< Amosi 7 >
1 Zimene Ambuye Yehova anandionetsa ndi izi: Yehova ankasonkhanitsa gulu la dzombe nthawi imene gawo la zokolola za mfumu linali litakololedwa kale ndipo mbewu zachiwiri zinali zitangoyamba kumera kumene.
Ka Boeipa Yahovah loh he he kai n'tueng. Canghnong a moe cuek vaengah yuet a tawn ne. Te dongah manghai lotul phoeikah canghnong ni ne.
2 Dzombelo litadya zomera zonse za mʼdzikomo, Ine ndinafuwula kuti, “Ambuye Yehova, khululukani! Kodi Yakobo adzapulumuka bwanji? Iye ndi wofowoka kwambiri!”
Khohmuen kah baelhing caak ham a khah coeng. Te dongah, “Ka Boeipa Yahovah aw, khodawkngai mai, Jakob amah he noe oeh tih ulong a thoh eh?,” ka ti.
3 Kotero Yehova anakhululuka. Yehovayo anati, “Izi sizidzachitika.”
BOEIPA loh ko a hlawt dongah BOEIPA loh, “He he om mahpawh,” a ti.
4 Zimene Ambuye Yehova anandionetsa ndi izi: Ambuye Yehova ankayitana malawi a moto kuti alange anthu. Motowo unawumitsa nyanja yakuya ndi kupsereza dziko.
Ka Boeipa Yahovah loh he he kai m'hmuh sak. Ho hamla ka Boeipa Yahovah loh hmai neh a khue coeng ke. Tuidung puei te a yoop tih khoyo te a hlawp.
5 Tsono ine ndinafuwula kuti, “Ambuye Yehova, chonde ndikukupemphani, lekani! Kodi Yakobo adzapulumuka bwanji? Iye ndi wofowoka kwambiri!”
Te vaengah, “Ka Boeipa Yahovah aw, paa mai laeh, Jakob amah he noe oeh tih ulong a thoh eh?,” ka ti.
6 Kotero Yehova anakhululuka. Ambuye Yehova anati, “Izinso sizidzachitika.”
He ham he BOEIPA loh ko a hlawt dongah ka Boeipa Yahovah loh, “Te khaw om mahpawh,” a ti.
7 Zimene Iye anandionetsa ndi izi: Ambuye anayima pambali pa khoma lomangamanga, mʼmanja mwake muli chingwe chowongolera khoma.
He he kai n'tueng vaengah ka Boeipa tah vongtung soah mikrhael rhui neh pai tih a kut dongah mikrhael rhui om.
8 Ndipo Ambuye anandifunsa kuti, “Amosi, nʼchiyani ukuonachi?” Ine ndinayankha kuti, “Chingwe chowongolera khoma.” Ndipo Yehova anati, “Taona, Ine ndikuyika chingwe chowongolerachi pakati pa anthu anga, Aisraeli; sindidzawalekereranso.
Te phoeiah BOEIPA loh kai taengah, “Amos nang balae na hmuh,” n'ti nah tih, “Mikrhael rhui,” ka ti nah. Te dongah ka Boeipa, “Ka pilnam Israel lakli ah mikrhael rhui ka khueh coeng ne. Anih te pah hamla ka koei voel mahpawh.
9 “Malo achipembedzo a Isake adzawonongedwa ndipo malo opatulika a Israeli adzasanduka bwinja; ndidzagwetsa nyumba ya Yeroboamu ndi lupanga langa.”
Isaak kah hmuensang te pong vetih Israel kah rhokso khaw khap uh ni. Jeroboam imkhui te cunghang neh ka pai thil ni,” a ti.
10 Pamenepo Amaziya wansembe wa ku Beteli anatumiza uthenga kwa Yeroboamu mfumu ya Israeli kuti, “Amosi akukuutsirani chiwembu pakati pa Aisraeli. Dziko silingalekerere zonena zake zonsezo.
Te vaengah Bethel khosoih Amaziah te Israel manghai Jeroboam taengla a tueih tih, “Israel im kah kotak ah Amos loh nang n'taeng thil. A ol boeih ueh ham khaw khohmuen loh a noeng moenih.
11 Pakuti zimene Amosi akunena ndi izi: “‘Yeroboamu adzaphedwa ndi lupanga, ndipo Israeli adzapita ndithu ku ukapolo, kutali ndi dziko lake.’”
Te dongah Amos loh, 'Jeroboam te cunghang dongah duek vetih Israel te a khohmuen dong lamloh a poelyoe rhoe a poelyoe ni, ' a ti,” a ti nah.
12 Ndipo Amaziya anawuza Amosi kuti, “Choka, mlosi iwe! Bwerera ku dziko la Yuda. Uzikalosera kumeneko ndipo anthu a kumeneko azikakudyetsa.
Te vaengah Amaziah loh Amos te, “Khohmu Nang te Judah khohmuen la cet lamtah yong laeh. Buh pahoi ca lamtah hnap tonghma nawn.
13 Usanenerenso ku Beteli, chifukwa kumeneko ndi malo opatulika a mfumu ndiponso ndi malo a nyumba yachipembedzo yaufumu.”
Tedae Bethel te tonghma thil ham koep koei boeh. He he manghai rhokso neh ram kah im ni,” a ti nah.
14 Amosi anayankha Amaziya kuti, “Ine sindine mneneri kapena mwana wa mneneri; koma ndine woweta ziweto, ndiponso mlimi wa nkhuyu.
Te dongah Amos loh a doo tih Amaziah te, “Kai he tonghma moenih, kai he tonghma capa moenih. Kai he saeldawn ni, thaihae ni ka hloe.
15 Koma Yehova ananditenga ndikuweta nkhosa ndipo anati, ‘Pita ukanenere kwa anthu anga Aisraeli.’
Tedae BOEIPA loh kai he boiva hnuk lamloh n'loh. Te vaengah BOEIPA loh kai te, “Cet lamtah ka pilnam Israel taengah tonghma laeh,” a ti.
16 Tsono imva mawu a Yehova. Iwe ukunena kuti, “‘Usanenere zotsutsa Israeli, ndipo siya kulalikira motsutsa nyumba ya Isake.’”
Te dongah, 'Israel taengah tonghma boel lamtah Isaak imkhui te saep boeh,’ na ti akhaw BOEIPA ol mah hnatun dae.
17 “Tsono zimene akunena Yehova ndi izi: “‘Mkazi wako adzasanduka wachiwerewere mu mzindamu, ndipo ana ako aamuna ndi aakazi adzaphedwa ndi lupanga. Munda wako udzayezedwa ndi chingwe ndi kugawidwa, ndipo iwe mwini udzafera mʼdziko la anthu osapembedza Mulungu. Ndipo Israeli adzatengedwa ndithu kupita ku ukapolo, kutali ndi dziko lake.’”
Te dongah BOEIPA loh he ni a thui. Na yuu te khopuei khuiah cukhalh vetih na capa neh na canu te cunghang dongah cungku uh ni. Na khohmuen khaw rhuihet loh a boe ni. Namah khaw diklai ah rhalawt la na duek ni. Israel te a khohmuen dongah lamloh a poelyoe rhoe a poelyoe uh ni,” a ti nah.