< Amosi 6 >

1 Tsoka kwa amene simukulabadira kanthu ku Ziyoni, ndiponso kwa inu amene mukukhala mwamtendere pa Phiri la Samariya, inu anthu otchuka ochokera ku mtundu wa anthu omveka, kumene Aisraeli amafikako!
Voi suruttomia Siionissa, huolettomia Samarian vuorella, kansoista ensimmäisen ylimyksiä, joiden tykö Israelin heimo tulee!
2 Pitani ku mzinda wa Kaline mukawuyangʼane; mukapitenso ku Hamati-raba mzinda waukulu uja, ndipo mukatsikirenso ku Gati kwa Afilisti. Kodi mizinda imeneyi ndi yopambana maufumu anu awiriwa? Kodi dziko lawo ndi lalikulu kupambana lanu?
Menkää Kalneen ja katsokaa, sieltä kulkekaa Suureen Hamatiin ja käykää filistealaisten Gatiin: ovatko ne paremmat kuin nämä valtakunnat, onko niiden alue suurempi kuin teidän alueenne?
3 Inu simulabadirako kuti tsiku loyipa lidzafika, zochita zanu zimafulumizitsa ulamuliro wankhanza.
Voi teitä, jotka lykkäätte kauas pahan päivän, mutta vedätte luoksenne väkivallan, valtaistuimelle istumaan;
4 Mumagona pa mabedi owakongoletsa ndi minyanga ya njovu, mumagona pa mipando yanu ya wofuwofu. Mumadya ana ankhosa onona ndi ana angʼombe onenepa.
jotka makaatte norsunluusohvilla ja venytte leposijoillanne, syötte karitsoita laumasta ja vasikoita navetasta;
5 Mumayimba azeze anu ndi kumangopeka nyimbo pa zingʼwenyengʼwenye ngati Davide.
jotka sepustatte lauluja harpulla säestäen ja sommittelette soittimia kuin mikäkin Daavid;
6 Mumamwera vinyo mʼzipanda zodzaza ndipo mumadzola mafuta abwino kwambiri, koma simumva chisoni ndi kuwonongeka kwa Yosefe.
jotka juotte viiniä maljoista ja voitelette itsenne parhaalla öljyllä, mutta ette murehdi Joosefin sortumista!
7 Nʼchifukwa chake inu mudzakhala mʼgulu la anthu oyamba kupita ku ukapolo; maphwando ndi zikondwerero zanu zidzatheratu.
Sentähden heidän nyt täytyy mennä pakkosiirtolaisuuteen pakkosiirtolaisten etunenässä. Silloin lakkaavat venyjäin ilohuudot.
8 Ambuye Yehova walumbira mʼdzina lake. Yehova Mulungu Wamphamvuzonse walengeza kuti, “Ndimanyansidwa ndi kunyada kwa Yakobo, ndimadana ndi nyumba zake zaufumu; Ine ndidzawupereka mzindawu pamodzi ndi zonse zili mʼmenemo.”
Herra, Herra on vannonut itse kauttansa, sanoo Herra, Jumala Sebaot: Jaakobin ylpeys on minulle kauhistus, minä vihaan hänen palatsejansa, ja minä jätän alttiiksi kaupungin kaikkinensa.
9 Ngati anthu khumi otsala adzabisala mʼnyumba imodzi, nawonso adzafa ndithu.
Ja jos silloin kymmenen miestä jää jäljelle yhteen taloon, niin he kuolevat.
10 Ndipo ngati mʼbale wake wa wina wakufayo, woyenera kusamala za maliro, adzafika kudzatulutsa mitembo mʼnyumbamo nʼkufunsa aliyense amene akubisalabe mʼnyumbamo kuti, “Kodi uli ndi wina wamoyo mʼmenemo?” Ndipo munthu wobisalayo ndi kuyankha kuti, “Ayi,” mʼbaleyo adzanena kuti, “Khala chete! Ife tisayerekeze kutchula dzina la Yehova.”
Ja jos kuolleen korjaa hänen omaisensa ja polttajansa, viedäkseen luut pois talosta, ja jos hän kysyy joltakin, joka on talon perimmäisessä sopessa: "Onko sinun tykönäsi vielä ketään?" niin tämä vastaa: "Ei ole", ja toinen sanoo: "Hiljaa!" -sillä Herran nimeä ei saa mainita.
11 Pakuti Yehova walamula kuti nyumba zikuluzikulu Iye adzazigamulagamula, ndipo nyumba zazingʼono zidzasanduka maduka okhaokha.
Sillä katso, Herra antaa käskyn, ja hän lyö suuren talon kappaleiksi ja pienen talon pirstaleiksi.
12 Kodi akavalo amathamanga pa thanthwe? Kodi wina amatipula ndi ngʼombe mʼnyanja? Koma chiweruzo cholungama mwachisandutsa kukhala zinthu zakupha ndipo chipatso cha chilungamo mwachisandutsa kukhala chowawa.
Juoksevatko hevoset kallionseinää, kynnetäänkö sitä härjillä? Sillä te muutatte oikeuden myrkyksi ja vanhurskauden hedelmän koiruohoksi,
13 Inu amene mukunyadira kuti munagonjetsa Lo Debara ndipo mukunena kuti, “Kodi sitinatenge Karinaimu ndi mphamvu zathu zokha?”
te, jotka iloitsette Loodabarista ja jotka sanotte: "Emmekö omalla voimallamme valloittaneet Karnaimia?"
14 Koma Yehova Mulungu Wamphamvuzonse akulengeza kuti, “Inu nyumba ya Israeli, ndidzakudzutsirani mtundu wina wa anthu umene udzakuzunzani kuchokera ku Lebo Hamati mpaka ku Chigwa cha Araba.”
Sillä katso, minä nostatan teitä vastaan, te Israelin heimo, sanoo Herra, Jumala Sebaot, kansan, joka on ahdistava teitä siitä asti, mistä mennään Hamatiin, hamaan Pajupuroon saakka.

< Amosi 6 >