< Amosi 6 >

1 Tsoka kwa amene simukulabadira kanthu ku Ziyoni, ndiponso kwa inu amene mukukhala mwamtendere pa Phiri la Samariya, inu anthu otchuka ochokera ku mtundu wa anthu omveka, kumene Aisraeli amafikako!
Woe to them that dwell at ease in Zion; That feel secure upon the mountain of Samaria; The honorable men of the chief of the nations, To whom the house of Israel resort!
2 Pitani ku mzinda wa Kaline mukawuyangʼane; mukapitenso ku Hamati-raba mzinda waukulu uja, ndipo mukatsikirenso ku Gati kwa Afilisti. Kodi mizinda imeneyi ndi yopambana maufumu anu awiriwa? Kodi dziko lawo ndi lalikulu kupambana lanu?
Pass over to Calneh, and see; And thence go to great Hamath; Then go down to Gath of the Philistines: Are they better than these kingdoms, Or is their border greater than your border?
3 Inu simulabadirako kuti tsiku loyipa lidzafika, zochita zanu zimafulumizitsa ulamuliro wankhanza.
Woe to them, that put far away the day of evil, And bring near the seat of oppression;
4 Mumagona pa mabedi owakongoletsa ndi minyanga ya njovu, mumagona pa mipando yanu ya wofuwofu. Mumadya ana ankhosa onona ndi ana angʼombe onenepa.
That lie upon beds of ivory, And stretch themselves upon their couches; That eat lambs from the flock, And calves from the stall;
5 Mumayimba azeze anu ndi kumangopeka nyimbo pa zingʼwenyengʼwenye ngati Davide.
That chant to the sound of the harp, And invent for themselves instruments of music, like David;
6 Mumamwera vinyo mʼzipanda zodzaza ndipo mumadzola mafuta abwino kwambiri, koma simumva chisoni ndi kuwonongeka kwa Yosefe.
That drink wine in bowls, And anoint themselves with the most precious perfumes, But grieve not for the destruction of Joseph!
7 Nʼchifukwa chake inu mudzakhala mʼgulu la anthu oyamba kupita ku ukapolo; maphwando ndi zikondwerero zanu zidzatheratu.
Therefore now shall they go captive at the head of the captives; Yea, the shouting of them that stretch themselves upon their couches shall cease.
8 Ambuye Yehova walumbira mʼdzina lake. Yehova Mulungu Wamphamvuzonse walengeza kuti, “Ndimanyansidwa ndi kunyada kwa Yakobo, ndimadana ndi nyumba zake zaufumu; Ine ndidzawupereka mzindawu pamodzi ndi zonse zili mʼmenemo.”
The Lord Jehovah hath sworn by himself, Thus saith Jehovah, the God of hosts: I abhor the pride of Jacob, And I hate his palaces; I will give up the city, and all that is therein.
9 Ngati anthu khumi otsala adzabisala mʼnyumba imodzi, nawonso adzafa ndithu.
And if ten men remain in one house, These also shall die.
10 Ndipo ngati mʼbale wake wa wina wakufayo, woyenera kusamala za maliro, adzafika kudzatulutsa mitembo mʼnyumbamo nʼkufunsa aliyense amene akubisalabe mʼnyumbamo kuti, “Kodi uli ndi wina wamoyo mʼmenemo?” Ndipo munthu wobisalayo ndi kuyankha kuti, “Ayi,” mʼbaleyo adzanena kuti, “Khala chete! Ife tisayerekeze kutchula dzina la Yehova.”
A man's relative, or a burner of the dead, shall take him up, To carry his bones out of the house, And he shall say to him that is in the innermost part of the house, Is there yet any one with thee? And he shall answer, No one! Then shall he say, Keep silence! For we may not make mention of the name of Jehovah.
11 Pakuti Yehova walamula kuti nyumba zikuluzikulu Iye adzazigamulagamula, ndipo nyumba zazingʼono zidzasanduka maduka okhaokha.
For behold Jehovah hath commanded, And he will smite the great house with breaches, And the small house with clefts.
12 Kodi akavalo amathamanga pa thanthwe? Kodi wina amatipula ndi ngʼombe mʼnyanja? Koma chiweruzo cholungama mwachisandutsa kukhala zinthu zakupha ndipo chipatso cha chilungamo mwachisandutsa kukhala chowawa.
Shall horses run upon rocks, Or will one plough rocks with oxen, That ye change justice into hemlock, And the fruit of equity into wormwood,
13 Inu amene mukunyadira kuti munagonjetsa Lo Debara ndipo mukunena kuti, “Kodi sitinatenge Karinaimu ndi mphamvu zathu zokha?”
Ye that rejoice in a thing of naught, And say, Have we not acquired dominion by our own strength?
14 Koma Yehova Mulungu Wamphamvuzonse akulengeza kuti, “Inu nyumba ya Israeli, ndidzakudzutsirani mtundu wina wa anthu umene udzakuzunzani kuchokera ku Lebo Hamati mpaka ku Chigwa cha Araba.”
Behold, O house of Israel, saith Jehovah, the God of hosts, I will raise against you a nation, That shall oppress you from Hamath Even to the brook of the desert.

< Amosi 6 >