< Amosi 5 >
1 Israeli, imva mawu awa, nyimbo ya maliro imene ndikuyimba za iweyo:
You people [MTY] of Israel, listen to this funeral song that I will sing about you:
2 “Namwali Israeli wagwa, moti sadzadzukanso, wasiyidwa mʼdziko lake lomwe, popanda woti ndi kumudzutsa.”
“You are like [MET] a young woman, but in spite of that, you will certainly be struck down and you will never get up again! You will lie on the ground, abandoned, and there will be no one to help you stand up.”
3 Ambuye Yehova akuti, “Mzinda umene udzapite ku nkhondo ndi anthu 1,000 amphamvu udzatsala ndi anthu 100 okha; mzinda umene udzapite ku nkhondo ndi anthu 100 amphamvu udzatsala ndi anthu khumi okha basi.”
This is what Yahweh the Lord says to the people [MTY] of Israel: [“When your enemies attack you, ] and when 1,000 [of your soldiers] will go [to a battle], there will be only 100 who will survive. When 100 soldiers march out [from a city to fight], there will be only ten who will remain alive.”
4 Zimene Yehova akunena kwa nyumba ya Israeli ndi izi: “Mundifunefune kuti mukhale ndi moyo;
Yahweh continues to say to the people [MTY] of Israel: “You Israeli people, return to me! If you do that, you will continue to remain alive.
5 musafunefune Beteli, musapite ku Giligala, musapite ku Beeriseba. Pakuti Giligala adzatengedwa ndithu kupita ku ukapolo, ndipo Beteli adzawonongekeratu.”
Do not go to Bethel to seek [my help]; do not go to Gilgal [to worship]; do not [even] go to Beersheba, because [your enemies] will drag away [the people of] Gilgal to other countries, and Bethel will be completely destroyed.”
6 Funani Yehova kuti mukhale ndi moyo, mukapanda kutero Iye adzatentha nyumba ya Yosefe ngati moto; motowo udzawononga, ndipo sipadzakhala wina wozimitsa motowo ku Beteli.
So, come to Yahweh; if you do that, you will remain alive. If you do not do that, Yahweh will descend on you descendants [MTY] of Joseph like [SIM] a fire; that fire will burn everything in Bethel, and (nothing/no one) will be able to save that town.
7 Inu amene mumasandutsa chiweruzo cholungama kukhala chowawa ndi kunyoza chilungamo.
You people distort what is fair/right and cause [people to think that] it is something that is very bitter; you treat good things as though they are evil.
8 (Iye amene analenga nyenyezi za Nsangwe ndi Akamwiniatsatana, amene amasandutsa mdima kuti ukhale mmawa ndi kudetsa usana kuti ukhale usiku, amene amayitana madzi a mʼnyanja ndi kuwathira pa dziko lapansi, Yehova ndiye dzina lake.
[Do you know who] created all the groups of stars and put them in their places? [Each morning] he causes the darkness to become the dawn, and [each evening] he causes the daylight to become darkness. He scoops up water from the oceans [to become clouds], and then he dumps the water [from the clouds] onto the earth. The one who does those things is named Yahweh.
9 Iyeyo amabweretsa chiwonongeko modzidzimutsa pa anthu amphamvu ndi kuwononga mizinda yotetezedwa),
He causes strong [soldiers] to be killed, and causes the (high walls around/fortresses of) cities to be torn down.
10 inu mumadana ndi amene amadzudzula mʼbwalo la milandu ndi kunyoza amene amanena zoona.
[He is the one who will punish you] because you hate those who challenge anyone who tries to make unjust decisions, and you hate those who tell the truth in your courts.
11 Mumapondereza munthu wosauka ndi kumukakamiza kuti akupatseni tirigu. Nʼchifukwa chake, ngakhale mwamanga nyumba zamiyala yosema, inuyo simudzakhalamo. Ngakhale mwalima minda yabwino ya mphesa, inu simudzamwa vinyo wake.
You oppress poor people and force them to pay big taxes. You have built big stone mansions [for yourselves], but you will not be able to live in them. You have planted vineyards, but there will not be any [grapes for you to harvest to make] wine.
12 Pakuti Ine ndikudziwa kuchuluka kwa zolakwa zanu ndi kukula kwa machimo anu. Inu mumapondereza anthu olungama ndi kulandira ziphuphu ndipo anthu osauka simuwaweruza mwachilungamo mʼmabwalo anu amilandu.
I know all of your sins and the terrible crimes that you have committed. You oppress righteous/honest people, and you accept bribes. You do not allow judges to treat poor people justly.
13 Nʼchifukwa chake pa nthawi yotere munthu wanzeru sayankhulapo kanthu, popeza ndi nthawi yoyipa.
This is a time when [many people do] evil things, so people who have good sense say nothing [when they hear about such things being done].
