< Amosi 5 >

1 Israeli, imva mawu awa, nyimbo ya maliro imene ndikuyimba za iweyo:
Hear this word, a lamentation, which I take up against you, O house of Israel.
2 “Namwali Israeli wagwa, moti sadzadzukanso, wasiyidwa mʼdziko lake lomwe, popanda woti ndi kumudzutsa.”
The virgin of Israel is fallen; she shall no more arise: she is cast down upon her land; there is none to raise her up.
3 Ambuye Yehova akuti, “Mzinda umene udzapite ku nkhondo ndi anthu 1,000 amphamvu udzatsala ndi anthu 100 okha; mzinda umene udzapite ku nkhondo ndi anthu 100 amphamvu udzatsala ndi anthu khumi okha basi.”
For thus saith the Lord Jehovah: The city that went forth a thousand shall have a hundred left, and that which went forth a hundred shall have ten left, for the house of Israel.
4 Zimene Yehova akunena kwa nyumba ya Israeli ndi izi: “Mundifunefune kuti mukhale ndi moyo;
For thus saith Jehovah unto the house of Israel: Seek ye me, and ye shall live.
5 musafunefune Beteli, musapite ku Giligala, musapite ku Beeriseba. Pakuti Giligala adzatengedwa ndithu kupita ku ukapolo, ndipo Beteli adzawonongekeratu.”
And seek not Bethel, neither go to Gilgal, and pass not to Beer-sheba; for Gilgal shall surely go into captivity, and Bethel shall come to nought.
6 Funani Yehova kuti mukhale ndi moyo, mukapanda kutero Iye adzatentha nyumba ya Yosefe ngati moto; motowo udzawononga, ndipo sipadzakhala wina wozimitsa motowo ku Beteli.
Seek Jehovah, and ye shall live; lest he break out like fire in the house of Joseph, and devour [it], and there be none to quench [it] in Bethel.
7 Inu amene mumasandutsa chiweruzo cholungama kukhala chowawa ndi kunyoza chilungamo.
Ye who turn judgment to wormwood, and cast down righteousness to the earth,
8 (Iye amene analenga nyenyezi za Nsangwe ndi Akamwiniatsatana, amene amasandutsa mdima kuti ukhale mmawa ndi kudetsa usana kuti ukhale usiku, amene amayitana madzi a mʼnyanja ndi kuwathira pa dziko lapansi, Yehova ndiye dzina lake.
[seek him] that made the Pleiades and Orion, and turneth the shadow of death into the morning, and maketh the day dark with night; that calleth for the waters of the sea, and poureth them out upon the face of the earth: Jehovah is his name.
9 Iyeyo amabweretsa chiwonongeko modzidzimutsa pa anthu amphamvu ndi kuwononga mizinda yotetezedwa),
He causeth destruction to break forth suddenly upon the strong, and bringeth destruction upon the fortress.
10 inu mumadana ndi amene amadzudzula mʼbwalo la milandu ndi kunyoza amene amanena zoona.
They hate him that reproveth in the gate, and they abhor him that speaketh uprightly.
11 Mumapondereza munthu wosauka ndi kumukakamiza kuti akupatseni tirigu. Nʼchifukwa chake, ngakhale mwamanga nyumba zamiyala yosema, inuyo simudzakhalamo. Ngakhale mwalima minda yabwino ya mphesa, inu simudzamwa vinyo wake.
Forasmuch, therefore, as ye trample upon the poor, and take from him presents of wheat: ye have built houses of hewn stone, but ye shall not dwell in them; ye have planted pleasant vineyards, and ye shall not drink the wine of them.
12 Pakuti Ine ndikudziwa kuchuluka kwa zolakwa zanu ndi kukula kwa machimo anu. Inu mumapondereza anthu olungama ndi kulandira ziphuphu ndipo anthu osauka simuwaweruza mwachilungamo mʼmabwalo anu amilandu.
For I know how manifold are your transgressions and your sins mighty: they afflict the just, they take a bribe, and they turn aside [the right of] the needy in the gate.
13 Nʼchifukwa chake pa nthawi yotere munthu wanzeru sayankhulapo kanthu, popeza ndi nthawi yoyipa.
Therefore the prudent shall keep silence in this time; for it is an evil time.
