< Amosi 7 >

1 Zimene Ambuye Yehova anandionetsa ndi izi: Yehova ankasonkhanitsa gulu la dzombe nthawi imene gawo la zokolola za mfumu linali litakololedwa kale ndipo mbewu zachiwiri zinali zitangoyamba kumera kumene.
thus to see: see me Lord YHWH/God and behold to form: formed locust in/on/with beginning to ascend: rise [the] spring crop and behold spring crop after fleece [the] king
2 Dzombelo litadya zomera zonse za mʼdzikomo, Ine ndinafuwula kuti, “Ambuye Yehova, khululukani! Kodi Yakobo adzapulumuka bwanji? Iye ndi wofowoka kwambiri!”
and to be if to end: finish to/for to eat [obj] vegetation [the] land: country/planet and to say Lord YHWH/God to forgive please who? to arise: establish Jacob for small he/she/it
3 Kotero Yehova anakhululuka. Yehovayo anati, “Izi sizidzachitika.”
to be sorry: relent LORD upon this not to be to say LORD
4 Zimene Ambuye Yehova anandionetsa ndi izi: Ambuye Yehova ankayitana malawi a moto kuti alange anthu. Motowo unawumitsa nyanja yakuya ndi kupsereza dziko.
thus to see: see me Lord YHWH/God and behold to call: call to to/for to contend in/on/with fire Lord YHWH/God and to eat [obj] abyss many and to eat [obj] [the] portion
5 Tsono ine ndinafuwula kuti, “Ambuye Yehova, chonde ndikukupemphani, lekani! Kodi Yakobo adzapulumuka bwanji? Iye ndi wofowoka kwambiri!”
and to say Lord YHWH/God to cease please who? to arise: establish Jacob for small he/she/it
6 Kotero Yehova anakhululuka. Ambuye Yehova anati, “Izinso sizidzachitika.”
to be sorry: relent LORD upon this also he/she/it not to be to say Lord YHWH/God
7 Zimene Iye anandionetsa ndi izi: Ambuye anayima pambali pa khoma lomangamanga, mʼmanja mwake muli chingwe chowongolera khoma.
thus to see: see me and behold Lord to stand upon wall plumbline and in/on/with hand his plumbline
8 Ndipo Ambuye anandifunsa kuti, “Amosi, nʼchiyani ukuonachi?” Ine ndinayankha kuti, “Chingwe chowongolera khoma.” Ndipo Yehova anati, “Taona, Ine ndikuyika chingwe chowongolerachi pakati pa anthu anga, Aisraeli; sindidzawalekereranso.
and to say LORD to(wards) me what? you(m. s.) to see: see Amos and to say plumbline and to say Lord look! I to set: make plumbline in/on/with entrails: among people my Israel not to add: again still to pass to/for him
9 “Malo achipembedzo a Isake adzawonongedwa ndipo malo opatulika a Israeli adzasanduka bwinja; ndidzagwetsa nyumba ya Yeroboamu ndi lupanga langa.”
and be desolate: destroyed high place Isaac and sanctuary Israel to destroy and to arise: attack upon house: household Jeroboam in/on/with sword
10 Pamenepo Amaziya wansembe wa ku Beteli anatumiza uthenga kwa Yeroboamu mfumu ya Israeli kuti, “Amosi akukuutsirani chiwembu pakati pa Aisraeli. Dziko silingalekerere zonena zake zonsezo.
and to send: depart Amaziah priest Bethel Bethel to(wards) Jeroboam king Israel to/for to say to conspire upon you Amos in/on/with entrails: among house: household Israel not be able [the] land: country/planet to/for to sustain [obj] all word his
11 Pakuti zimene Amosi akunena ndi izi: “‘Yeroboamu adzaphedwa ndi lupanga, ndipo Israeli adzapita ndithu ku ukapolo, kutali ndi dziko lake.’”
for thus to say Amos in/on/with sword to die Jeroboam and Israel to reveal: remove to reveal: remove from upon land: soil his
12 Ndipo Amaziya anawuza Amosi kuti, “Choka, mlosi iwe! Bwerera ku dziko la Yuda. Uzikalosera kumeneko ndipo anthu a kumeneko azikakudyetsa.
and to say Amaziah to(wards) Amos seer to go: went to flee to/for you to(wards) land: country/planet Judah and to eat there food: bread and there to prophesy
13 Usanenerenso ku Beteli, chifukwa kumeneko ndi malo opatulika a mfumu ndiponso ndi malo a nyumba yachipembedzo yaufumu.”
and Bethel Bethel not to add: again still to/for to prophesy for sanctuary king he/she/it and house: home kingdom he/she/it
14 Amosi anayankha Amaziya kuti, “Ine sindine mneneri kapena mwana wa mneneri; koma ndine woweta ziweto, ndiponso mlimi wa nkhuyu.
and to answer Amos and to say to(wards) Amaziah not prophet I and not son: child prophet I for herdsman I and to gather/tend figs sycamore
15 Koma Yehova ananditenga ndikuweta nkhosa ndipo anati, ‘Pita ukanenere kwa anthu anga Aisraeli.’
and to take: take me LORD from after [the] flock and to say to(wards) me LORD to go: went to prophesy to(wards) people my Israel
16 Tsono imva mawu a Yehova. Iwe ukunena kuti, “‘Usanenere zotsutsa Israeli, ndipo siya kulalikira motsutsa nyumba ya Isake.’”
and now to hear: hear word LORD you(m. s.) to say not to prophesy upon Israel and not to drip/prophesy upon house: household Isaac
17 “Tsono zimene akunena Yehova ndi izi: “‘Mkazi wako adzasanduka wachiwerewere mu mzindamu, ndipo ana ako aamuna ndi aakazi adzaphedwa ndi lupanga. Munda wako udzayezedwa ndi chingwe ndi kugawidwa, ndipo iwe mwini udzafera mʼdziko la anthu osapembedza Mulungu. Ndipo Israeli adzatengedwa ndithu kupita ku ukapolo, kutali ndi dziko lake.’”
to/for so thus to say LORD woman: wife your in/on/with city to fornicate and son: child your and daughter your in/on/with sword to fall: kill and land: soil your in/on/with cord to divide and you(m. s.) upon land: soil unclean to die and Israel to reveal: remove to reveal: remove from upon land: soil his

< Amosi 7 >