< Amosi 7 >

1 Zimene Ambuye Yehova anandionetsa ndi izi: Yehova ankasonkhanitsa gulu la dzombe nthawi imene gawo la zokolola za mfumu linali litakololedwa kale ndipo mbewu zachiwiri zinali zitangoyamba kumera kumene.
Niin Herra, Herra osoitti minulle näyssä; ja katso, yksi seisoi, joka heinäsirkkoja teki, juuri silloin, kuin oras rupesi käymään ylös, toisen kerran sittekuin kuningas oli antanut niittää.
2 Dzombelo litadya zomera zonse za mʼdzikomo, Ine ndinafuwula kuti, “Ambuye Yehova, khululukani! Kodi Yakobo adzapulumuka bwanji? Iye ndi wofowoka kwambiri!”
Kuin ne niin tahtoivat kaiken tulon syödä maalta, sanoin minä: voi Herra, Herra, ole armollinen! kuka tahtoo Jakobin taas auttaa? sillä hän on aivan vähä.
3 Kotero Yehova anakhululuka. Yehovayo anati, “Izi sizidzachitika.”
Niin Herra katui sitä: ei sen pidä tapahtuman, sanoi Herra.
4 Zimene Ambuye Yehova anandionetsa ndi izi: Ambuye Yehova ankayitana malawi a moto kuti alange anthu. Motowo unawumitsa nyanja yakuya ndi kupsereza dziko.
Niin Herra, Herra osoitti minulla näyssä, ja katso, Herra, Herra kutsui tulen rankaisemaan, jonka piti suuren syvyyden syömän, ja se söi jo parhaan osan.
5 Tsono ine ndinafuwula kuti, “Ambuye Yehova, chonde ndikukupemphani, lekani! Kodi Yakobo adzapulumuka bwanji? Iye ndi wofowoka kwambiri!”
Niin minä sanoin: voi Herra, Herra, lakkaa nyt, kuka tahtoo Jakobia taas auttaa? sillä hän on aivan vähä.
6 Kotero Yehova anakhululuka. Ambuye Yehova anati, “Izinso sizidzachitika.”
Niin Herra katui myös sitä: ei senkään pidä tapahtuman, sanoi Herra, Herra.
7 Zimene Iye anandionetsa ndi izi: Ambuye anayima pambali pa khoma lomangamanga, mʼmanja mwake muli chingwe chowongolera khoma.
Mutta hän osoitti minulle tämän näyssä, ja katso, Herra seisoi muurin päällä, joka mittanuoralla mitattu oli, ja hän piti mittanuoran kädessänsä.
8 Ndipo Ambuye anandifunsa kuti, “Amosi, nʼchiyani ukuonachi?” Ine ndinayankha kuti, “Chingwe chowongolera khoma.” Ndipo Yehova anati, “Taona, Ine ndikuyika chingwe chowongolerachi pakati pa anthu anga, Aisraeli; sindidzawalekereranso.
Ja Herra sanoi minulle: mitäs näet, Amos? minä sanoin: mittanuoran. Herra sanoi: katso, minä tahdon vetää mittanuoran keskelle minun kansaani Israelia, ja en käy enään häntä ohitse.
9 “Malo achipembedzo a Isake adzawonongedwa ndipo malo opatulika a Israeli adzasanduka bwinja; ndidzagwetsa nyumba ya Yeroboamu ndi lupanga langa.”
Vaan Isaakin korkeudet pitää autioksi tuleman, ja Israelin pyhyydet pitää hävitettämän; ja minä tahdon nostaa miekan Jerobeamin huonetta vastaan.
10 Pamenepo Amaziya wansembe wa ku Beteli anatumiza uthenga kwa Yeroboamu mfumu ya Israeli kuti, “Amosi akukuutsirani chiwembu pakati pa Aisraeli. Dziko silingalekerere zonena zake zonsezo.
Niin Betelin pappi Amatsia lähetti Israelin kuninkaan tykö, sanoen: Amos tekee kapinan sinua vastaan Israelin huoneessa, eipä maakaan voi kaikkia hänen sanojansa kärsiä.
11 Pakuti zimene Amosi akunena ndi izi: “‘Yeroboamu adzaphedwa ndi lupanga, ndipo Israeli adzapita ndithu ku ukapolo, kutali ndi dziko lake.’”
Sillä näin sanoo Amos: Jerobeamin täytyy miekalla kuolla, ja Israel pitää vietämän vangittuna pois maastansa.
12 Ndipo Amaziya anawuza Amosi kuti, “Choka, mlosi iwe! Bwerera ku dziko la Yuda. Uzikalosera kumeneko ndipo anthu a kumeneko azikakudyetsa.
Ja Amatsia sanoi Amokselle: sinä näkiä, mene pois, ja ennusta siellä.
13 Usanenerenso ku Beteli, chifukwa kumeneko ndi malo opatulika a mfumu ndiponso ndi malo a nyumba yachipembedzo yaufumu.”
Ja älä Betelissä enään ennusta; se on kuninkaan pyhä sia ja valtakunnan huone.
14 Amosi anayankha Amaziya kuti, “Ine sindine mneneri kapena mwana wa mneneri; koma ndine woweta ziweto, ndiponso mlimi wa nkhuyu.
Amos vastasi ja sanoi Amatsialle: en minä ole propheta enkä prophetan poika, vaan minä olen karjan paimen ja marjain hakia.
15 Koma Yehova ananditenga ndikuweta nkhosa ndipo anati, ‘Pita ukanenere kwa anthu anga Aisraeli.’
Mutta Herra otti minun karjasta, ja sanoi minulle: mene ja ennusta minun kansaani Israelia vastaan.
16 Tsono imva mawu a Yehova. Iwe ukunena kuti, “‘Usanenere zotsutsa Israeli, ndipo siya kulalikira motsutsa nyumba ya Isake.’”
Niin kuule siis Herran sanaa: sinä sanot: älä ennusta Israelia vastaan, älä myös puhu Isaakin huonetta vastaan;
17 “Tsono zimene akunena Yehova ndi izi: “‘Mkazi wako adzasanduka wachiwerewere mu mzindamu, ndipo ana ako aamuna ndi aakazi adzaphedwa ndi lupanga. Munda wako udzayezedwa ndi chingwe ndi kugawidwa, ndipo iwe mwini udzafera mʼdziko la anthu osapembedza Mulungu. Ndipo Israeli adzatengedwa ndithu kupita ku ukapolo, kutali ndi dziko lake.’”
Sentähden sanoo Herra näin: sinun emäntäs pitää kaupungissa raiskattaman, ja sinun poikas ja tyttäres pitää miekalla lankeeman, ja sinun peltos pitää nuoralla jaettaman; mutta itse sinun pitää saastaisessa maassa kuoleman, ja Israel pitää ajettaman peräti pois maastansa.

< Amosi 7 >