14 Muyike mtima wanu pa zabwino osati pa zoyipa, kuti mukhale ndi moyo. Mukatero Yehova Mulungu Wamphamvuzonse adzakhala nanu, monga mmene mumanenera kuti ali nanu.
Seek good, and not evil, that ye may live; and so Jehovah, the God of hosts, shall be with you, as ye say.
15 Mudane ndi zoyipa, mukonde zabwino; mukhazikitse chiweruzo cholungama mʼmabwalo anu amilandu. Mwina mwake Yehova Mulungu Wamphamvuzonse adzachitira chifundo anthu otsala a mʼbanja la Yosefe.
Hate evil, and love good, and establish judgment in the gate: it may be that Jehovah, the God of hosts, will be gracious unto the remnant of Joseph.
16 Choncho izi ndi zimene Ambuye, Yehova Mulungu Wamphamvuzonse, akunena: “Mʼmisewu monse mudzakhala kulira mofuwula, ndi kulira chifukwa cha kuwawa kwa masautso kudzakhala paliponse. Adzayitana alimi kuti adzalire, ndipo anthu odziwa maliridwe anthetemya adzalira mofuwula.
Therefore thus saith Jehovah, the God of hosts, the Lord: Wailing shall be in all broadways; and they shall say in all the streets, Alas! alas! And they shall call the husbandman to mourning, and such as are skilful of lamentation to wailing.
17 Mʼminda yonse ya mpesa mudzakhala kulira kokhakokha, pakuti Ine ndidzadutsa pakati panu,” akutero Yehova.
And in all vineyards shall be wailing; for I will pass through the midst of thee, saith Jehovah.
18 Tsoka kwa inu amene mumalakalaka tsiku la Yehova! Chifukwa chiyani mumalakalaka tsiku la Yehova? Tsikulo kudzakhala mdima osati kuwala.
Woe unto you that desire the day of Jehovah! To what end is the day of Jehovah for you? It shall be darkness and not light:
19 Lidzakhala ngati tsiku limene munthu pothawa mkango amakumana ndi chimbalangondo, ngati pamene munthu walowa mʼnyumba, natsamira dzanja lake pa khoma ndipo njoka nʼkuluma.
as if a man fled from a lion, and a bear met him; or went into the house and leaned his hand on the wall, and a serpent bit him.
20 Kodi tsiku la Yehova silidzakhala mdima osati kuwala, mdima wandiweyani, popanda powala pena paliponse?
Shall not the day of Jehovah be darkness, and not light? even very dark, and no brightness in it?
21 “Ndimadana nawo masiku anu achikondwerero ndipo ndimawanyoza; sindikondwera nayo misonkhano yanu.
I hate, I despise your feasts, and I will not smell [a sweet odour] in your solemn assemblies.
22 Ngakhale mupereke nsembe zopsereza ndi nsembe zachakudya, Ine sindidzazilandira. Ngakhale mupereke nsembe zabwino zachiyanjano, Ine sindidzaziyangʼana nʼkomwe.
For if ye offer up unto me burnt-offerings and your oblations, I will not accept [them]; neither will I regard the peace-offerings of your fatted beasts.
23 Musandisokose nazo nyimbo zanu! Sindidzamvetsera kulira kwa azeze anu.
Take away from me the noise of thy songs, and I will not hear the melody of thy lutes;
24 Koma chiweruzo cholungama chiyende ngati madzi, chilungamo ngati mtsinje wosaphwa!
but let judgment roll down as waters, and righteousness as an ever-flowing stream.
25 “Kodi pa zaka makumi anayi zimene munakhala mʼchipululu muja munkandibweretsera nsembe ndi zopereka, inu nyumba ya Israeli?
Did ye bring unto me sacrifices and oblations in the wilderness forty years, O house of Israel?
26 Inu mwanyamula kachisi wa mfumu yanu, ndi nyenyezi ija Kaiwani, mulungu wanu, mafano amene munadzipangira.
Yea, ye took up the tabernacle of your Moloch, and Chiun your images, the star of your god, which ye had made to yourselves;
27 Nʼchifukwa chake Ine ndidzakupititsani ku ukapolo, kutali kupitirira ku Damasiko,” akutero Yehova, amene dzina lake ndi Mulungu Wamphamvuzonse.
and I will cause you to go into captivity beyond Damascus, saith Jehovah, whose name is the God of hosts.

< Amosi 5 >