< Amosi 9 >

1 Ine ndinaona Ambuye atayima pambali pa guwa lansembe, ndipo anati: “Kantha mitu ya nsanamira kuti ziwundo za nyumba zigwedezeke. Muzigwetsere pa mitu ya anthu onse, onse amene atsalira ndidzawapha ndi lupanga. Palibe ndi mmodzi yemwe amene adzathawe, palibe amene adzapulumuke.
I saw the Lord standing upon the altar, and he said: Strike the hinges, and let the lintels be shook: for there is covetousness in the head of them all, and I will slay the last of them with the sword: there shall be no flight for them: they shall flee, and he that shall flee of them shall not be delivered.
2 Ngakhale atakumba pansi mpaka ku malo a anthu akufa, dzanja langa lidzawatulutsa kumeneko. Ngakhale atakwera kumwamba Ine ndidzawatsakamutsa kumeneko. (Sheol h7585)
Though they go down even to hell, thence shall my hand bring them out: and though they climb up to heaven, thence will I bring them down. (Sheol h7585)
3 Ngakhale atakabisala pamwamba pa phiri la Karimeli, Ine ndidzawasaka kumeneko ndi kuwagwira. Ngakhale atakabisala pansi pa nyanja yayikulu, ndidzalamula njoka kuti iwalume kumeneko.
And though they be hid in the top of Carmel, I will search and take them away from thence: and though they hide themselves from my eyes in the depth of the sea, there will I command the serpent and he shall bite them.
4 Ngakhale adani awo awakusire ku ukapolo, ndidzalamula lupanga kuti liwaphe kumeneko. Ndidzawayangʼanitsitsa kuti zoyipa ziwagwere; osati zabwino.”
And if they go into captivity before their enemies, there will I command the sword, and it shall kill them. And I will set my eyes upon them for evil, and not for good.
5 Ambuye Yehova Wamphamvuzonse amene amakhudza dziko lapansi ndipo dzikolo limasungunuka, onse amene amakhala mʼmenemo amalira. Dziko lonse lidzadzaza ngati mtsinje wa Nailo, kenaka nʼkuphwera ngati mtsinje wa ku Igupto.
And the Lord the God of hosts is he who toucheth the earth, and it shall melt: and all that dwell therein shall mourn: and it shall rise up as a river, and shall run down as the river of Egypt.
6 Iye amene amamanga malo ake okhalamo kumwamba, ndi kuyika maziko ake pa dziko lapansi, Iye amene amayitana madzi a ku nyanja ndikuwakhuthulira pa dziko lapansi, dzina lake ndiye Yehova.
He that buildeth his ascension in heaven, and hath founded his bundle upon the earth: who calleth the waters of the sea, and poureth them out upon the face of the earth, the Lord is his name.
7 “Kodi kwa Ine, inu Aisraeli, simuli chimodzimodzi ndi Akusi?” Akutero Yehova. “Kodi sindine amene ndinatulutsa Israeli ku Igupto, Afilisti ku Kafitori ndi Aaramu ku Kiri?
Are not you as the children of the Ethiopians unto me, O children of Israel, saith the Lord? did not I bring up Israel, out of the land of Egypt: and the Philistines out of Cappadocia, and the Syrians out of Cyrene?
8 “Taonani, maso a Ambuye Yehova ali pa ufumu wochimwawu. Ndidzawufafaniza pa dziko lapansi. Komabe sindidzawononga kotheratu nyumba ya Yakobo,” akutero Yehova.
Behold the eyes of the Lord God are upon the sinful kingdom, and I will destroy it from the face of the earth: but yet I will not utterly destroy the house of Jacob, saith the Lord.
9 “Pakuti ndidzalamula, ndipo ndidzagwedeza nyumba ya Israeli pakati pa mitundu yonse ya anthu monga momwe amasefera ufa mʼsefa, koma palibe nʼkamwala kamodzi komwe kamene kadzagwe pansi.
For behold I will command, and I will sift the house of Israel among all nations, as corn is sifted in a sieve: and there shall not a little stone fall to the ground.
10 Anthu onse ochimwa pakati pa anthu anga adzaphedwa ndi lupanga, onse amene amanena kuti, ‘Tsoka silidzatigwera ife kapena kutiwononga.’
All the sinners of my people shall fall by the sword: who say: The evils shall not approach, and shall not come upon us.
11 “Tsiku limenelo ndidzabwezeretsa nyumba ya Davide imene inagwa. Ndidzakonzanso malo amene anagumuka, ndi kuyimanganso monga inalili poyamba,
In that day I will raise up the tabernacle of David, that is fallen: and I will close up the breaches of the walls thereof, and repair what was fallen: and I will rebuild it as in the days of old.
12 kuti adzatengenso otsala a Edomu ndi mitundu yonse imene imatchedwa ndi dzina langa,” akutero Yehova amene adzachita zinthu izi.
That they may possess the remnant of Edom, and all nations, because my name is invoked upon them: saith the Lord that doth these things.
13 Yehova akunena kuti “Nthawi ikubwera pamene mlimi wotipula adzapyola wokolola ndipo woponda mphesa adzapyola wodzala mbewu. Mapiri adzachucha vinyo watsopano ndi kuyenderera pa zitunda zonse.
Behold the days come, saith the Lord, when the ploughman shall overtake the reaper, and the treader of grapes him that soweth seed: and the mountains shall drop sweetness, and every hill shall be tilled.
14 Ndidzawabwezeranso pabwino anthu anga Aisraeli; mizinda imene inali mabwinja idzamangidwanso ndipo azidzakhalamo. Adzalima minda ya mpesa ndipo adzamwa vinyo wake; adzalima minda ndipo adzadya zipatso zake.
And I will bring back the captivity of my people Israel: and they shall build the abandoned cities, and inhabit them: and they shall plant vineyards, and drink the wine of them: and shall make gardens, and eat the fruits of them.
15 Ndidzakhazika Aisraeli mʼdziko mwawo, ndipo sadzachotsedwamonso mʼdziko limene Ine ndawapatsa,” akutero Yehova Mulungu wako.
And I will plant them upon their own land: and I will no more pluck them out of their land which I have given them, saith the Lord thy God.

< Amosi 9 >