< Amosi 5 >
1 Israeli, imva mawu awa, nyimbo ya maliro imene ndikuyimba za iweyo:
Slyšte slovo toto, kteréž já vynáším proti vám, totiž naříkání nad domem Izraelským.
2 “Namwali Israeli wagwa, moti sadzadzukanso, wasiyidwa mʼdziko lake lomwe, popanda woti ndi kumudzutsa.”
Padneť, aniž více povstane panna Izraelská; opuštěna bude v zemi své, nebude žádného, kdo by jí pozdvihl.
3 Ambuye Yehova akuti, “Mzinda umene udzapite ku nkhondo ndi anthu 1,000 amphamvu udzatsala ndi anthu 100 okha; mzinda umene udzapite ku nkhondo ndi anthu 100 amphamvu udzatsala ndi anthu khumi okha basi.”
Nebo takto praví Panovník Hospodin: V městě, z kteréhož vycházelo tisíc, zůstane sto, v tom pak, z kteréhož vycházelo sto, zůstane deset domu Izraelskému.
4 Zimene Yehova akunena kwa nyumba ya Israeli ndi izi: “Mundifunefune kuti mukhale ndi moyo;
Nebo takto praví Hospodin domu Izraelskému: Hledejte mne a živi buďte.
5 musafunefune Beteli, musapite ku Giligala, musapite ku Beeriseba. Pakuti Giligala adzatengedwa ndithu kupita ku ukapolo, ndipo Beteli adzawonongekeratu.”
A nehledejte Bethel, aniž choďte do Galgala, a do Bersabé se nesmýkejte; nebo Galgal jistotně se přestěhuje, a Bethel přijde na nic.
6 Funani Yehova kuti mukhale ndi moyo, mukapanda kutero Iye adzatentha nyumba ya Yosefe ngati moto; motowo udzawononga, ndipo sipadzakhala wina wozimitsa motowo ku Beteli.
Hledejte Hospodina, (a živi buďte, aby nepronikl jako oheň domu Jozefova, a nesehltil, a nebylo by žádného, kdo by uhasil Bethelské,
7 Inu amene mumasandutsa chiweruzo cholungama kukhala chowawa ndi kunyoza chilungamo.
Kteříž proměňují v pelynek soud, a spravedlnosti na zemi zanechávají),
8 (Iye amene analenga nyenyezi za Nsangwe ndi Akamwiniatsatana, amene amasandutsa mdima kuti ukhale mmawa ndi kudetsa usana kuti ukhale usiku, amene amayitana madzi a mʼnyanja ndi kuwathira pa dziko lapansi, Yehova ndiye dzina lake.
Toho, kterýž učinil Kuřátka i Oriona, kterýž proměňuje stín smrti v jitro, a den v temnosti noční, kterýž přivolává vody mořské, a vylévá je na svrchek země, jehož jméno jest Hospodin,
9 Iyeyo amabweretsa chiwonongeko modzidzimutsa pa anthu amphamvu ndi kuwononga mizinda yotetezedwa),
Kterýž očerstvuje zemdleného proti silnému, tak že zemdlený do pevnosti vchází.
10 inu mumadana ndi amene amadzudzula mʼbwalo la milandu ndi kunyoza amene amanena zoona.
Nenávidí trescícího v bráně, a toho, kdož mluví věci pravé, v ohavnosti mají.
11 Mumapondereza munthu wosauka ndi kumukakamiza kuti akupatseni tirigu. Nʼchifukwa chake, ngakhale mwamanga nyumba zamiyala yosema, inuyo simudzakhalamo. Ngakhale mwalima minda yabwino ya mphesa, inu simudzamwa vinyo wake.
A protož, proto že loupíte chudého, a břímě obilé béřete od něho, domů z tesaného kamení nastavěli jste, ale nebudete bydliti v nich; vinic výborných naštěpovali jste, ale nebudete píti vína z nich.
12 Pakuti Ine ndikudziwa kuchuluka kwa zolakwa zanu ndi kukula kwa machimo anu. Inu mumapondereza anthu olungama ndi kulandira ziphuphu ndipo anthu osauka simuwaweruza mwachilungamo mʼmabwalo anu amilandu.
Nebo já vím o mnohých nešlechetnostech vašich a velikých hříších vašich, že trápíte spravedlivého, berouce poctu, a nuzných při v bráně převracíte.
13 Nʼchifukwa chake pa nthawi yotere munthu wanzeru sayankhulapo kanthu, popeza ndi nthawi yoyipa.
Protož rozumný v ten čas mlčeti musí, nebo čas ten zlý jest.
