< Amosi 6 >
1 Tsoka kwa amene simukulabadira kanthu ku Ziyoni, ndiponso kwa inu amene mukukhala mwamtendere pa Phiri la Samariya, inu anthu otchuka ochokera ku mtundu wa anthu omveka, kumene Aisraeli amafikako!
Běda pokoj majícím na Sionu, a doufajícím v horu Samařskou, kteréžto hory jsou slovoutné mimo jiné u těch národů, k nimž se scházejí dům Izraelský.
2 Pitani ku mzinda wa Kaline mukawuyangʼane; mukapitenso ku Hamati-raba mzinda waukulu uja, ndipo mukatsikirenso ku Gati kwa Afilisti. Kodi mizinda imeneyi ndi yopambana maufumu anu awiriwa? Kodi dziko lawo ndi lalikulu kupambana lanu?
Projděte až do Chalne, a odtud jděte do Emat veliké, a sstupte do Gát Filistinských, a shlédněte, jsou-li která království lepší nežli tato? Jest-li větší jejich kraj nežli kraj váš?
3 Inu simulabadirako kuti tsiku loyipa lidzafika, zochita zanu zimafulumizitsa ulamuliro wankhanza.
Kteříž smyslíte, že jest daleko den bídy, a přistavujete stolici nátisku.
4 Mumagona pa mabedi owakongoletsa ndi minyanga ya njovu, mumagona pa mipando yanu ya wofuwofu. Mumadya ana ankhosa onona ndi ana angʼombe onenepa.
Kteříž léhají na ložcích slonových, a rozkošně sobě počínají na postelích svých, kteříž jídají berany z stáda a telata nejtučnější,
5 Mumayimba azeze anu ndi kumangopeka nyimbo pa zingʼwenyengʼwenye ngati Davide.
Přizpěvujíce k loutně jako David, vymýšlejíce sobě nástroje muzické.
6 Mumamwera vinyo mʼzipanda zodzaza ndipo mumadzola mafuta abwino kwambiri, koma simumva chisoni ndi kuwonongeka kwa Yosefe.
Kteříž pijí z bání vinných, a drahými mastmi se maží, aniž jsou čitelni bolesti pro potření Jozefovo.
7 Nʼchifukwa chake inu mudzakhala mʼgulu la anthu oyamba kupita ku ukapolo; maphwando ndi zikondwerero zanu zidzatheratu.
Pročež jižť půjdou v zajetí v prvním houfu stěhujících se, a tak nastane žalost těm, kteříž sobě rozkošně počínají.
8 Ambuye Yehova walumbira mʼdzina lake. Yehova Mulungu Wamphamvuzonse walengeza kuti, “Ndimanyansidwa ndi kunyada kwa Yakobo, ndimadana ndi nyumba zake zaufumu; Ine ndidzawupereka mzindawu pamodzi ndi zonse zili mʼmenemo.”
Přisáhl Panovník Hospodin skrze sebe samého, dí Hospodin Bůh zástupů: V ohavnosti mám pýchu Jákobovu, i paláců jeho nenávidím, pročež vydám město i vše, což v něm jest.
9 Ngati anthu khumi otsala adzabisala mʼnyumba imodzi, nawonso adzafa ndithu.
I stane se, že pozůstane-li deset osob v domě jednom, i ti zemrou.
10 Ndipo ngati mʼbale wake wa wina wakufayo, woyenera kusamala za maliro, adzafika kudzatulutsa mitembo mʼnyumbamo nʼkufunsa aliyense amene akubisalabe mʼnyumbamo kuti, “Kodi uli ndi wina wamoyo mʼmenemo?” Ndipo munthu wobisalayo ndi kuyankha kuti, “Ayi,” mʼbaleyo adzanena kuti, “Khala chete! Ife tisayerekeze kutchula dzina la Yehova.”
A vezme někoho strýc jeho, aneb ten, kterýž mu strojí pohřeb, aby vynesl kosti z domu, a dí tomu, kdož jest v pokoji domu: Jest-liž ještě s tebou kdo? I dí: Není žádného. I řekne: Mlč, proto že nepřipomínali jména Hospodinova.
11 Pakuti Yehova walamula kuti nyumba zikuluzikulu Iye adzazigamulagamula, ndipo nyumba zazingʼono zidzasanduka maduka okhaokha.
Nebo aj, Hospodin přikáže, a bíti bude na dům veliký přívaly, a na dům menší rozsedlinami.
12 Kodi akavalo amathamanga pa thanthwe? Kodi wina amatipula ndi ngʼombe mʼnyanja? Koma chiweruzo cholungama mwachisandutsa kukhala zinthu zakupha ndipo chipatso cha chilungamo mwachisandutsa kukhala chowawa.
Zdaliž koni běžeti mohou po skále? Zdaliž ji kdo orati může voly? Nebo jste proměnili soud v jed, a ovoce spravedlnosti v pelynek,
13 Inu amene mukunyadira kuti munagonjetsa Lo Debara ndipo mukunena kuti, “Kodi sitinatenge Karinaimu ndi mphamvu zathu zokha?”
Vy, kteříž se veselíte, ano není z čeho, říkajíce: Zdaliž jsme svou silou nevzali sobě rohů?
14 Koma Yehova Mulungu Wamphamvuzonse akulengeza kuti, “Inu nyumba ya Israeli, ndidzakudzutsirani mtundu wina wa anthu umene udzakuzunzani kuchokera ku Lebo Hamati mpaka ku Chigwa cha Araba.”
Ale aj, já vzbudím proti vám, ó dome Izraelský, praví Hospodin Bůh zástupů, národ, kterýž vás ssouží, odtud, kudy se jde do Emat, až do potoka roviny.