< Amosi 6 >

1 Tsoka kwa amene simukulabadira kanthu ku Ziyoni, ndiponso kwa inu amene mukukhala mwamtendere pa Phiri la Samariya, inu anthu otchuka ochokera ku mtundu wa anthu omveka, kumene Aisraeli amafikako!
Malheur à vous, qui vous croyez en sécurité à Sion, et à vous, si pleins de quiétude sur le mont de Samarie, qui formez l’élite de la première des nations et attirez à vous la maison d’Israël!
2 Pitani ku mzinda wa Kaline mukawuyangʼane; mukapitenso ku Hamati-raba mzinda waukulu uja, ndipo mukatsikirenso ku Gati kwa Afilisti. Kodi mizinda imeneyi ndi yopambana maufumu anu awiriwa? Kodi dziko lawo ndi lalikulu kupambana lanu?
Passez donc à Calné et regardez; de là, rendez-vous à Hamath-la-Grande, puis descendez à Gath au pays des Philistins: sont-ils plus prospères que ces royaumes-ci, leur territoire est-il plus considérable que le vôtre?
3 Inu simulabadirako kuti tsiku loyipa lidzafika, zochita zanu zimafulumizitsa ulamuliro wankhanza.
Vous vous imaginez reculer le jour du malheur et vous avancez le règne de la violence!
4 Mumagona pa mabedi owakongoletsa ndi minyanga ya njovu, mumagona pa mipando yanu ya wofuwofu. Mumadya ana ankhosa onona ndi ana angʼombe onenepa.
Couchés sur des lits d’ivoire, étendus sur leurs divans, nourris d’agneaux choisis dans le troupeau, de veaux mis à l’engrais,
5 Mumayimba azeze anu ndi kumangopeka nyimbo pa zingʼwenyengʼwenye ngati Davide.
fredonnant au son du luth, comme David inventant à leur usage des instruments de musique,
6 Mumamwera vinyo mʼzipanda zodzaza ndipo mumadzola mafuta abwino kwambiri, koma simumva chisoni ndi kuwonongeka kwa Yosefe.
ils boivent du vin à même les amphores, se frottent d’huiles de choix et ne s’affligent guère du désastre de Joseph!
7 Nʼchifukwa chake inu mudzakhala mʼgulu la anthu oyamba kupita ku ukapolo; maphwando ndi zikondwerero zanu zidzatheratu.
C’Est pourquoi, tantôt, ils s’en iront en tête des déportés; alors c’en sera fini des chants bruyants de ces voluptueux.
8 Ambuye Yehova walumbira mʼdzina lake. Yehova Mulungu Wamphamvuzonse walengeza kuti, “Ndimanyansidwa ndi kunyada kwa Yakobo, ndimadana ndi nyumba zake zaufumu; Ine ndidzawupereka mzindawu pamodzi ndi zonse zili mʼmenemo.”
"Le Seigneur a juré par lui-même, c’est la parole de l’Eternel Dieu-Cebaot: Je déteste l’orgueil de Jacob, je hais ses palais, je livrerai donc en proie la ville et ce qu’elle renferme.
9 Ngati anthu khumi otsala adzabisala mʼnyumba imodzi, nawonso adzafa ndithu.
Que s’il reste dix hommes dans une maison, ils mourront.
10 Ndipo ngati mʼbale wake wa wina wakufayo, woyenera kusamala za maliro, adzafika kudzatulutsa mitembo mʼnyumbamo nʼkufunsa aliyense amene akubisalabe mʼnyumbamo kuti, “Kodi uli ndi wina wamoyo mʼmenemo?” Ndipo munthu wobisalayo ndi kuyankha kuti, “Ayi,” mʼbaleyo adzanena kuti, “Khala chete! Ife tisayerekeze kutchula dzina la Yehova.”
Et quand le proche parent, chargé de l’incinération, emportera le corps afin de débarrasser la maison des ossements, il demandera à celui qui se trouve au fond de l’appartement: "Y a-t-il encore quelqu’un?", et l’autre répondra: "Non, personne!" et ajoutera: "Silence!" car ce ne sera pas le moment de prononcer le nom de l’Eternel."
11 Pakuti Yehova walamula kuti nyumba zikuluzikulu Iye adzazigamulagamula, ndipo nyumba zazingʼono zidzasanduka maduka okhaokha.
En vérité, l’Eternel donne des ordres: il fera tomber en ruines les grandes maisons et mettra en morceaux les petites.
12 Kodi akavalo amathamanga pa thanthwe? Kodi wina amatipula ndi ngʼombe mʼnyanja? Koma chiweruzo cholungama mwachisandutsa kukhala zinthu zakupha ndipo chipatso cha chilungamo mwachisandutsa kukhala chowawa.
Est-ce que les chevaux courent sur le roc? Le laboure-t-on avec des bœufs? Mais vous, vous avez changé le bon droit en poison, et l’œuvre de la justice en plante vénéneuse.
13 Inu amene mukunyadira kuti munagonjetsa Lo Debara ndipo mukunena kuti, “Kodi sitinatenge Karinaimu ndi mphamvu zathu zokha?”
Vous trouvez votre joie dans ce qui est néant, vous dites: "N’Est-ce pas grâce à notre énergie que nous avons conquis la puissance?"
14 Koma Yehova Mulungu Wamphamvuzonse akulengeza kuti, “Inu nyumba ya Israeli, ndidzakudzutsirani mtundu wina wa anthu umene udzakuzunzani kuchokera ku Lebo Hamati mpaka ku Chigwa cha Araba.”
Eh bien! Me voici, suscitant contre vous, maison d’Israël, dit l’Eternel, Dieu-Cebaot, un peuple qui vous serrera de près dès la région de Hamath jusqu’au torrent de la Plaine.

< Amosi 6 >