< Amosi 5 >
1 Israeli, imva mawu awa, nyimbo ya maliro imene ndikuyimba za iweyo:
Écoutez cette parole, que je profère sur vous, — une lamentation, — maison d’Israël:
2 “Namwali Israeli wagwa, moti sadzadzukanso, wasiyidwa mʼdziko lake lomwe, popanda woti ndi kumudzutsa.”
Elle est tombée, elle ne se relèvera plus, la vierge d’Israël! Elle est renversée sur sa terre, personne ne la relèvera.
3 Ambuye Yehova akuti, “Mzinda umene udzapite ku nkhondo ndi anthu 1,000 amphamvu udzatsala ndi anthu 100 okha; mzinda umene udzapite ku nkhondo ndi anthu 100 amphamvu udzatsala ndi anthu khumi okha basi.”
Car ainsi parle Yahweh: La ville qui se mettait en campagne avec mille guerriers en gardera cent; celle qui se mettait en campagne avec cent en gardera dix, pour la maison d’Israël.
4 Zimene Yehova akunena kwa nyumba ya Israeli ndi izi: “Mundifunefune kuti mukhale ndi moyo;
Car ainsi parle Yahweh à la maison d’Israël: Cherchez-moi et vivez!
5 musafunefune Beteli, musapite ku Giligala, musapite ku Beeriseba. Pakuti Giligala adzatengedwa ndithu kupita ku ukapolo, ndipo Beteli adzawonongekeratu.”
Ne cherchez pas Béthel, ne venez pas à Galgala, ne passez pas à Bersabée! Car Galgala sera emmené captif, et Béthel deviendra néant.
6 Funani Yehova kuti mukhale ndi moyo, mukapanda kutero Iye adzatentha nyumba ya Yosefe ngati moto; motowo udzawononga, ndipo sipadzakhala wina wozimitsa motowo ku Beteli.
Cherchez Yahweh et vivez, de peur qu’il ne fonde, comme un feu, sur la maison de Joseph, et ne la dévore, sans que Béthel ait personne pour éteindre.
7 Inu amene mumasandutsa chiweruzo cholungama kukhala chowawa ndi kunyoza chilungamo.
Ils changent le droit en absinthe, et jettent à terre la justice!
8 (Iye amene analenga nyenyezi za Nsangwe ndi Akamwiniatsatana, amene amasandutsa mdima kuti ukhale mmawa ndi kudetsa usana kuti ukhale usiku, amene amayitana madzi a mʼnyanja ndi kuwathira pa dziko lapansi, Yehova ndiye dzina lake.
Il a fait les Pléiades et Orion; il change en aurore les ténèbres, et le jour en une nuit obscure; il appelle les eaux de la mer, et les répand sur la face de la terre; Yahweh est son nom.
9 Iyeyo amabweretsa chiwonongeko modzidzimutsa pa anthu amphamvu ndi kuwononga mizinda yotetezedwa),
Il fait éclater la ruine sur le puissant, et la ruine fond sur la ville forte.
10 inu mumadana ndi amene amadzudzula mʼbwalo la milandu ndi kunyoza amene amanena zoona.
Ils haïssent à la Porte celui qui censure; et celui qui parle avec intégrité, ils l’ont en horreur.
11 Mumapondereza munthu wosauka ndi kumukakamiza kuti akupatseni tirigu. Nʼchifukwa chake, ngakhale mwamanga nyumba zamiyala yosema, inuyo simudzakhalamo. Ngakhale mwalima minda yabwino ya mphesa, inu simudzamwa vinyo wake.
C’est pourquoi, parce que vous foulez aux pieds le pauvre, et que vous prélevez sur lui un tribut de blé; vous avez bâti des maisons en pierres de taille, et vous n’y habiterez pas, vous avez planté des vignes excellentes, et vous n’en boirez pas le vin.
12 Pakuti Ine ndikudziwa kuchuluka kwa zolakwa zanu ndi kukula kwa machimo anu. Inu mumapondereza anthu olungama ndi kulandira ziphuphu ndipo anthu osauka simuwaweruza mwachilungamo mʼmabwalo anu amilandu.
Car je sais que nombreux sont vos crimes, que grands sont vos péchés, vous qui opprimez le juste, qui prenez des présents, et qui faites fléchir le droit des pauvres à la Porte.
13 Nʼchifukwa chake pa nthawi yotere munthu wanzeru sayankhulapo kanthu, popeza ndi nthawi yoyipa.
C’est pourquoi l’homme sage, en ce temps-ci, se tait; car c’est un temps mauvais.
