< Amosi 7 >

1 Zimene Ambuye Yehova anandionetsa ndi izi: Yehova ankasonkhanitsa gulu la dzombe nthawi imene gawo la zokolola za mfumu linali litakololedwa kale ndipo mbewu zachiwiri zinali zitangoyamba kumera kumene.
To mi ukazał panujący Pan. Oto tworzył szarańczę, gdy najpierwej począł odrastać potraw, gdy oto potraw był po pokoszeniu królewskiem.
2 Dzombelo litadya zomera zonse za mʼdzikomo, Ine ndinafuwula kuti, “Ambuye Yehova, khululukani! Kodi Yakobo adzapulumuka bwanji? Iye ndi wofowoka kwambiri!”
A gdy zjadły trawę ziemi, rzekłem: Panujący Panie! sfolguj proszę; bo któż zostanie Jakóbowi, gdyż maluczki jest?
3 Kotero Yehova anakhululuka. Yehovayo anati, “Izi sizidzachitika.”
I żałował Pan tego; a rzekł Pan: Nie stanie się.
4 Zimene Ambuye Yehova anandionetsa ndi izi: Ambuye Yehova ankayitana malawi a moto kuti alange anthu. Motowo unawumitsa nyanja yakuya ndi kupsereza dziko.
Tedy mi ukazał panujący Pan, a oto panujący Pan wołał, że sprawę swoję powiedzie ogniem, a spaliwszy przepaść wielką, spalił i część królestwa Izraelskiego.
5 Tsono ine ndinafuwula kuti, “Ambuye Yehova, chonde ndikukupemphani, lekani! Kodi Yakobo adzapulumuka bwanji? Iye ndi wofowoka kwambiri!”
Tedym rzekł: Panujący Panie! przestań proszę; bo któż zostanie Jakóbowi, gdyż maluczki jest?
6 Kotero Yehova anakhululuka. Ambuye Yehova anati, “Izinso sizidzachitika.”
I żałował Pan tego, a rzekł panujący Pan: I toć się nie stanie.
7 Zimene Iye anandionetsa ndi izi: Ambuye anayima pambali pa khoma lomangamanga, mʼmanja mwake muli chingwe chowongolera khoma.
Potem ukazał mi, a oto Pan stał na murze według sznuru zbudowanym, w którego ręku było prawidło.
8 Ndipo Ambuye anandifunsa kuti, “Amosi, nʼchiyani ukuonachi?” Ine ndinayankha kuti, “Chingwe chowongolera khoma.” Ndipo Yehova anati, “Taona, Ine ndikuyika chingwe chowongolerachi pakati pa anthu anga, Aisraeli; sindidzawalekereranso.
I rzekł Pan do mnie: Cóż widzisz Amosie? I rzekłem: Prawidło. Tedy rzekł Pan: Oto Ja położę prawidło w pośrodku ludu mego Izraelskiego, a już mu więcej nie będę przeglądał.
9 “Malo achipembedzo a Isake adzawonongedwa ndipo malo opatulika a Israeli adzasanduka bwinja; ndidzagwetsa nyumba ya Yeroboamu ndi lupanga langa.”
Bo wyżyny Izaakowe spustoszone będą, a świątnice Izraelskie zburzone będą, gdy powstanę przeciwko domowi Jeroboamowemu z mieczem.
10 Pamenepo Amaziya wansembe wa ku Beteli anatumiza uthenga kwa Yeroboamu mfumu ya Israeli kuti, “Amosi akukuutsirani chiwembu pakati pa Aisraeli. Dziko silingalekerere zonena zake zonsezo.
Tedy posłał Amazyjasz, kapłan Betelski, do Jeroboama, króla Izraelskiego, mówiąc: Sprzysiągł się przeciwko tobie w pośrodku domu Izraelskiego, tak, iż ziemia nie może znieść wszystkich słów jego.
11 Pakuti zimene Amosi akunena ndi izi: “‘Yeroboamu adzaphedwa ndi lupanga, ndipo Israeli adzapita ndithu ku ukapolo, kutali ndi dziko lake.’”
Bo tak mówi Amos: Jeroboam od miecza umrze, a Izrael zapewne do więzienia z ziemi swojej zaprowadzony będzie.
12 Ndipo Amaziya anawuza Amosi kuti, “Choka, mlosi iwe! Bwerera ku dziko la Yuda. Uzikalosera kumeneko ndipo anthu a kumeneko azikakudyetsa.
Potem rzekł Amazyjasz do Amosa: O widzący! uchodź, uciekaj do ziemi Judzkiej, a jedz tam chleb, i tam prorokuj;
13 Usanenerenso ku Beteli, chifukwa kumeneko ndi malo opatulika a mfumu ndiponso ndi malo a nyumba yachipembedzo yaufumu.”
Ale w Betelu więcej nie prorokuj; bo to jest świątnica królewska, i dom królewski.
14 Amosi anayankha Amaziya kuti, “Ine sindine mneneri kapena mwana wa mneneri; koma ndine woweta ziweto, ndiponso mlimi wa nkhuyu.
Tedy odpowiedział i rzekł do Amazyjasza: Nie byłem ja prorokiem, nawet ani synem prorockim; alem był skotarzem, a zbierałem figi leśne.
15 Koma Yehova ananditenga ndikuweta nkhosa ndipo anati, ‘Pita ukanenere kwa anthu anga Aisraeli.’
Ale mię Pan wziął, gdym chodził za bydłem, i rzekł do mnie Pan: Idź, prorokuj ludowi memu Izraelskiemu.
16 Tsono imva mawu a Yehova. Iwe ukunena kuti, “‘Usanenere zotsutsa Israeli, ndipo siya kulalikira motsutsa nyumba ya Isake.’”
Teraz tedy słuchaj słowa Pańskiego. Ty mówisz: Nie prorokuj w Izraelu, i nie każ w domu Izaakowym;
17 “Tsono zimene akunena Yehova ndi izi: “‘Mkazi wako adzasanduka wachiwerewere mu mzindamu, ndipo ana ako aamuna ndi aakazi adzaphedwa ndi lupanga. Munda wako udzayezedwa ndi chingwe ndi kugawidwa, ndipo iwe mwini udzafera mʼdziko la anthu osapembedza Mulungu. Ndipo Israeli adzatengedwa ndithu kupita ku ukapolo, kutali ndi dziko lake.’”
Przetoż tak mówi Pan: Żona twoja w mieście nierząd płodzić będzie, a synowie twoi i córki twoje od miecza polegną, a ziemia twoja sznurem będzie podzielona, a ty w ziemi splugawionej umrzesz; lecz Izrael zapewne zaprowadzony będzie do więzienia z ziemi swojej.

< Amosi 7 >