< Amosi 9 >

1 Ine ndinaona Ambuye atayima pambali pa guwa lansembe, ndipo anati: “Kantha mitu ya nsanamira kuti ziwundo za nyumba zigwedezeke. Muzigwetsere pa mitu ya anthu onse, onse amene atsalira ndidzawapha ndi lupanga. Palibe ndi mmodzi yemwe amene adzathawe, palibe amene adzapulumuke.
I saw the Lord standing over an altar, and he said: “Strike the hinges, and let the lintels be shaken. For there is avarice at the head of them all, and I will execute the very last of them with the sword. There will be no escape for them. They will flee, and he who flees from among them will not be saved.
2 Ngakhale atakumba pansi mpaka ku malo a anthu akufa, dzanja langa lidzawatulutsa kumeneko. Ngakhale atakwera kumwamba Ine ndidzawatsakamutsa kumeneko. (Sheol h7585)
If they descend even to the underworld, from there my hand will draw them out; and if they ascend even to the sky, from there will I pull them down. (Sheol h7585)
3 Ngakhale atakabisala pamwamba pa phiri la Karimeli, Ine ndidzawasaka kumeneko ndi kuwagwira. Ngakhale atakabisala pansi pa nyanja yayikulu, ndidzalamula njoka kuti iwalume kumeneko.
And if they were hiding at the top of Carmel, when searching there, I would steal them away, and if they conceal themselves from my eyes in the depths of the sea, I will command the serpent there and he will bite them.
4 Ngakhale adani awo awakusire ku ukapolo, ndidzalamula lupanga kuti liwaphe kumeneko. Ndidzawayangʼanitsitsa kuti zoyipa ziwagwere; osati zabwino.”
And if they go into captivity in the sight of their enemies, there I will command the sword, and it will kill them. And I will set my eyes over them for harm and not for good.”
5 Ambuye Yehova Wamphamvuzonse amene amakhudza dziko lapansi ndipo dzikolo limasungunuka, onse amene amakhala mʼmenemo amalira. Dziko lonse lidzadzaza ngati mtsinje wa Nailo, kenaka nʼkuphwera ngati mtsinje wa ku Igupto.
And the Lord God of hosts, he touches the earth and it will melt. And all who dwell in it will mourn. And everyone will rise up like a river, and will flow away like the river of Egypt.
6 Iye amene amamanga malo ake okhalamo kumwamba, ndi kuyika maziko ake pa dziko lapansi, Iye amene amayitana madzi a ku nyanja ndikuwakhuthulira pa dziko lapansi, dzina lake ndiye Yehova.
He establishes his ascension into heaven, and he has founded his bundle on the earth. He calls the waters of the ocean, and pours them over the face of the earth. The Lord is his name.
7 “Kodi kwa Ine, inu Aisraeli, simuli chimodzimodzi ndi Akusi?” Akutero Yehova. “Kodi sindine amene ndinatulutsa Israeli ku Igupto, Afilisti ku Kafitori ndi Aaramu ku Kiri?
Sons of Israel, are you not like the sons of the Ethiopians to me, says the Lord? Did I not cause Israel to rise up out of the land of Egypt, and the Philistines out of Cappadocia, and the Syrians out of Cyrene?
8 “Taonani, maso a Ambuye Yehova ali pa ufumu wochimwawu. Ndidzawufafaniza pa dziko lapansi. Komabe sindidzawononga kotheratu nyumba ya Yakobo,” akutero Yehova.
Behold, the eyes of the Lord God are on the sinning kingdom, and I will wipe it from the face of the earth. Though truly, when destroying, I will not wipe away the house of Jacob, says the Lord.
9 “Pakuti ndidzalamula, ndipo ndidzagwedeza nyumba ya Israeli pakati pa mitundu yonse ya anthu monga momwe amasefera ufa mʼsefa, koma palibe nʼkamwala kamodzi komwe kamene kadzagwe pansi.
For behold, I will command, and I will sift the house of Israel among all the nations, as wheat is sifted in a sieve. And not even one small stone will fall to the ground.
10 Anthu onse ochimwa pakati pa anthu anga adzaphedwa ndi lupanga, onse amene amanena kuti, ‘Tsoka silidzatigwera ife kapena kutiwononga.’
All the sinners of my people will die by the sword. They say, “Disaster will not come near us, and it will not overcome us.”
11 “Tsiku limenelo ndidzabwezeretsa nyumba ya Davide imene inagwa. Ndidzakonzanso malo amene anagumuka, ndi kuyimanganso monga inalili poyamba,
In that day, I will raise up the tabernacle of David, which is fallen. And I will repair the breaches in its walls, and I will restore that which collapsed. And I will rebuild it, just as in the days of antiquity,
12 kuti adzatengenso otsala a Edomu ndi mitundu yonse imene imatchedwa ndi dzina langa,” akutero Yehova amene adzachita zinthu izi.
so that they may possess the remnant of Idumea and all the nations, for my name has been invoked over them, says the Lord who does this.
13 Yehova akunena kuti “Nthawi ikubwera pamene mlimi wotipula adzapyola wokolola ndipo woponda mphesa adzapyola wodzala mbewu. Mapiri adzachucha vinyo watsopano ndi kuyenderera pa zitunda zonse.
Behold, the days pass, says the Lord, and the plower will overtake the harvester, and the treader of grapes will overtake the sower of seed. And the mountains will drip sweetness, and every hill will be cultivated.
14 Ndidzawabwezeranso pabwino anthu anga Aisraeli; mizinda imene inali mabwinja idzamangidwanso ndipo azidzakhalamo. Adzalima minda ya mpesa ndipo adzamwa vinyo wake; adzalima minda ndipo adzadya zipatso zake.
And I will turn back the captivity of my people Israel. And they will rebuild the deserted cities and inhabit them. And they will plant vineyards and drink their wine. And they will create gardens and eat their fruits.
15 Ndidzakhazika Aisraeli mʼdziko mwawo, ndipo sadzachotsedwamonso mʼdziko limene Ine ndawapatsa,” akutero Yehova Mulungu wako.
And I will plant them on their own soil. And I will no longer root them out of their own land, which I have given them, says the Lord your God.

< Amosi 9 >