< Amosi 9 >
1 Ine ndinaona Ambuye atayima pambali pa guwa lansembe, ndipo anati: “Kantha mitu ya nsanamira kuti ziwundo za nyumba zigwedezeke. Muzigwetsere pa mitu ya anthu onse, onse amene atsalira ndidzawapha ndi lupanga. Palibe ndi mmodzi yemwe amene adzathawe, palibe amene adzapulumuke.
I saw the Lord stationed by the side of the altar, giving blows to the tops of the pillars so that the doorsteps were shaking: and he said, I will let all of them be broken with earth-shocks; I will put the last of them to the sword: if any one of them goes in flight he will not get away, not one of them will be safe.
2 Ngakhale atakumba pansi mpaka ku malo a anthu akufa, dzanja langa lidzawatulutsa kumeneko. Ngakhale atakwera kumwamba Ine ndidzawatsakamutsa kumeneko. (Sheol )
Even if they go deep into the underworld, my hand will take them up from there; if they go up to heaven, I will get them down: (Sheol )
3 Ngakhale atakabisala pamwamba pa phiri la Karimeli, Ine ndidzawasaka kumeneko ndi kuwagwira. Ngakhale atakabisala pansi pa nyanja yayikulu, ndidzalamula njoka kuti iwalume kumeneko.
Though they take cover on the top of Carmel, I will go in search of them and get them out; though they keep themselves from my eyes in the bed of the sea, I will give orders to the great snake there and he will give them a bite:
4 Ngakhale adani awo awakusire ku ukapolo, ndidzalamula lupanga kuti liwaphe kumeneko. Ndidzawayangʼanitsitsa kuti zoyipa ziwagwere; osati zabwino.”
And though they are taken away as prisoners by their attackers, even there will I give orders to the sword to put them to death: my eyes will be fixed on them for evil and not for good.
5 Ambuye Yehova Wamphamvuzonse amene amakhudza dziko lapansi ndipo dzikolo limasungunuka, onse amene amakhala mʼmenemo amalira. Dziko lonse lidzadzaza ngati mtsinje wa Nailo, kenaka nʼkuphwera ngati mtsinje wa ku Igupto.
For the Lord, the God of armies, is he at whose touch the land is turned to water, and everyone in it will be given up to sorrow; all of it will be overflowing like the River, and will go down again like the River of Egypt;
6 Iye amene amamanga malo ake okhalamo kumwamba, ndi kuyika maziko ake pa dziko lapansi, Iye amene amayitana madzi a ku nyanja ndikuwakhuthulira pa dziko lapansi, dzina lake ndiye Yehova.
It is he who makes his rooms in the heaven, basing his arch on the earth; whose voice goes out to the waters of the sea, and sends them flowing over the face of the earth; the Lord is his name.
7 “Kodi kwa Ine, inu Aisraeli, simuli chimodzimodzi ndi Akusi?” Akutero Yehova. “Kodi sindine amene ndinatulutsa Israeli ku Igupto, Afilisti ku Kafitori ndi Aaramu ku Kiri?
Are you not as the children of the Ethiopians to me, O children of Israel? says the Lord. Have I not taken Israel up out of the land of Egypt, and the Philistines from Caphtor, and the Aramaeans from Kir?
8 “Taonani, maso a Ambuye Yehova ali pa ufumu wochimwawu. Ndidzawufafaniza pa dziko lapansi. Komabe sindidzawononga kotheratu nyumba ya Yakobo,” akutero Yehova.
See, the eyes of the Lord are on the evil kingdom, and I will put an end to it in all the earth; but I will not send complete destruction on Jacob, says the Lord.
9 “Pakuti ndidzalamula, ndipo ndidzagwedeza nyumba ya Israeli pakati pa mitundu yonse ya anthu monga momwe amasefera ufa mʼsefa, koma palibe nʼkamwala kamodzi komwe kamene kadzagwe pansi.
For see, I will give orders, and I will have Israel moved about among all the nations, as grain is moved about by the shaking of the tray, but not the smallest seed will be dropped on the earth.
10 Anthu onse ochimwa pakati pa anthu anga adzaphedwa ndi lupanga, onse amene amanena kuti, ‘Tsoka silidzatigwera ife kapena kutiwononga.’
All those sinners among my people will be put to the sword who say, Evil will not overtake us or come face to face with us.
11 “Tsiku limenelo ndidzabwezeretsa nyumba ya Davide imene inagwa. Ndidzakonzanso malo amene anagumuka, ndi kuyimanganso monga inalili poyamba,
In that day I will put up the tent of David which has come down, and make good its broken places; and I will put up again his damaged walls, building it up as in the past;
12 kuti adzatengenso otsala a Edomu ndi mitundu yonse imene imatchedwa ndi dzina langa,” akutero Yehova amene adzachita zinthu izi.
So that the rest of Edom may be their heritage, and all the nations who have been named by my name, says the Lord, who is doing this.
13 Yehova akunena kuti “Nthawi ikubwera pamene mlimi wotipula adzapyola wokolola ndipo woponda mphesa adzapyola wodzala mbewu. Mapiri adzachucha vinyo watsopano ndi kuyenderera pa zitunda zonse.
See, the days will come, says the Lord, when the ploughman will overtake him who is cutting the grain, and the crusher of the grapes him who is planting seed; and sweet wine will be dropping from the mountains, and the hills will be turned into streams of wine.
14 Ndidzawabwezeranso pabwino anthu anga Aisraeli; mizinda imene inali mabwinja idzamangidwanso ndipo azidzakhalamo. Adzalima minda ya mpesa ndipo adzamwa vinyo wake; adzalima minda ndipo adzadya zipatso zake.
And I will let the fate of my people Israel be changed, and they will be building up again the waste towns and living in them; they will again be planting vine-gardens and taking the wine for their drink; and they will make gardens and get the fruit of them.
15 Ndidzakhazika Aisraeli mʼdziko mwawo, ndipo sadzachotsedwamonso mʼdziko limene Ine ndawapatsa,” akutero Yehova Mulungu wako.
And I will have them planted in their land, and never again will they be uprooted from their land which I have given them, says the Lord your God.