< Amosi 5 >

1 Israeli, imva mawu awa, nyimbo ya maliro imene ndikuyimba za iweyo:
to hear: hear [obj] [the] word [the] this which I to lift: loud upon you dirge house: household Israel
2 “Namwali Israeli wagwa, moti sadzadzukanso, wasiyidwa mʼdziko lake lomwe, popanda woti ndi kumudzutsa.”
to fall: fall not to add: again to arise: rise virgin Israel to leave upon land: soil her nothing to arise: raise her
3 Ambuye Yehova akuti, “Mzinda umene udzapite ku nkhondo ndi anthu 1,000 amphamvu udzatsala ndi anthu 100 okha; mzinda umene udzapite ku nkhondo ndi anthu 100 amphamvu udzatsala ndi anthu khumi okha basi.”
for thus to say Lord YHWH/God [the] city [the] to come out: come thousand to remain hundred and [the] to come out: come hundred to remain ten to/for house: household Israel
4 Zimene Yehova akunena kwa nyumba ya Israeli ndi izi: “Mundifunefune kuti mukhale ndi moyo;
for thus to say LORD to/for house: household Israel to seek me and to live
5 musafunefune Beteli, musapite ku Giligala, musapite ku Beeriseba. Pakuti Giligala adzatengedwa ndithu kupita ku ukapolo, ndipo Beteli adzawonongekeratu.”
and not to seek Bethel Bethel and [the] Gilgal not to come (in): come and Beersheba Beersheba not to pass for [the] Gilgal to reveal: remove to reveal: remove and Bethel Bethel to be to/for evil: trouble
6 Funani Yehova kuti mukhale ndi moyo, mukapanda kutero Iye adzatentha nyumba ya Yosefe ngati moto; motowo udzawononga, ndipo sipadzakhala wina wozimitsa motowo ku Beteli.
to seek [obj] LORD and to live lest to rush like/as fire house: household Joseph and to eat and nothing to quench to/for Bethel Bethel
7 Inu amene mumasandutsa chiweruzo cholungama kukhala chowawa ndi kunyoza chilungamo.
[the] to overturn to/for wormwood justice and righteousness to/for land: country/planet to rest
8 (Iye amene analenga nyenyezi za Nsangwe ndi Akamwiniatsatana, amene amasandutsa mdima kuti ukhale mmawa ndi kudetsa usana kuti ukhale usiku, amene amayitana madzi a mʼnyanja ndi kuwathira pa dziko lapansi, Yehova ndiye dzina lake.
to make Pleiades and Orion and to overturn to/for morning shadow and day night to darken [the] to call: call to to/for water [the] sea and to pour: pour them upon face: surface [the] land: country/planet LORD name his
9 Iyeyo amabweretsa chiwonongeko modzidzimutsa pa anthu amphamvu ndi kuwononga mizinda yotetezedwa),
[the] be cheerful violence upon strong and violence upon fortification to come (in): come
10 inu mumadana ndi amene amadzudzula mʼbwalo la milandu ndi kunyoza amene amanena zoona.
to hate in/on/with gate to rebuke and to speak: speak unblemished: blameless to abhor
11 Mumapondereza munthu wosauka ndi kumukakamiza kuti akupatseni tirigu. Nʼchifukwa chake, ngakhale mwamanga nyumba zamiyala yosema, inuyo simudzakhalamo. Ngakhale mwalima minda yabwino ya mphesa, inu simudzamwa vinyo wake.
to/for so because to trample you upon poor and tribute grain to take: take from him house: home cutting to build and not to dwell in/on/with them vineyard delight to plant and not to drink [obj] wine their
12 Pakuti Ine ndikudziwa kuchuluka kwa zolakwa zanu ndi kukula kwa machimo anu. Inu mumapondereza anthu olungama ndi kulandira ziphuphu ndipo anthu osauka simuwaweruza mwachilungamo mʼmabwalo anu amilandu.
for to know many transgression your and mighty sin your to vex righteous to take: take ransom and needy in/on/with gate to stretch
13 Nʼchifukwa chake pa nthawi yotere munthu wanzeru sayankhulapo kanthu, popeza ndi nthawi yoyipa.
to/for so [the] be prudent in/on/with time [the] he/she/it to silence: silent for time distress: evil he/she/it
14 Muyike mtima wanu pa zabwino osati pa zoyipa, kuti mukhale ndi moyo. Mukatero Yehova Mulungu Wamphamvuzonse adzakhala nanu, monga mmene mumanenera kuti ali nanu.
