< Amosi 6 >

1 Tsoka kwa amene simukulabadira kanthu ku Ziyoni, ndiponso kwa inu amene mukukhala mwamtendere pa Phiri la Samariya, inu anthu otchuka ochokera ku mtundu wa anthu omveka, kumene Aisraeli amafikako!
Biada beztroskim na Syjonie i pokładającym ufność w górze Samarii; tym, którzy są przywódcami wśród tych narodów, do których schodzi się dom Izraela.
2 Pitani ku mzinda wa Kaline mukawuyangʼane; mukapitenso ku Hamati-raba mzinda waukulu uja, ndipo mukatsikirenso ku Gati kwa Afilisti. Kodi mizinda imeneyi ndi yopambana maufumu anu awiriwa? Kodi dziko lawo ndi lalikulu kupambana lanu?
Idźcie do Kalne i rozejrzyjcie się, a stamtąd idźcie do Chamat wielkiego. Potem zstąpcie do Gat filistyńskiego. Czy są to lepsze królestwa niż te? Czy ich obszar jest większy niż wasz obszar?
3 Inu simulabadirako kuti tsiku loyipa lidzafika, zochita zanu zimafulumizitsa ulamuliro wankhanza.
[Biada wam, którzy sądzicie], że dzień zły jest daleko i przybliżacie panowanie przemocy;
4 Mumagona pa mabedi owakongoletsa ndi minyanga ya njovu, mumagona pa mipando yanu ya wofuwofu. Mumadya ana ankhosa onona ndi ana angʼombe onenepa.
Którzy sypiacie na łożach z kości słoniowej, a rozciągacie się na swoich posłaniach; którzy jadacie jagnięta z trzody, a cielce tuczone z zagrody;
5 Mumayimba azeze anu ndi kumangopeka nyimbo pa zingʼwenyengʼwenye ngati Davide.
Którzy śpiewacie przy lutni i wymyślacie sobie instrumenty muzyczne jak Dawid;
6 Mumamwera vinyo mʼzipanda zodzaza ndipo mumadzola mafuta abwino kwambiri, koma simumva chisoni ndi kuwonongeka kwa Yosefe.
Którzy pijecie wino z czasz i namaszczacie się drogimi maściami, a nie bolejecie nad utrapieniem Józefa.
7 Nʼchifukwa chake inu mudzakhala mʼgulu la anthu oyamba kupita ku ukapolo; maphwando ndi zikondwerero zanu zidzatheratu.
Dlatego teraz pójdą do niewoli na czele pojmanych i skończy się biesiada hulaków.
8 Ambuye Yehova walumbira mʼdzina lake. Yehova Mulungu Wamphamvuzonse walengeza kuti, “Ndimanyansidwa ndi kunyada kwa Yakobo, ndimadana ndi nyumba zake zaufumu; Ine ndidzawupereka mzindawu pamodzi ndi zonse zili mʼmenemo.”
Pan BÓG przysiągł na siebie samego, mówi PAN, Bóg zastępów: Obrzydła mi pycha Jakuba i nienawidzę jego pałaców. Dlatego wydam miasto i wszystko, co w nim jest.
9 Ngati anthu khumi otsala adzabisala mʼnyumba imodzi, nawonso adzafa ndithu.
A stanie się tak: Jeśli pozostanie dziesięć osób w jednym domu i one pomrą.
10 Ndipo ngati mʼbale wake wa wina wakufayo, woyenera kusamala za maliro, adzafika kudzatulutsa mitembo mʼnyumbamo nʼkufunsa aliyense amene akubisalabe mʼnyumbamo kuti, “Kodi uli ndi wina wamoyo mʼmenemo?” Ndipo munthu wobisalayo ndi kuyankha kuti, “Ayi,” mʼbaleyo adzanena kuti, “Khala chete! Ife tisayerekeze kutchula dzina la Yehova.”
I każdego z nich weźmie jego stryj, i spali go, aby wynieść kości z domu, i zapyta tego, który jest w zakątkach domu: Czy jest jeszcze ktoś z tobą? A [ten] odpowie: Nie ma. Wtedy powie: Milcz, bo nie wolno wspominać imienia PANA.
11 Pakuti Yehova walamula kuti nyumba zikuluzikulu Iye adzazigamulagamula, ndipo nyumba zazingʼono zidzasanduka maduka okhaokha.
Oto bowiem PAN rozkaże i uderzy w wielki dom rozpadlinami, a w mały dom – pęknięciem.
12 Kodi akavalo amathamanga pa thanthwe? Kodi wina amatipula ndi ngʼombe mʼnyanja? Koma chiweruzo cholungama mwachisandutsa kukhala zinthu zakupha ndipo chipatso cha chilungamo mwachisandutsa kukhala chowawa.
Czy konie mogą biegać po skale? Czy można [tam] orać wołami? Sąd bowiem zamieniliście w truciznę, a owoc sprawiedliwości w piołun.
13 Inu amene mukunyadira kuti munagonjetsa Lo Debara ndipo mukunena kuti, “Kodi sitinatenge Karinaimu ndi mphamvu zathu zokha?”
[Biada wam], którzy się cieszycie, a to z niczego, mówiąc: Czy nie wzięliśmy sobie rogów własną siłą?
14 Koma Yehova Mulungu Wamphamvuzonse akulengeza kuti, “Inu nyumba ya Israeli, ndidzakudzutsirani mtundu wina wa anthu umene udzakuzunzani kuchokera ku Lebo Hamati mpaka ku Chigwa cha Araba.”
Ale oto ja wzbudzę naród przeciwko wam, domu Izraela, mówi PAN, Bóg zastępów, który was będzie uciskał od wejścia do Chamat aż do strumienia pustyni.

< Amosi 6 >