na ateɛ afi nkoko no nyinaa so.
14 Ndidzawabwezeranso pabwino anthu anga Aisraeli; mizinda imene inali mabwinja idzamangidwanso ndipo azidzakhalamo. Adzalima minda ya mpesa ndipo adzamwa vinyo wake; adzalima minda ndipo adzadya zipatso zake.
Mede me nkurɔfo Israel nnommum bɛsan aba. “Wɔbɛsan asiesie nkuropɔn a asɛe no na wɔatena mu. Wɔbɛyɛ bobe nturo na wɔanom mu nsa; wɔbɛyɛ mfikyifuw na wɔadi so nnuaba.
15 Ndidzakhazika Aisraeli mʼdziko mwawo, ndipo sadzachotsedwamonso mʼdziko limene Ine ndawapatsa,” akutero Yehova Mulungu wako.
Mede Israelfo bedua wɔn ankasa asase so a wɔrentu bio da mfi asase a mede ama wɔn no so,” sɛnea Awurade, mo Nyankopɔn se ni.

< Amosi 9 >