< Amosi 5 >

1 Israeli, imva mawu awa, nyimbo ya maliro imene ndikuyimba za iweyo:
Чујте ову реч, нарицање које подижем за вама, доме Израиљев.
2 “Namwali Israeli wagwa, moti sadzadzukanso, wasiyidwa mʼdziko lake lomwe, popanda woti ndi kumudzutsa.”
Паде, неће више устати девојка Израиљева; бачена је на земљу своју, нема никога да је подигне.
3 Ambuye Yehova akuti, “Mzinda umene udzapite ku nkhondo ndi anthu 1,000 amphamvu udzatsala ndi anthu 100 okha; mzinda umene udzapite ku nkhondo ndi anthu 100 amphamvu udzatsala ndi anthu khumi okha basi.”
Јер овако вели Господ Господ: У граду из ког је излазила хиљада остаће стотина, а из ког је излазила стотина у њему ће остати десет дому Израиљевом.
4 Zimene Yehova akunena kwa nyumba ya Israeli ndi izi: “Mundifunefune kuti mukhale ndi moyo;
Јер овако вели Господ дому Израиљевом: Тражите ме, и бићете живи.
5 musafunefune Beteli, musapite ku Giligala, musapite ku Beeriseba. Pakuti Giligala adzatengedwa ndithu kupita ku ukapolo, ndipo Beteli adzawonongekeratu.”
А не тражите Ветиља, и не идите у Галгал, и не пролазите у Вирсавеју, јер ће Галгал отићи у ропство, а Ветиљ ће се обратити у ништа.
6 Funani Yehova kuti mukhale ndi moyo, mukapanda kutero Iye adzatentha nyumba ya Yosefe ngati moto; motowo udzawononga, ndipo sipadzakhala wina wozimitsa motowo ku Beteli.
Тражите Господа и бићете живи, да не обузме дом Јосифов као огањ и спали и не буде никога да гаси Ветиљ.
7 Inu amene mumasandutsa chiweruzo cholungama kukhala chowawa ndi kunyoza chilungamo.
Који обраћате суд у пелен, и правду на земљи обарате.
8 (Iye amene analenga nyenyezi za Nsangwe ndi Akamwiniatsatana, amene amasandutsa mdima kuti ukhale mmawa ndi kudetsa usana kuti ukhale usiku, amene amayitana madzi a mʼnyanja ndi kuwathira pa dziko lapansi, Yehova ndiye dzina lake.
Оног тражите који је створио звезде, кола и штапе, и који претвара сен смртни у јутро, а дан у тамну ноћ, који дозива воде морске и пролива их по земљи; име Му је Господ.
9 Iyeyo amabweretsa chiwonongeko modzidzimutsa pa anthu amphamvu ndi kuwononga mizinda yotetezedwa),
Који подиже погибао на јакога, те погибао дође на град.
10 inu mumadana ndi amene amadzudzula mʼbwalo la milandu ndi kunyoza amene amanena zoona.
Мрзе на оног који кара на вратима, и гаде се на оног који говори право.
11 Mumapondereza munthu wosauka ndi kumukakamiza kuti akupatseni tirigu. Nʼchifukwa chake, ngakhale mwamanga nyumba zamiyala yosema, inuyo simudzakhalamo. Ngakhale mwalima minda yabwino ya mphesa, inu simudzamwa vinyo wake.
Зато што газите сиромаха и узимате од њега жито у данак, саградисте куће од тесаног камена, али нећете седети у њима; насадисте лепе винограде, али нећете пити вино из њих.
12 Pakuti Ine ndikudziwa kuchuluka kwa zolakwa zanu ndi kukula kwa machimo anu. Inu mumapondereza anthu olungama ndi kulandira ziphuphu ndipo anthu osauka simuwaweruza mwachilungamo mʼmabwalo anu amilandu.
Јер знам безакоња ваша, којих је много, и грехе ваше, који су велики, који мучите праведника, примате поклоне и изврћете правду убогима на вратима.
13 Nʼchifukwa chake pa nthawi yotere munthu wanzeru sayankhulapo kanthu, popeza ndi nthawi yoyipa.
Зато ће праведни ћутати у ово време, јер је зло време.
