< Amosi 8 >

1 Zimene Ambuye Yehova anandionetsa ndi izi: dengu la zipatso zakupsa.
Saaledes lod HERREN mig skue: Se, der var en Kurv Sommerfrugt.
2 Iye anandifunsa kuti, “Amosi nʼchiyani ukuona?” Ine ndinayankha kuti, “Dengu la zipatso zakupsa.” Ndipo Yehova anati kwa ine, “Nthawi yachimaliziro yawakwanira anthu anga Aisraeli; sindidzawakhululukiranso.
Og han sagde: »Hvad ser du, Amos?« Jeg svarede: »En Kurv Sommerfrugt!« Da sagde HERREN til mig: »Enden er kommet for mit Folk Israel; jeg vil ikke længer bære over med det.«
3 “Tsiku limenelo,” Ambuye Yehova akulengeza kuti, “Nyimbo za mʼNyumba ya Mulungu zidzasanduka kulira kofuwula. Mitembo ya anthu idzachuluka, ndipo adzayiponya ponseponse! Kudzangoti zii!”
Paladsets Sangerinder skal jamre paa denne Dag, saa lyder det fra den Herre HERREN, Dynger af Lig er henkastet alle Vegne.
4 Imvani izi, inu amene mumapondereza anthu osowa ndipo simulabadira anthu osauka a mʼdzikomu.
Hør, I, som knuser de fattige, gør det af med de arme i Landet
5 Mumanena kuti, “Kodi chikondwerero cha mwezi watsopano chidzatha liti kuti tigulitse zinthu? Ndipo tsiku la Sabata litha liti kuti tigulitse tirigu, kuti tichepetse miyeso, kukweza mitengo kuti tibere anthu ndi miyeso ya chinyengo,
og siger: »Hvornaar er Nymaanen omme, saa vi kan faa solgt noget Korn, Sabbaten, saa vi kan aabne vort Kornsalg, gøre Efaen lille og Sekelen stor og med Svig gøre Vægten falsk
6 tigule osauka ndi ndalama zasiliva ndi osowa powapatsa nsapato, tigulitse ngakhale mungu wa tirigu?”
for at købe den ringe for Sølv, den fattige for et Par Sko og faa Affaldskornet solgt?«
7 Yehova amene Yakobo amamunyadira, walumbira kuti: Ine sindidzayiwala chilichonse chimene anachita.
HERREN svor ved Jakobs Stolthed: Aldrig glemmer jeg een af deres Gerninger!
8 “Kodi dziko silidzagwedezeka chifukwa cha zimenezi, ndi onse okhala mʼmenemo kulira mwachisoni? Dziko lonse lidzavunduka ngati mtsinje wa Nailo; lidzagwedezeka kenaka nʼkukhala bata ngati mtsinje wa ku Igupto.
Maa Jorden ej skælve derover og enhver, som bor paa den, sørge? Den stiger overalt som Nilen og synker som Ægyptens Flod.
9 “Tsiku limenelo,” Ambuye Yehova akunena kuti, “Ndidzadetsa dzuwa masana ndi kugwetsa mdima pa dziko lapansi dzuwa likuswa mtengo.
Paa hin Dag lader jeg det ske, saa lyder det fra den Herre HERREN, at Solen gaar ned ved Middag, og Jorden bliver mørk ved højlys Dag.
10 Maphwando anu achipembedzo ndidzawasandutsa kulira kwa chisoni ndipo kuyimba kwanu konse ndidzakusandutsa maliro. Ndidzakuvekani chiguduli nonsenu ndi kumeta mipala mitu yanu. Nthawi imeneyo idzakhala ngati yolira mwana wamwamuna mmodzi yekhayo, ndipo tsikulo lidzakhala lowawa mpaka kutha kwake.
Jeg vender eders Fester til Sorg og alle eders Sange til klage, lægger Sæk om alle Lænder, gør hvert et Hoved skaldet, bringer Sorg som over en enbaaren, en bitter Dag til sidst.
11 “Nthawi ikubwera,” Ambuye Yehova akunena kuti, “Ndidzagwetsa njala mʼdziko lonse; osati njala ya chakudya kapena ludzu la madzi, koma njala yofuna kumva mawu a Yehova.
Se, Dage skal komme, lyder det fra den Herre HERREN, da jeg sender Hunger i Landet, ikke Hunger efter Brød, ikke Tørst efter Vand, men efter at høre HERRENS Ord.
12 Anthu azidzangoyendayenda kuchoka ku nyanja ina kupita ku nyanja ina. Azidzangoyendayenda kuchoka kumpoto kupita kummawa, kufunafuna mawu a Yehova, koma sadzawapeza.
Da vanker de fra Hav til Hav, flakker fra Nord til Øst for at søge HERRENS Ord, men finder det ej.
13 “Tsiku limenelo “anamwali okongola ndi anyamata amphamvu adzakomoka ndi ludzu.
Den Dag vansmægter af Tørst de fagre Jomfruer og unge Mænd,
14 Onse amene amalumbira pa tchimo la Samariya, kapena kumanena kuti, ‘Iwe Dani, pali mulungu wako wamoyo,’ kapena, ‘Pali mulungu wamoyo wa ku Beeriseba.’ Iwowo adzagwa ndipo sadzadzukanso.”
som sværger ved Samarias Synd, som siger: »Ved din Gud, o Dan!« »Ved din Skytsgud, o Be'ersjeba!« de skal falde, ej mere staa op.

< Amosi 8 >