< Amosi 9 >

1 Ine ndinaona Ambuye atayima pambali pa guwa lansembe, ndipo anati: “Kantha mitu ya nsanamira kuti ziwundo za nyumba zigwedezeke. Muzigwetsere pa mitu ya anthu onse, onse amene atsalira ndidzawapha ndi lupanga. Palibe ndi mmodzi yemwe amene adzathawe, palibe amene adzapulumuke.
Видях Господа, че стоеше при олтара и рече: Удари капителите, за да се потресат праговете, И разтроши ги върху главата на всички тях; А останалите от тях ще погубя с меч; Който от тях бяга, няма да избегне, И който от тях се отърве, няма да се избави.
2 Ngakhale atakumba pansi mpaka ku malo a anthu akufa, dzanja langa lidzawatulutsa kumeneko. Ngakhale atakwera kumwamba Ine ndidzawatsakamutsa kumeneko. (Sheol h7585)
Ако изкопаят до Шеол, И от там ръката ми ще ги изтръгне; И ако се изкачат на небето, От там ще ги сваля; (Sheol h7585)
3 Ngakhale atakabisala pamwamba pa phiri la Karimeli, Ine ndidzawasaka kumeneko ndi kuwagwira. Ngakhale atakabisala pansi pa nyanja yayikulu, ndidzalamula njoka kuti iwalume kumeneko.
Ако се скрият на връх Кармил, Ще ги издиря и ще ги взема от там; И ако се скрият от очите Ми в морските дълбочини, Там ще заповядам на змията, и ще ги ухапе;
4 Ngakhale adani awo awakusire ku ukapolo, ndidzalamula lupanga kuti liwaphe kumeneko. Ndidzawayangʼanitsitsa kuti zoyipa ziwagwere; osati zabwino.”
Ако отидат в плен пред неприятелите си, Там ще заповядам на ножа, та ще ги убие; И ще насоча очите Си върху тях за зло, а не за добро.
5 Ambuye Yehova Wamphamvuzonse amene amakhudza dziko lapansi ndipo dzikolo limasungunuka, onse amene amakhala mʼmenemo amalira. Dziko lonse lidzadzaza ngati mtsinje wa Nailo, kenaka nʼkuphwera ngati mtsinje wa ku Igupto.
Защото Господ Иеова на Силите е оня, Който се допира до земята, и тя се топи, Така щото всички, които живеят на нея ще жалеят; Защото тя цяла ще се издига като Нил, И ще спада пак като Египетската река:
6 Iye amene amamanga malo ake okhalamo kumwamba, ndi kuyika maziko ake pa dziko lapansi, Iye amene amayitana madzi a ku nyanja ndikuwakhuthulira pa dziko lapansi, dzina lake ndiye Yehova.
Той е, който гради сферите си на небето, И основава свода си на земята; Който повиква морските води, И излива ги по лицето на земята; Иеова е името му.
7 “Kodi kwa Ine, inu Aisraeli, simuli chimodzimodzi ndi Akusi?” Akutero Yehova. “Kodi sindine amene ndinatulutsa Israeli ku Igupto, Afilisti ku Kafitori ndi Aaramu ku Kiri?
Вие Израиляни, казва Господ, Не сте ли на Мене като Етиопяни? Не възведох ли както Израиля от Египетската земя, Така и Филистимците от Кафтор И Сирийците от Кир?
8 “Taonani, maso a Ambuye Yehova ali pa ufumu wochimwawu. Ndidzawufafaniza pa dziko lapansi. Komabe sindidzawononga kotheratu nyumba ya Yakobo,” akutero Yehova.
Ето, очите на Господа Иеова са върху грешното царство, И ще го погубя от лицето на света; Само че няма да погубя съвсем Якововия дом, казва Господ.
9 “Pakuti ndidzalamula, ndipo ndidzagwedeza nyumba ya Israeli pakati pa mitundu yonse ya anthu monga momwe amasefera ufa mʼsefa, koma palibe nʼkamwala kamodzi komwe kamene kadzagwe pansi.
Защото, ето, аз ще заповядам, И ще пресея Израилевия дом между всичките народи Както се пресява житото в решетото; Обаче ни най-малко зърно няма да падне на земята.
10 Anthu onse ochimwa pakati pa anthu anga adzaphedwa ndi lupanga, onse amene amanena kuti, ‘Tsoka silidzatigwera ife kapena kutiwononga.’
От мене ще измрат всичките грешници между людете ми, Които казват - Това зло няма да стигне до нас, Нито ще ни предвари.
11 “Tsiku limenelo ndidzabwezeretsa nyumba ya Davide imene inagwa. Ndidzakonzanso malo amene anagumuka, ndi kuyimanganso monga inalili poyamba,
В оня ден ще въздигна падналата Давидова скиния, И ще заградя проломите й; Ще въздигна развалините й, И ще я съградя пак както в древните дни,
12 kuti adzatengenso otsala a Edomu ndi mitundu yonse imene imatchedwa ndi dzina langa,” akutero Yehova amene adzachita zinthu izi.
За да завладеят останалите от Едом И всичките народи, които се наричаха с името ми, Казва Господ, който прави това.
13 Yehova akunena kuti “Nthawi ikubwera pamene mlimi wotipula adzapyola wokolola ndipo woponda mphesa adzapyola wodzala mbewu. Mapiri adzachucha vinyo watsopano ndi kuyenderera pa zitunda zonse.
Ето, идат дни, казва Господ, Когато орачът ще стигне жетваря, И линотъпкачът сеятеля, От планините ще капе мъст, И всичките хълми ще се стопят.
14 Ndidzawabwezeranso pabwino anthu anga Aisraeli; mizinda imene inali mabwinja idzamangidwanso ndipo azidzakhalamo. Adzalima minda ya mpesa ndipo adzamwa vinyo wake; adzalima minda ndipo adzadya zipatso zake.
И аз ще върна от плен людете си Израиля; Те ще съградят запустелите градове и ще ги населят, Ще насадят лозя и ще пият виното им, И ще направят градини и ще ядат плодът им,
15 Ndidzakhazika Aisraeli mʼdziko mwawo, ndipo sadzachotsedwamonso mʼdziko limene Ine ndawapatsa,” akutero Yehova Mulungu wako.
И те няма вече да се изтръъгат от земята, Която им дадох, казва Господ твоя Бог.

< Amosi 9 >