14 Muyike mtima wanu pa zabwino osati pa zoyipa, kuti mukhale ndi moyo. Mukatero Yehova Mulungu Wamphamvuzonse adzakhala nanu, monga mmene mumanenera kuti ali nanu.
Cherchez le bien et non le mal, afin que vous viviez, et qu’ainsi Yahweh, le Dieu des armées, soit avec vous, comme vous le dites.
15 Mudane ndi zoyipa, mukonde zabwino; mukhazikitse chiweruzo cholungama mʼmabwalo anu amilandu. Mwina mwake Yehova Mulungu Wamphamvuzonse adzachitira chifundo anthu otsala a mʼbanja la Yosefe.
Haïssez le mal et aimez le bien, et restaurez le droit à la Porte: peut-être Yahweh, le Dieu des armées, aura-t-il pitié du reste de Joseph!
16 Choncho izi ndi zimene Ambuye, Yehova Mulungu Wamphamvuzonse, akunena: “Mʼmisewu monse mudzakhala kulira mofuwula, ndi kulira chifukwa cha kuwawa kwa masautso kudzakhala paliponse. Adzayitana alimi kuti adzalire, ndipo anthu odziwa maliridwe anthetemya adzalira mofuwula.
C’est pourquoi ainsi parle Yahweh, le Dieu des armées, le Seigneur: Dans toutes les places, on se lamentera; dans toutes les rues on dira: Hélas! hélas! On appellera le laboureur au deuil, et aux lamentations, avec ceux qui savent gémir.
17 Mʼminda yonse ya mpesa mudzakhala kulira kokhakokha, pakuti Ine ndidzadutsa pakati panu,” akutero Yehova.
Dans toutes les vignes on se lamentera; car je passerai au milieu de toi, dit Yahweh.
18 Tsoka kwa inu amene mumalakalaka tsiku la Yehova! Chifukwa chiyani mumalakalaka tsiku la Yehova? Tsikulo kudzakhala mdima osati kuwala.
Malheur à ceux qui désirent le jour de Yahweh! Que sera-t-il pour vous, le jour de Yahweh? Il sera ténèbres, et non lumière.
19 Lidzakhala ngati tsiku limene munthu pothawa mkango amakumana ndi chimbalangondo, ngati pamene munthu walowa mʼnyumba, natsamira dzanja lake pa khoma ndipo njoka nʼkuluma.
Comme un homme qui s’enfuit devant le lion, et l’ours vient à sa rencontre; il entre dans sa maison, appuie sa main sur le mur, et le serpent le mord!...
20 Kodi tsiku la Yehova silidzakhala mdima osati kuwala, mdima wandiweyani, popanda powala pena paliponse?
N’est-il pas ténèbres, le jour de Yahweh, et non lumière, obscurité, sans aucun éclat?
21 “Ndimadana nawo masiku anu achikondwerero ndipo ndimawanyoza; sindikondwera nayo misonkhano yanu.
Je hais, je dédaigne vos fêtes, je n’ai aucun goût à vos assemblées.
22 Ngakhale mupereke nsembe zopsereza ndi nsembe zachakudya, Ine sindidzazilandira. Ngakhale mupereke nsembe zabwino zachiyanjano, Ine sindidzaziyangʼana nʼkomwe.
Si vous m’offrez vos holocaustes et vos oblations, je n’y prends pas plaisir, et vos sacrifices de veaux engraissés, je ne les regarde pas.
23 Musandisokose nazo nyimbo zanu! Sindidzamvetsera kulira kwa azeze anu.
Éloigne de moi le bruit de tes cantiques; que je n’entende pas le son de tes harpes!
24 Koma chiweruzo cholungama chiyende ngati madzi, chilungamo ngati mtsinje wosaphwa!
Mais que le jugement coule comme l’eau, et la justice comme un torrent qui ne tarit pas!
25 “Kodi pa zaka makumi anayi zimene munakhala mʼchipululu muja munkandibweretsera nsembe ndi zopereka, inu nyumba ya Israeli?
Des sacrifices et des oblations m’en avez-vous offert, dans le désert pendant quarante ans, maison d’Israël?
26 Inu mwanyamula kachisi wa mfumu yanu, ndi nyenyezi ija Kaiwani, mulungu wanu, mafano amene munadzipangira.
Vous avez porté la tente de votre roi, et Kijoum, vos idoles, l’étoile de votre dieu, que vous vous êtes fabriqué.
27 Nʼchifukwa chake Ine ndidzakupititsani ku ukapolo, kutali kupitirira ku Damasiko,” akutero Yehova, amene dzina lake ndi Mulungu Wamphamvuzonse.
Je vous déporterai par delà Damas, dit Yahweh; Dieu des armées est son nom.