14 Muyike mtima wanu pa zabwino osati pa zoyipa, kuti mukhale ndi moyo. Mukatero Yehova Mulungu Wamphamvuzonse adzakhala nanu, monga mmene mumanenera kuti ali nanu.
Hledejte dobrého a ne zlého, abyste živi byli, a budeť tak Hospodin Bůh zástupů s vámi, jakž pravíte.
15 Mudane ndi zoyipa, mukonde zabwino; mukhazikitse chiweruzo cholungama mʼmabwalo anu amilandu. Mwina mwake Yehova Mulungu Wamphamvuzonse adzachitira chifundo anthu otsala a mʼbanja la Yosefe.
Mějte v nenávisti zlé, a milujte dobré, a ustanovte v bráně soud; snad Hospodin Bůh zástupů milost učiní ostatkům Jozefovým.
16 Choncho izi ndi zimene Ambuye, Yehova Mulungu Wamphamvuzonse, akunena: “Mʼmisewu monse mudzakhala kulira mofuwula, ndi kulira chifukwa cha kuwawa kwa masautso kudzakhala paliponse. Adzayitana alimi kuti adzalire, ndipo anthu odziwa maliridwe anthetemya adzalira mofuwula.
Protož takto praví Panovník Hospodin, Bůh zástupů: Po všech ulicích bude kvílení, a na všecky strany zkřiknou: Ouvech, ouvech, a povolají oráče k pláči a kvílení s těmi, kteříž umějí naříkati.
17 Mʼminda yonse ya mpesa mudzakhala kulira kokhakokha, pakuti Ine ndidzadutsa pakati panu,” akutero Yehova.
Nýbrž i po všech vinicích bude kvílení, když projdu prostředkem tebe, dí Hospodin.
18 Tsoka kwa inu amene mumalakalaka tsiku la Yehova! Chifukwa chiyani mumalakalaka tsiku la Yehova? Tsikulo kudzakhala mdima osati kuwala.
Běda těm, kteříž žádají dne Hospodinova. K čemuž jest vám ten den Hospodinův, poněvadž jest tmy a ne světla?
19 Lidzakhala ngati tsiku limene munthu pothawa mkango amakumana ndi chimbalangondo, ngati pamene munthu walowa mʼnyumba, natsamira dzanja lake pa khoma ndipo njoka nʼkuluma.
Jako když by někdo utíkal před lvem, potkal by se s ním nedvěd; aneb když by všel do domu, a zpolehna rukou svou na stěnu, ušťkl by ho had.
20 Kodi tsiku la Yehova silidzakhala mdima osati kuwala, mdima wandiweyani, popanda powala pena paliponse?
Zdali není tmy a ne světla den Hospodinův, v němž není blesku, ale mrákota?
21 “Ndimadana nawo masiku anu achikondwerero ndipo ndimawanyoza; sindikondwera nayo misonkhano yanu.
Nenávidím, zavrhl jsem svátky vaše, aniž sobě chutnám slavností vašich.
22 Ngakhale mupereke nsembe zopsereza ndi nsembe zachakudya, Ine sindidzazilandira. Ngakhale mupereke nsembe zabwino zachiyanjano, Ine sindidzaziyangʼana nʼkomwe.
Nebo budete-li mi obětovati zápaly a suché oběti vaše, neoblíbím jich, a na pokojné oběti krmného dobytka vašeho nepopatřím.
23 Musandisokose nazo nyimbo zanu! Sindidzamvetsera kulira kwa azeze anu.
Odejmi ode mne hluk písní svých, ani hudby louten vašich nechci poslouchati.
24 Koma chiweruzo cholungama chiyende ngati madzi, chilungamo ngati mtsinje wosaphwa!
Ale povalí se jako voda soud, a spravedlnost jako potok silný.
25 “Kodi pa zaka makumi anayi zimene munakhala mʼchipululu muja munkandibweretsera nsembe ndi zopereka, inu nyumba ya Israeli?
Zdali jste mně oběti a dary obětovali na poušti za čtyřidceti let, dome Izraelský?
26 Inu mwanyamula kachisi wa mfumu yanu, ndi nyenyezi ija Kaiwani, mulungu wanu, mafano amene munadzipangira.
Nýbrž nosili jste stánek Melecha vašeho a Kijuna, obrazy vaše, hvězdu boha vašeho, kteréžto věci sami jste sobě zdělali.
27 Nʼchifukwa chake Ine ndidzakupititsani ku ukapolo, kutali kupitirira ku Damasiko,” akutero Yehova, amene dzina lake ndi Mulungu Wamphamvuzonse.
Protož přestěhuji vás dále než Damašské, praví Hospodin, jehož jméno jest Bůh zástupů.