14 Muyike mtima wanu pa zabwino osati pa zoyipa, kuti mukhale ndi moyo. Mukatero Yehova Mulungu Wamphamvuzonse adzakhala nanu, monga mmene mumanenera kuti ali nanu.
In order to remain alive, you must stop doing what is wrong, and start doing what is right. If you do that, the Commander of the armies of angels will be with you like you claim [that he always is].
15 Mudane ndi zoyipa, mukonde zabwino; mukhazikitse chiweruzo cholungama mʼmabwalo anu amilandu. Mwina mwake Yehova Mulungu Wamphamvuzonse adzachitira chifundo anthu otsala a mʼbanja la Yosefe.
Love what is good, and hate what is evil! Try to cause [judges] in your courts to make decisions that are right/fair! If you do those things, perhaps the Commander of the armies of angels will act mercifully toward [you descendants of] Joseph who are still alive.
16 Choncho izi ndi zimene Ambuye, Yehova Mulungu Wamphamvuzonse, akunena: “Mʼmisewu monse mudzakhala kulira mofuwula, ndi kulira chifukwa cha kuwawa kwa masautso kudzakhala paliponse. Adzayitana alimi kuti adzalire, ndipo anthu odziwa maliridwe anthetemya adzalira mofuwula.
“Because I, Yahweh, [will punish you for your sins], this is what I have solemnly declared: People will be wailing loudly in every street, and people will be very sorrowful in every plaza. Farmers will be summoned to [come and] weep, along with the other official mourners who will wail [for those who have died].
17 Mʼminda yonse ya mpesa mudzakhala kulira kokhakokha, pakuti Ine ndidzadutsa pakati panu,” akutero Yehova.
People will be wailing in your vineyards, because I will punish you [IDM] severely. [That will surely happen because] I, Yahweh, have said it!”
18 Tsoka kwa inu amene mumalakalaka tsiku la Yehova! Chifukwa chiyani mumalakalaka tsiku la Yehova? Tsikulo kudzakhala mdima osati kuwala.
Terrible things will happen to you who desire that it will soon be the day when Yahweh [will punish your enemies], because that will be a day of darkness, not of light.
19 Lidzakhala ngati tsiku limene munthu pothawa mkango amakumana ndi chimbalangondo, ngati pamene munthu walowa mʼnyumba, natsamira dzanja lake pa khoma ndipo njoka nʼkuluma.
[At that time, ] when you try to run from a lion, you will face a bear. When you run into your house [to be safe], and you put your hand on a wall, it will be bitten by a snake.
20 Kodi tsiku la Yehova silidzakhala mdima osati kuwala, mdima wandiweyani, popanda powala pena paliponse?
That day, [when he punishes people], will certainly be [RHQ] a very dark day [MET], without even a little bit of light.
21 “Ndimadana nawo masiku anu achikondwerero ndipo ndimawanyoza; sindikondwera nayo misonkhano yanu.
[Yahweh says], “I hate your religious celebrations and the times when you gather to worship me; I detest them [DOU].
22 Ngakhale mupereke nsembe zopsereza ndi nsembe zachakudya, Ine sindidzazilandira. Ngakhale mupereke nsembe zabwino zachiyanjano, Ine sindidzaziyangʼana nʼkomwe.
Even if you bring me offerings that will be completely burned [on the altar] and offerings of grain, I will no longer accept them. Even if you bring me offerings to renew/maintain fellowship with me, I will not pay any attention to them.
23 Musandisokose nazo nyimbo zanu! Sindidzamvetsera kulira kwa azeze anu.
So, stop singing noisy/loud songs! I will not listen when you play harps.
24 Koma chiweruzo cholungama chiyende ngati madzi, chilungamo ngati mtsinje wosaphwa!
Instead, your continually acting justly/fairly and righteously should be [never stop, ] like [SIM] [the water in] a river that never stops flowing.
25 “Kodi pa zaka makumi anayi zimene munakhala mʼchipululu muja munkandibweretsera nsembe ndi zopereka, inu nyumba ya Israeli?
You Israeli people [MTY], your [ancestors] wandered through the desert for 40 years; and during that time, they never brought any sacrifices and offerings to me!
26 Inu mwanyamula kachisi wa mfumu yanu, ndi nyenyezi ija Kaiwani, mulungu wanu, mafano amene munadzipangira.
But they carried the two idols that they had made— the idols of Succoth, the god [that they considered to be] their king, and Kaiwan, [the image of the] star [that they worshiped].
27 Nʼchifukwa chake Ine ndidzakupititsani ku ukapolo, kutali kupitirira ku Damasiko,” akutero Yehova, amene dzina lake ndi Mulungu Wamphamvuzonse.
Therefore, now I will force you to go to [a country that is] far beyond Damascus! [That will surely happen because] I, the Commander of the armies of angels, have said it!”