< Amosi 7 >

1 Zimene Ambuye Yehova anandionetsa ndi izi: Yehova ankasonkhanitsa gulu la dzombe nthawi imene gawo la zokolola za mfumu linali litakololedwa kale ndipo mbewu zachiwiri zinali zitangoyamba kumera kumene.
Egemen RAB bana şunu gösterdi: Kralın payına düşen otlar biçilmişti. Otlar yeniden yeşermeye başlarken RAB sürüyle çekirge yaratıyordu.
2 Dzombelo litadya zomera zonse za mʼdzikomo, Ine ndinafuwula kuti, “Ambuye Yehova, khululukani! Kodi Yakobo adzapulumuka bwanji? Iye ndi wofowoka kwambiri!”
Çekirgeler ülkedeki yeşil bitkileri yiyip bitirince: “Ey Egemen RAB, lütfen halkını bağışla!” dedim, “Yakup soyu buna nasıl dayanır? Zaten küçük bir halk!”
3 Kotero Yehova anakhululuka. Yehovayo anati, “Izi sizidzachitika.”
Bunun üzerine RAB düşüncesini değiştirdi. “Gerçekleşmeyecek bu” dedi.
4 Zimene Ambuye Yehova anandionetsa ndi izi: Ambuye Yehova ankayitana malawi a moto kuti alange anthu. Motowo unawumitsa nyanja yakuya ndi kupsereza dziko.
Egemen RAB bana şunu gösterdi: Baktım, Egemen RAB halkını cezalandırmak için ateşi çağırdı. Ateş enginleri yakıp tüketti, karayı yakıp tüketmeye başladı.
5 Tsono ine ndinafuwula kuti, “Ambuye Yehova, chonde ndikukupemphani, lekani! Kodi Yakobo adzapulumuka bwanji? Iye ndi wofowoka kwambiri!”
O zaman, “Ey Egemen RAB, lütfen dur!” dedim, “Yakup soyu buna nasıl dayanır? Zaten küçük bir halk!”
6 Kotero Yehova anakhululuka. Ambuye Yehova anati, “Izinso sizidzachitika.”
Bunun üzerine RAB düşüncesini değiştirdi. Egemen RAB, “Bu da gerçekleşmeyecek” dedi.
7 Zimene Iye anandionetsa ndi izi: Ambuye anayima pambali pa khoma lomangamanga, mʼmanja mwake muli chingwe chowongolera khoma.
Başka bir görümde şunu gösterdi bana: Baktım, Rab çekül kullanılarak örülmüş dümdüz bir duvarın yanında duruyor; elinde bir çekül var.
8 Ndipo Ambuye anandifunsa kuti, “Amosi, nʼchiyani ukuonachi?” Ine ndinayankha kuti, “Chingwe chowongolera khoma.” Ndipo Yehova anati, “Taona, Ine ndikuyika chingwe chowongolerachi pakati pa anthu anga, Aisraeli; sindidzawalekereranso.
RAB, “Ne görüyorsun, Amos?” diye sordu. Ben de, “Bir çekül” dedim. Bunun üzerine Rab, “İşte, halkım İsrail'in ortasına da bir çekül koyacağım” dedi, “Bir daha onları esirgemeyeceğim.
9 “Malo achipembedzo a Isake adzawonongedwa ndipo malo opatulika a Israeli adzasanduka bwinja; ndidzagwetsa nyumba ya Yeroboamu ndi lupanga langa.”
“Yok olacak İshak soyunun tapınma yerleri, Yıkılacak İsrail'in kutsal yerleri, Kılıçla yürüyeceğim Yarovam soyunun üstüne.”
10 Pamenepo Amaziya wansembe wa ku Beteli anatumiza uthenga kwa Yeroboamu mfumu ya Israeli kuti, “Amosi akukuutsirani chiwembu pakati pa Aisraeli. Dziko silingalekerere zonena zake zonsezo.
Beytel'deki Kâhin Amatsya, İsrail Kralı Yarovam'a haber gönderip şöyle dedi: “Amos İsrail'in göbeğinde sana düzen kurdu. Ülke onun bunca sözünü kaldıramaz.
11 Pakuti zimene Amosi akunena ndi izi: “‘Yeroboamu adzaphedwa ndi lupanga, ndipo Israeli adzapita ndithu ku ukapolo, kutali ndi dziko lake.’”
Çünkü Amos diyor ki, “‘Yarovam kılıçla öldürülecek, İsrail halkı kesinlikle ülkesinin dışına, Sürgüne gönderilecek.’”
12 Ndipo Amaziya anawuza Amosi kuti, “Choka, mlosi iwe! Bwerera ku dziko la Yuda. Uzikalosera kumeneko ndipo anthu a kumeneko azikakudyetsa.
Bunun üzerine Amatsya Amos'a, “Çek git, ey bilici!” dedi, “Yahuda'ya kaç. Ekmeğini orada kazan. Orada peygamberlik et.
13 Usanenerenso ku Beteli, chifukwa kumeneko ndi malo opatulika a mfumu ndiponso ndi malo a nyumba yachipembedzo yaufumu.”
Bir daha Beytel'de peygamberlik etme. Çünkü burası kralın kutsal yeri, krallık tapınağıdır.”
14 Amosi anayankha Amaziya kuti, “Ine sindine mneneri kapena mwana wa mneneri; koma ndine woweta ziweto, ndiponso mlimi wa nkhuyu.
Amos, “Ben ne peygamberdim ne de peygamber oğluydum” diye karşılık verdi, “Yalnızca sığır yetiştirirdim. Yabanıl incir ağaçlarına bakardım.
15 Koma Yehova ananditenga ndikuweta nkhosa ndipo anati, ‘Pita ukanenere kwa anthu anga Aisraeli.’
RAB beni sürünün ardından aldı, ‘Git, halkım İsrail'e peygamberlik et’ dedi.
16 Tsono imva mawu a Yehova. Iwe ukunena kuti, “‘Usanenere zotsutsa Israeli, ndipo siya kulalikira motsutsa nyumba ya Isake.’”
Şimdi kulak ver RAB'bin sözlerine: “‘İsrail'e karşı peygamberlik etme, İshak soyuna karşı konuşma!’ diyorsun.
17 “Tsono zimene akunena Yehova ndi izi: “‘Mkazi wako adzasanduka wachiwerewere mu mzindamu, ndipo ana ako aamuna ndi aakazi adzaphedwa ndi lupanga. Munda wako udzayezedwa ndi chingwe ndi kugawidwa, ndipo iwe mwini udzafera mʼdziko la anthu osapembedza Mulungu. Ndipo Israeli adzatengedwa ndithu kupita ku ukapolo, kutali ndi dziko lake.’”
Bu yüzden RAB şöyle diyor: ‘Karın kentte fahişe olacak, Oğulların, kızların kılıçtan geçirilecek. Ölçü ipiyle paylaşılacak toprağın, Sen ise kirli sayılan toprakta can vereceksin. İsrail halkı kesinlikle ülke dışına, Sürgüne gönderilecek.’”

< Amosi 7 >