< Amosi 6 >

1 Tsoka kwa amene simukulabadira kanthu ku Ziyoni, ndiponso kwa inu amene mukukhala mwamtendere pa Phiri la Samariya, inu anthu otchuka ochokera ku mtundu wa anthu omveka, kumene Aisraeli amafikako!
Alas for the careless in Zion, and for them who put confidence in the mountain of Samaria, —the distinguished among the first group of nations, to whom came in the house of Israel.
2 Pitani ku mzinda wa Kaline mukawuyangʼane; mukapitenso ku Hamati-raba mzinda waukulu uja, ndipo mukatsikirenso ku Gati kwa Afilisti. Kodi mizinda imeneyi ndi yopambana maufumu anu awiriwa? Kodi dziko lawo ndi lalikulu kupambana lanu?
Pass ye over to Calneh, and see, and go on from thence to Hamath the great, —and go down to Gath of the Philistines, are they better than these kingdoms? or their boundary larger than your boundary?
3 Inu simulabadirako kuti tsiku loyipa lidzafika, zochita zanu zimafulumizitsa ulamuliro wankhanza.
Ye who are putting far away the day of calamity, —but bringing near the abode of violence:
4 Mumagona pa mabedi owakongoletsa ndi minyanga ya njovu, mumagona pa mipando yanu ya wofuwofu. Mumadya ana ankhosa onona ndi ana angʼombe onenepa.
Who are lying on beds of ivory, and sprawling on their couch of pleasure, —and eating the well-fed of the flock, and the fatted calves out of the midst of the stalls:
5 Mumayimba azeze anu ndi kumangopeka nyimbo pa zingʼwenyengʼwenye ngati Davide.
Who are bawling at the bidding of the harp, —like David, have they invented for themselves instruments of song:
6 Mumamwera vinyo mʼzipanda zodzaza ndipo mumadzola mafuta abwino kwambiri, koma simumva chisoni ndi kuwonongeka kwa Yosefe.
Who are quaffing bowls of wine, and, with the best of oils, anointing themselves, —and are not afflicted for the injury of Joseph: —
7 Nʼchifukwa chake inu mudzakhala mʼgulu la anthu oyamba kupita ku ukapolo; maphwando ndi zikondwerero zanu zidzatheratu.
Therefore, at once, shall they go into exile among the first of the exiles, —so shall be disturbed the revelry of sprawlers.
8 Ambuye Yehova walumbira mʼdzina lake. Yehova Mulungu Wamphamvuzonse walengeza kuti, “Ndimanyansidwa ndi kunyada kwa Yakobo, ndimadana ndi nyumba zake zaufumu; Ine ndidzawupereka mzindawu pamodzi ndi zonse zili mʼmenemo.”
Sworn hath the Lord, Yahweh, by his own life, Declareth Yahweh, God of hosts, abhorring am I, the grandeur of Jacob, and, his palaces, I hate, —therefore will I cast off the city and the fulness thereof.
9 Ngati anthu khumi otsala adzabisala mʼnyumba imodzi, nawonso adzafa ndithu.
And it shall come to pass, though there be left remaining ten men in one house, yet shall they die;
10 Ndipo ngati mʼbale wake wa wina wakufayo, woyenera kusamala za maliro, adzafika kudzatulutsa mitembo mʼnyumbamo nʼkufunsa aliyense amene akubisalabe mʼnyumbamo kuti, “Kodi uli ndi wina wamoyo mʼmenemo?” Ndipo munthu wobisalayo ndi kuyankha kuti, “Ayi,” mʼbaleyo adzanena kuti, “Khala chete! Ife tisayerekeze kutchula dzina la Yehova.”
And a man’s near of kin, even he who is about to burn the bones, shall carry him out of the house, when he shall say to him that is in the hinder parts of the house—Are there yet any with thee? and he shall say—No one. Then shall he say—Hush! for we must not invoke the name of Yahweh.
11 Pakuti Yehova walamula kuti nyumba zikuluzikulu Iye adzazigamulagamula, ndipo nyumba zazingʼono zidzasanduka maduka okhaokha.
For lo! Yahweh, is giving command, and will smite the great house into ruins, —and the little house with clefts.
12 Kodi akavalo amathamanga pa thanthwe? Kodi wina amatipula ndi ngʼombe mʼnyanja? Koma chiweruzo cholungama mwachisandutsa kukhala zinthu zakupha ndipo chipatso cha chilungamo mwachisandutsa kukhala chowawa.
Shall horses run upon crag? or will a man plough [there] with oxen? For ye have turned to poison the sentence of justice, and the fruit of righteousness, to wormwood:
13 Inu amene mukunyadira kuti munagonjetsa Lo Debara ndipo mukunena kuti, “Kodi sitinatenge Karinaimu ndi mphamvu zathu zokha?”
Who rejoice in a thing of nought, —who say, Have we not by our own strength, taken to ourselves horns?
14 Koma Yehova Mulungu Wamphamvuzonse akulengeza kuti, “Inu nyumba ya Israeli, ndidzakudzutsirani mtundu wina wa anthu umene udzakuzunzani kuchokera ku Lebo Hamati mpaka ku Chigwa cha Araba.”
For behold me! raising up against you, O house of Israel, Declareth Yahweh, the God of hosts—a nation! And they shall crush you, from the entering in of Hamath, unto the torrent-bed of the waste plain.

< Amosi 6 >