< Amosi 8 >

1 Zimene Ambuye Yehova anandionetsa ndi izi: dengu la zipatso zakupsa.
Také mi ukázal Panovník Hospodin, a aj, byl koš ovoce letního.
2 Iye anandifunsa kuti, “Amosi nʼchiyani ukuona?” Ine ndinayankha kuti, “Dengu la zipatso zakupsa.” Ndipo Yehova anati kwa ine, “Nthawi yachimaliziro yawakwanira anthu anga Aisraeli; sindidzawakhululukiranso.
A řekl: Co ty vidíš, Amose? I řekl jsem: Koš ovoce letního. Opět mi řekl Hospodin: Přišeltě konec lidu mému Izraelskému, nebuduť již více promíjeti jemu.
3 “Tsiku limenelo,” Ambuye Yehova akulengeza kuti, “Nyimbo za mʼNyumba ya Mulungu zidzasanduka kulira kofuwula. Mitembo ya anthu idzachuluka, ndipo adzayiponya ponseponse! Kudzangoti zii!”
Pročež kvíliti budou zpěvové chrámoví v ten den, praví Panovník Hospodin. Množství mrtvých, mlče, namece na všelijaké místo.
4 Imvani izi, inu amene mumapondereza anthu osowa ndipo simulabadira anthu osauka a mʼdzikomu.
Slyštež to vy, kteříž sehlcujete chudého, abyste vyhladili nuzné z země,
5 Mumanena kuti, “Kodi chikondwerero cha mwezi watsopano chidzatha liti kuti tigulitse zinthu? Ndipo tsiku la Sabata litha liti kuti tigulitse tirigu, kuti tichepetse miyeso, kukweza mitengo kuti tibere anthu ndi miyeso ya chinyengo,
Říkajíce: Skoro-liž pomine novměsíce, abychom prodávali obilé, a sobota, abychom otevřeli obilnice, abychom ujímali efi, a přivětšovali váhy, a faleš provodili vážkami falešnými,
6 tigule osauka ndi ndalama zasiliva ndi osowa powapatsa nsapato, tigulitse ngakhale mungu wa tirigu?”
Kupujíce za peníze nuzné, a chudého za pár střevíců, nadto abychom plevy obilné prodávali?
7 Yehova amene Yakobo amamunyadira, walumbira kuti: Ine sindidzayiwala chilichonse chimene anachita.
Přisáhl Hospodin skrze důstojnost Jákobovu: Žeť se nezapomenu na věky na všecky skutky jejich.
8 “Kodi dziko silidzagwedezeka chifukwa cha zimenezi, ndi onse okhala mʼmenemo kulira mwachisoni? Dziko lonse lidzavunduka ngati mtsinje wa Nailo; lidzagwedezeka kenaka nʼkukhala bata ngati mtsinje wa ku Igupto.
Nad tím-liž by se netřásla i země, a nekvílil by každý, kdož přebývá na ní? Proto-liž by neměla vystoupiti všecka jako potok, a zachvácena i zatopena býti jako potokem Egyptským?
9 “Tsiku limenelo,” Ambuye Yehova akunena kuti, “Ndidzadetsa dzuwa masana ndi kugwetsa mdima pa dziko lapansi dzuwa likuswa mtengo.
Anobrž stane se v ten den, praví Panovník Hospodin, učiním, že slunce zajde o poledni, a uvedu tmy na zemi v jasný den.
10 Maphwando anu achipembedzo ndidzawasandutsa kulira kwa chisoni ndipo kuyimba kwanu konse ndidzakusandutsa maliro. Ndidzakuvekani chiguduli nonsenu ndi kumeta mipala mitu yanu. Nthawi imeneyo idzakhala ngati yolira mwana wamwamuna mmodzi yekhayo, ndipo tsikulo lidzakhala lowawa mpaka kutha kwake.
A proměním svátky vaše v kvílení, a všecky zpěvy vaše v naříkání, a způsobím to, že bude na každých bedrách žíně, a na každé hlavě lysina, a bude v zemi této kvílení jako nad jednorozeným, a poslední věci její jako den hořkosti.
11 “Nthawi ikubwera,” Ambuye Yehova akunena kuti, “Ndidzagwetsa njala mʼdziko lonse; osati njala ya chakudya kapena ludzu la madzi, koma njala yofuna kumva mawu a Yehova.
Aj, dnové jdou, dí Panovník Hospodin, že pošli hlad na zemi, ne hlad chleba, ani žízeň vody, ale slyšení slov Hospodinových,
12 Anthu azidzangoyendayenda kuchoka ku nyanja ina kupita ku nyanja ina. Azidzangoyendayenda kuchoka kumpoto kupita kummawa, kufunafuna mawu a Yehova, koma sadzawapeza.
Tak že toulati se budou od moře až k moři, a od půlnoci až na východ běhati, hledajíce slova Hospodinova, však nenajdou.
13 “Tsiku limenelo “anamwali okongola ndi anyamata amphamvu adzakomoka ndi ludzu.
V ten čas umdlévati budou panny krásné, ano i mládenci tou žízní,
14 Onse amene amalumbira pa tchimo la Samariya, kapena kumanena kuti, ‘Iwe Dani, pali mulungu wako wamoyo,’ kapena, ‘Pali mulungu wamoyo wa ku Beeriseba.’ Iwowo adzagwa ndipo sadzadzukanso.”
Kteříž přisahají skrze ohavnost Samařskou, a říkají: Živť jest Bůh tvůj, ó Dan, a živa jest cesta Bersabé. I padnou, a nepovstanou více.

< Amosi 8 >