14 Muyike mtima wanu pa zabwino osati pa zoyipa, kuti mukhale ndi moyo. Mukatero Yehova Mulungu Wamphamvuzonse adzakhala nanu, monga mmene mumanenera kuti ali nanu.
Тражите добро а не зло, да бисте били живи; и тако ће Господ Бог над војскама бити с вама, како рекосте.
15 Mudane ndi zoyipa, mukonde zabwino; mukhazikitse chiweruzo cholungama mʼmabwalo anu amilandu. Mwina mwake Yehova Mulungu Wamphamvuzonse adzachitira chifundo anthu otsala a mʼbanja la Yosefe.
Мрзите на зло и љубите добро, и поставите на вратима суд, не би ли се Господ Бог над војскама смиловао на остатак Јосифов.
16 Choncho izi ndi zimene Ambuye, Yehova Mulungu Wamphamvuzonse, akunena: “Mʼmisewu monse mudzakhala kulira mofuwula, ndi kulira chifukwa cha kuwawa kwa masautso kudzakhala paliponse. Adzayitana alimi kuti adzalire, ndipo anthu odziwa maliridwe anthetemya adzalira mofuwula.
Зато овако вели Господ Бог над војскама, Господ: Биће тужњава по свим улицама, и по свим путевима говориће: Јаох! Јаох! И зваће ратаре на жалост и на тужњаву оне који умеју нарицати.
17 Mʼminda yonse ya mpesa mudzakhala kulira kokhakokha, pakuti Ine ndidzadutsa pakati panu,” akutero Yehova.
И по свим ће виноградима бити тужњава, јер ћу проћи посред тебе, говори Господ.
18 Tsoka kwa inu amene mumalakalaka tsiku la Yehova! Chifukwa chiyani mumalakalaka tsiku la Yehova? Tsikulo kudzakhala mdima osati kuwala.
Тешко онима који желе дан Господњи! Шта ће вам дан Господњи? Тада је мрак а не видело.
19 Lidzakhala ngati tsiku limene munthu pothawa mkango amakumana ndi chimbalangondo, ngati pamene munthu walowa mʼnyumba, natsamira dzanja lake pa khoma ndipo njoka nʼkuluma.
Као да би ко бежао од лава па би га срео медвед; или као да би ко дошао у кућу и наслонио се руком на зид, па би га змија ујела.
20 Kodi tsiku la Yehova silidzakhala mdima osati kuwala, mdima wandiweyani, popanda powala pena paliponse?
Није ли дан Господњи мрак, а не видело? И тама, без светлости?
21 “Ndimadana nawo masiku anu achikondwerero ndipo ndimawanyoza; sindikondwera nayo misonkhano yanu.
Мрзим на ваше празнике, одбацио сам их, и нећу да миришем светковина ваших.
22 Ngakhale mupereke nsembe zopsereza ndi nsembe zachakudya, Ine sindidzazilandira. Ngakhale mupereke nsembe zabwino zachiyanjano, Ine sindidzaziyangʼana nʼkomwe.
Ако ми принесете жртве паљенице и приносе своје, нећу их примити, и нећу погледати на захвалне жртве од угојене стоке ваше.
23 Musandisokose nazo nyimbo zanu! Sindidzamvetsera kulira kwa azeze anu.
Уклони од мене буку песама својих, и свирања псалтира твојих, нећу да чујем.
24 Koma chiweruzo cholungama chiyende ngati madzi, chilungamo ngati mtsinje wosaphwa!
Него суд нека тече као вода и правда као силан поток.
25 “Kodi pa zaka makumi anayi zimene munakhala mʼchipululu muja munkandibweretsera nsembe ndi zopereka, inu nyumba ya Israeli?
Јесте ли мени приносили жртве и даре у пустињи четрдесет година, доме Израиљев?
26 Inu mwanyamula kachisi wa mfumu yanu, ndi nyenyezi ija Kaiwani, mulungu wanu, mafano amene munadzipangira.
Него сте носили шатор Молоха свог, и Хијуна, ликове своје, звезду бога свог, које сами себи начинисте.
27 Nʼchifukwa chake Ine ndidzakupititsani ku ukapolo, kutali kupitirira ku Damasiko,” akutero Yehova, amene dzina lake ndi Mulungu Wamphamvuzonse.
Зато ћу вас преселити иза Дамаска, говори Господ, коме је име Бог над војскама.

< Amosi 5 >