< Amosi 9 >

1 Ine ndinaona Ambuye atayima pambali pa guwa lansembe, ndipo anati: “Kantha mitu ya nsanamira kuti ziwundo za nyumba zigwedezeke. Muzigwetsere pa mitu ya anthu onse, onse amene atsalira ndidzawapha ndi lupanga. Palibe ndi mmodzi yemwe amene adzathawe, palibe amene adzapulumuke.
Jeg så Herren stå ved alteret, og han sa: Slå til søilehodene, så dørtersklene skjelver, og knus dem, så de faller ned over hodet på dem alle! Den siste levning av dem vil jeg drepe med sverdet; ingen av dem skal kunne undfly, ingen av dem komme unda.
2 Ngakhale atakumba pansi mpaka ku malo a anthu akufa, dzanja langa lidzawatulutsa kumeneko. Ngakhale atakwera kumwamba Ine ndidzawatsakamutsa kumeneko. (Sheol h7585)
Om de bryter sig inn i dødsriket, så skal min hånd hente dem derfra, og om de farer op til himmelen, skal jeg styrte dem ned derfra; (Sheol h7585)
3 Ngakhale atakabisala pamwamba pa phiri la Karimeli, Ine ndidzawasaka kumeneko ndi kuwagwira. Ngakhale atakabisala pansi pa nyanja yayikulu, ndidzalamula njoka kuti iwalume kumeneko.
om de skjuler sig på Karmels topp, skal jeg lete dem op og hente dem derfra, og om de gjemmer sig for mine øine på havets bunn, skal jeg kalle ormen frem, og den skal bite dem,
4 Ngakhale adani awo awakusire ku ukapolo, ndidzalamula lupanga kuti liwaphe kumeneko. Ndidzawayangʼanitsitsa kuti zoyipa ziwagwere; osati zabwino.”
og om de føres i fangenskap av sine fiender, skal jeg der byde sverdet å slå dem ihjel; jeg skal la mitt øie hvile på dem, til det onde og ikke til det gode.
5 Ambuye Yehova Wamphamvuzonse amene amakhudza dziko lapansi ndipo dzikolo limasungunuka, onse amene amakhala mʼmenemo amalira. Dziko lonse lidzadzaza ngati mtsinje wa Nailo, kenaka nʼkuphwera ngati mtsinje wa ku Igupto.
Og Herren, Israels Gud, hærskarenes Gud, han rører ved jorden, da smelter den, og alle som bor på den, sørger, og hele jorden hever sig som Nilen og faller som Egyptens elv,
6 Iye amene amamanga malo ake okhalamo kumwamba, ndi kuyika maziko ake pa dziko lapansi, Iye amene amayitana madzi a ku nyanja ndikuwakhuthulira pa dziko lapansi, dzina lake ndiye Yehova.
Han har bygget sine høie saler i himmelen og grunnfestet sin hvelving over jorden, han kaller på havets vann og øser dem ut over jorden; Herren er hans navn.
7 “Kodi kwa Ine, inu Aisraeli, simuli chimodzimodzi ndi Akusi?” Akutero Yehova. “Kodi sindine amene ndinatulutsa Israeli ku Igupto, Afilisti ku Kafitori ndi Aaramu ku Kiri?
Er I mere verd for mig enn etiopernes barn, I Israels barn? sier Herren; har jeg ikke ført Israel op fra Egyptens land og filistrene fra Kaftor og syrerne fra Kir?
8 “Taonani, maso a Ambuye Yehova ali pa ufumu wochimwawu. Ndidzawufafaniza pa dziko lapansi. Komabe sindidzawononga kotheratu nyumba ya Yakobo,” akutero Yehova.
Se, Herrens, Israels Guds øine er vendt mot dette syndige rike, og jeg vil utslette det av jorden; men jeg vil ikke aldeles utslette Jakobs hus, sier Herren.
9 “Pakuti ndidzalamula, ndipo ndidzagwedeza nyumba ya Israeli pakati pa mitundu yonse ya anthu monga momwe amasefera ufa mʼsefa, koma palibe nʼkamwala kamodzi komwe kamene kadzagwe pansi.
For se, jeg byder at Israels ætt skal rystes blandt alle folkeslag, likesom en ryster med et sold, og ikke et korn faller til jorden.
10 Anthu onse ochimwa pakati pa anthu anga adzaphedwa ndi lupanga, onse amene amanena kuti, ‘Tsoka silidzatigwera ife kapena kutiwononga.’
For mitt sverd skal de dø alle syndere blandt mitt folk, de som sier: Ulykken skal ikke nå oss eller kommer over oss.
11 “Tsiku limenelo ndidzabwezeretsa nyumba ya Davide imene inagwa. Ndidzakonzanso malo amene anagumuka, ndi kuyimanganso monga inalili poyamba,
På den dag vil jeg reise op igjen Davids falne hytte, og jeg vil mure igjen dens revner og reise op det som er nedbrutt av den, og jeg vil bygge den op igjen som i fordums dager,
12 kuti adzatengenso otsala a Edomu ndi mitundu yonse imene imatchedwa ndi dzina langa,” akutero Yehova amene adzachita zinthu izi.
så at de får ta i eie det som er igjen av Edom, og alle de hedningefolk som kalles med mitt navn, sier Herren, han som gjør dette.
13 Yehova akunena kuti “Nthawi ikubwera pamene mlimi wotipula adzapyola wokolola ndipo woponda mphesa adzapyola wodzala mbewu. Mapiri adzachucha vinyo watsopano ndi kuyenderera pa zitunda zonse.
Se, dager kommer, sier Herren, da den som pløier, skal nå den som høster, og den som trår vindruer, skal nå den som kaster ut sæden, og fjellene skal dryppe av most, og alle haugene skal flyte over.
14 Ndidzawabwezeranso pabwino anthu anga Aisraeli; mizinda imene inali mabwinja idzamangidwanso ndipo azidzakhalamo. Adzalima minda ya mpesa ndipo adzamwa vinyo wake; adzalima minda ndipo adzadya zipatso zake.
Og jeg vil gjøre ende på mitt folk Israels fangenskap, og de skal bygge op igjen de ødelagte byer og bo der og plante vingårder og drikke deres vin og dyrke op haver og ete deres frukt.
15 Ndidzakhazika Aisraeli mʼdziko mwawo, ndipo sadzachotsedwamonso mʼdziko limene Ine ndawapatsa,” akutero Yehova Mulungu wako.
Og jeg vil plante dem i deres land, og de skal aldri mere rykkes op av sitt land, det som jeg har gitt dem, sier Herren din Gud.

< Amosi 9 >