< Amosi 8 >
1 Zimene Ambuye Yehova anandionetsa ndi izi: dengu la zipatso zakupsa.
Thus the lord Jehovah showed me: And, behold, a basket of summer fruit.
2 Iye anandifunsa kuti, “Amosi nʼchiyani ukuona?” Ine ndinayankha kuti, “Dengu la zipatso zakupsa.” Ndipo Yehova anati kwa ine, “Nthawi yachimaliziro yawakwanira anthu anga Aisraeli; sindidzawakhululukiranso.
And he said, Amos, what do thou see? And I said, A basket of summer fruit. Then Jehovah said to me, The end has come upon my people Israel. I will not again pass by them any more.
3 “Tsiku limenelo,” Ambuye Yehova akulengeza kuti, “Nyimbo za mʼNyumba ya Mulungu zidzasanduka kulira kofuwula. Mitembo ya anthu idzachuluka, ndipo adzayiponya ponseponse! Kudzangoti zii!”
And the songs of the temple shall be wailings in that day, says the lord Jehovah. The dead bodies shall be many. In every place they shall cast them forth with silence.
4 Imvani izi, inu amene mumapondereza anthu osowa ndipo simulabadira anthu osauka a mʼdzikomu.
Hear this, O ye who would swallow up a needy man, and cause the poor of the land to fail,
5 Mumanena kuti, “Kodi chikondwerero cha mwezi watsopano chidzatha liti kuti tigulitse zinthu? Ndipo tsiku la Sabata litha liti kuti tigulitse tirigu, kuti tichepetse miyeso, kukweza mitengo kuti tibere anthu ndi miyeso ya chinyengo,
saying, When will the new moon be gone, that we may sell grain? And the sabbath, that we may set forth wheat, making the ephah small, and the shekel great, and dealing falsely with balances of deceit,
6 tigule osauka ndi ndalama zasiliva ndi osowa powapatsa nsapato, tigulitse ngakhale mungu wa tirigu?”
that we may buy the poor for silver, and a needy man for a pair of shoes, and sell the refuse of the wheat?
7 Yehova amene Yakobo amamunyadira, walumbira kuti: Ine sindidzayiwala chilichonse chimene anachita.
Jehovah has sworn by the excellency of Jacob, Surely I will never forget any of their works.
8 “Kodi dziko silidzagwedezeka chifukwa cha zimenezi, ndi onse okhala mʼmenemo kulira mwachisoni? Dziko lonse lidzavunduka ngati mtsinje wa Nailo; lidzagwedezeka kenaka nʼkukhala bata ngati mtsinje wa ku Igupto.
Shall the land not tremble for this, and everyone mourn who dwells therein? Yea, it shall rise up wholly like the River, and it shall be troubled and sink again like the River of Egypt.
9 “Tsiku limenelo,” Ambuye Yehova akunena kuti, “Ndidzadetsa dzuwa masana ndi kugwetsa mdima pa dziko lapansi dzuwa likuswa mtengo.
And it shall come to pass in that day, says the lord Jehovah, that I will cause the sun to go down at noon, and I will darken the earth in the clear day.
10 Maphwando anu achipembedzo ndidzawasandutsa kulira kwa chisoni ndipo kuyimba kwanu konse ndidzakusandutsa maliro. Ndidzakuvekani chiguduli nonsenu ndi kumeta mipala mitu yanu. Nthawi imeneyo idzakhala ngati yolira mwana wamwamuna mmodzi yekhayo, ndipo tsikulo lidzakhala lowawa mpaka kutha kwake.
And I will turn your feasts into mourning, and all your songs into lamentation. And I will bring sackcloth upon all loins, and baldness upon every head, and I will make it as the mourning for an only son, and the end thereof as a bitter day.
11 “Nthawi ikubwera,” Ambuye Yehova akunena kuti, “Ndidzagwetsa njala mʼdziko lonse; osati njala ya chakudya kapena ludzu la madzi, koma njala yofuna kumva mawu a Yehova.
Behold, the days come, says the lord Jehovah, that I will send a famine in the land, not a famine of bread, nor a thirst for water, but of hearing the words of Jehovah.
12 Anthu azidzangoyendayenda kuchoka ku nyanja ina kupita ku nyanja ina. Azidzangoyendayenda kuchoka kumpoto kupita kummawa, kufunafuna mawu a Yehova, koma sadzawapeza.
And they shall wander from sea to sea, and from the north even to the east. They shall run to and fro to seek the word of Jehovah, and shall not find it.
13 “Tsiku limenelo “anamwali okongola ndi anyamata amphamvu adzakomoka ndi ludzu.
In that day the fair virgins and the young men shall faint for thirst.
14 Onse amene amalumbira pa tchimo la Samariya, kapena kumanena kuti, ‘Iwe Dani, pali mulungu wako wamoyo,’ kapena, ‘Pali mulungu wamoyo wa ku Beeriseba.’ Iwowo adzagwa ndipo sadzadzukanso.”
Those who swear by the sin of Samaria, and say, As thy god, O Dan, lives, and, As the way of Beersheba lives, they shall fall, and never rise up again.