< Amosi 6 >
1 Tsoka kwa amene simukulabadira kanthu ku Ziyoni, ndiponso kwa inu amene mukukhala mwamtendere pa Phiri la Samariya, inu anthu otchuka ochokera ku mtundu wa anthu omveka, kumene Aisraeli amafikako!
Горе безпе́чним на Сіоні, тим, хто наді́ється на самарійськую го́ру, тим шляхе́тним „першого з наро́дів“, до яких прибува́є Ізраїлів дім!
2 Pitani ku mzinda wa Kaline mukawuyangʼane; mukapitenso ku Hamati-raba mzinda waukulu uja, ndipo mukatsikirenso ku Gati kwa Afilisti. Kodi mizinda imeneyi ndi yopambana maufumu anu awiriwa? Kodi dziko lawo ndi lalikulu kupambana lanu?
Перейді́ть до Калне́ та й побачте, і звідти підіть до Гама́ту великого, і зійді́ть до Ґату филисти́млян! Чи ліпші вони від цих царств? Чи їхня границя більша за вашу границю?
3 Inu simulabadirako kuti tsiku loyipa lidzafika, zochita zanu zimafulumizitsa ulamuliro wankhanza.
День нещастя вважаєте ви за далекий, а час насильства зближа́єте!
4 Mumagona pa mabedi owakongoletsa ndi minyanga ya njovu, mumagona pa mipando yanu ya wofuwofu. Mumadya ana ankhosa onona ndi ana angʼombe onenepa.
Ви виле́жуєтеся на ло́жах з слоно́вої кости і вива́люєтесь на постелях своїх, і їсте барані́в із отари та ситих теля́т із обо́ри.
5 Mumayimba azeze anu ndi kumangopeka nyimbo pa zingʼwenyengʼwenye ngati Davide.
Під гу́сла співаєте ви, мов Давид, ви музичні знаря́ддя собі видумля́єте.
6 Mumamwera vinyo mʼzipanda zodzaza ndipo mumadzola mafuta abwino kwambiri, koma simumva chisoni ndi kuwonongeka kwa Yosefe.
Ви вино попива́єте ча́шами, і намащуєтесь добірною оливою, і над спусто́шенням Йо́сипа не вболіва́єте.
7 Nʼchifukwa chake inu mudzakhala mʼgulu la anthu oyamba kupita ku ukapolo; maphwando ndi zikondwerero zanu zidzatheratu.
Тому́ вони пі́дуть тепер на вигна́ння на чолі́ полоне́них, і перестане крик ви́пещених.
8 Ambuye Yehova walumbira mʼdzina lake. Yehova Mulungu Wamphamvuzonse walengeza kuti, “Ndimanyansidwa ndi kunyada kwa Yakobo, ndimadana ndi nyumba zake zaufumu; Ine ndidzawupereka mzindawu pamodzi ndi zonse zili mʼmenemo.”
Господь присягнув був Своєю душею, говорить Господь, Бог Савао́т: Пишно́тою Якова бриджу, і пала́ти його Я нена́виджу, і видам те місто та все, що є в ньо́му.
9 Ngati anthu khumi otsala adzabisala mʼnyumba imodzi, nawonso adzafa ndithu.
І бу́де, якщо десять лю́да зоста́нуться в домі одно́му, то й вони повмирають.
10 Ndipo ngati mʼbale wake wa wina wakufayo, woyenera kusamala za maliro, adzafika kudzatulutsa mitembo mʼnyumbamo nʼkufunsa aliyense amene akubisalabe mʼnyumbamo kuti, “Kodi uli ndi wina wamoyo mʼmenemo?” Ndipo munthu wobisalayo ndi kuyankha kuti, “Ayi,” mʼbaleyo adzanena kuti, “Khala chete! Ife tisayerekeze kutchula dzina la Yehova.”
І його візьме родич та й спалить його, щоб ви́нести кості із дому, і скаже до того, хто буде в сере́дині дому: „Чи ще є хто з тобою?“А той відповість: „ Вже немає ніко́го!“і скаже той: „Тихше, бо не згадується Йме́ння Господа!“
11 Pakuti Yehova walamula kuti nyumba zikuluzikulu Iye adzazigamulagamula, ndipo nyumba zazingʼono zidzasanduka maduka okhaokha.
Бо Господь ось накаже, — і ворог розі́б'є великий той дім на відла́мки, а дім мали́й — на тріски́.
12 Kodi akavalo amathamanga pa thanthwe? Kodi wina amatipula ndi ngʼombe mʼnyanja? Koma chiweruzo cholungama mwachisandutsa kukhala zinthu zakupha ndipo chipatso cha chilungamo mwachisandutsa kukhala chowawa.
Чи бігають коні по ске́лі? Чи хто виоре море худобою? Таж ви суд обернули на гіркість, а плід справедливости — на поли́н!
13 Inu amene mukunyadira kuti munagonjetsa Lo Debara ndipo mukunena kuti, “Kodi sitinatenge Karinaimu ndi mphamvu zathu zokha?”
Ви марно́тою тішитеся та говорите: Хіба ж ми не власною силою набули́ собі роги?
14 Koma Yehova Mulungu Wamphamvuzonse akulengeza kuti, “Inu nyumba ya Israeli, ndidzakudzutsirani mtundu wina wa anthu umene udzakuzunzani kuchokera ku Lebo Hamati mpaka ku Chigwa cha Araba.”
Бо ось Я поставлю наро́д проти вас, доме Ізраїлів, — каже Госпо́дь, Бог Савао́т, — і вони вас потиснуть ізвідти, де йдуть до Гама́ту, аж до степово́го пото́ку!