to seek good and not bad: evil because to live and to be so LORD God Hosts with you like/as as which to say
15 Mudane ndi zoyipa, mukonde zabwino; mukhazikitse chiweruzo cholungama mʼmabwalo anu amilandu. Mwina mwake Yehova Mulungu Wamphamvuzonse adzachitira chifundo anthu otsala a mʼbanja la Yosefe.
to hate bad: evil and to love: lover good and to set in/on/with gate justice perhaps be gracious LORD God Hosts remnant Joseph
16 Choncho izi ndi zimene Ambuye, Yehova Mulungu Wamphamvuzonse, akunena: “Mʼmisewu monse mudzakhala kulira mofuwula, ndi kulira chifukwa cha kuwawa kwa masautso kudzakhala paliponse. Adzayitana alimi kuti adzalire, ndipo anthu odziwa maliridwe anthetemya adzalira mofuwula.
to/for so thus to say LORD God Hosts Lord in/on/with all street/plaza mourning and in/on/with all outside to say Ah! Ah! and to call: call out farmer to(wards) mourning and mourning to(wards) to know wailing
17 Mʼminda yonse ya mpesa mudzakhala kulira kokhakokha, pakuti Ine ndidzadutsa pakati panu,” akutero Yehova.
and in/on/with all vineyard mourning for to pass in/on/with entrails: among your to say LORD
18 Tsoka kwa inu amene mumalakalaka tsiku la Yehova! Chifukwa chiyani mumalakalaka tsiku la Yehova? Tsikulo kudzakhala mdima osati kuwala.
woe! [the] to desire [obj] day LORD to/for what? this to/for you day LORD he/she/it darkness and not light
19 Lidzakhala ngati tsiku limene munthu pothawa mkango amakumana ndi chimbalangondo, ngati pamene munthu walowa mʼnyumba, natsamira dzanja lake pa khoma ndipo njoka nʼkuluma.
like/as as which to flee man: anyone from face: before [the] lion and to fall on him [the] bear and to come (in): come [the] house: home and to support hand his upon [the] wall and to bite him [the] serpent
20 Kodi tsiku la Yehova silidzakhala mdima osati kuwala, mdima wandiweyani, popanda powala pena paliponse?
not darkness day LORD and not light and gloom and not brightness to/for him
21 “Ndimadana nawo masiku anu achikondwerero ndipo ndimawanyoza; sindikondwera nayo misonkhano yanu.
to hate to reject feast your and not to smell in/on/with assembly your
22 Ngakhale mupereke nsembe zopsereza ndi nsembe zachakudya, Ine sindidzazilandira. Ngakhale mupereke nsembe zabwino zachiyanjano, Ine sindidzaziyangʼana nʼkomwe.
that if: except if: except to ascend: offer up to/for me burnt offering and offering your not to accept and peace offering fatling your not to look
23 Musandisokose nazo nyimbo zanu! Sindidzamvetsera kulira kwa azeze anu.
to turn aside: remove from upon me crowd song your and melody harp your not to hear: hear
24 Koma chiweruzo cholungama chiyende ngati madzi, chilungamo ngati mtsinje wosaphwa!
and to roll like/as water justice and righteousness like/as torrent: river strong
25 “Kodi pa zaka makumi anayi zimene munakhala mʼchipululu muja munkandibweretsera nsembe ndi zopereka, inu nyumba ya Israeli?
sacrifice and offering to approach: bring to/for me in/on/with wilderness forty year house: household Israel
26 Inu mwanyamula kachisi wa mfumu yanu, ndi nyenyezi ija Kaiwani, mulungu wanu, mafano amene munadzipangira.
and to lift: raise [obj] Sikkuth king your and [obj] Kiyyun image your star God your which to make to/for you
27 Nʼchifukwa chake Ine ndidzakupititsani ku ukapolo, kutali kupitirira ku Damasiko,” akutero Yehova, amene dzina lake ndi Mulungu Wamphamvuzonse.
and to reveal: remove [obj] you from further to/for Damascus to say LORD God Hosts name his

< Amosi 5 >