< Amosi 5 >

1 Israeli, imva mawu awa, nyimbo ya maliro imene ndikuyimba za iweyo:
以色列家! 你們你們應聽這話,應聽我為你們唱的這首哀歌!
2 “Namwali Israeli wagwa, moti sadzadzukanso, wasiyidwa mʼdziko lake lomwe, popanda woti ndi kumudzutsa.”
「以色列處女已跌倒,不能再起;摔在地上,無人攙扶。
3 Ambuye Yehova akuti, “Mzinda umene udzapite ku nkhondo ndi anthu 1,000 amphamvu udzatsala ndi anthu 100 okha; mzinda umene udzapite ku nkhondo ndi anthu 100 amphamvu udzatsala ndi anthu khumi okha basi.”
因為吾主上主這樣論以色列家說:出一千兵的城只生還一百;出一百的,只生還十個。尋求上主者生,作惡者亡。
4 Zimene Yehova akunena kwa nyumba ya Israeli ndi izi: “Mundifunefune kuti mukhale ndi moyo;
因為上主這樣對以色列家說:你們尋求我,才可生存。
5 musafunefune Beteli, musapite ku Giligala, musapite ku Beeriseba. Pakuti Giligala adzatengedwa ndithu kupita ku ukapolo, ndipo Beteli adzawonongekeratu.”
不可往基耳加耳,不不去巴爾估巴,因為基耳加耳必被擄掠,貝特耳必化為烏有。
6 Funani Yehova kuti mukhale ndi moyo, mukapanda kutero Iye adzatentha nyumba ya Yosefe ngati moto; motowo udzawononga, ndipo sipadzakhala wina wozimitsa motowo ku Beteli.
你們尋求上主,才可生存,免得衪如火衝入若瑟家中,燒毀一切,無人能為以色列家撲滅。
7 Inu amene mumasandutsa chiweruzo cholungama kukhala chowawa ndi kunyoza chilungamo.
是衪創造了昴星和參星,變昏黑為黎明,使白畫為黑夜,召海水傾流於地面,衪名叫「雅威。」
8 (Iye amene analenga nyenyezi za Nsangwe ndi Akamwiniatsatana, amene amasandutsa mdima kuti ukhale mmawa ndi kudetsa usana kuti ukhale usiku, amene amayitana madzi a mʼnyanja ndi kuwathira pa dziko lapansi, Yehova ndiye dzina lake.
衪使滅亡閃擊強者,使毀滅臨於城堡。
9 Iyeyo amabweretsa chiwonongeko modzidzimutsa pa anthu amphamvu ndi kuwononga mizinda yotetezedwa),
凡以毒害代替公正,棄正義於地的,是有禍的!
10 inu mumadana ndi amene amadzudzula mʼbwalo la milandu ndi kunyoza amene amanena zoona.
他們憎恨在城門口主持公道的人,厭惡講真話的人。
11 Mumapondereza munthu wosauka ndi kumukakamiza kuti akupatseni tirigu. Nʼchifukwa chake, ngakhale mwamanga nyumba zamiyala yosema, inuyo simudzakhalamo. Ngakhale mwalima minda yabwino ya mphesa, inu simudzamwa vinyo wake.
為此,你們既然欺壓窮人,向他們橫征錢糧,你們縱然用方石建築了房屋,卻不得住在裏面;栽植了美麗的葡萄園,卻喝不到園中的酒。
12 Pakuti Ine ndikudziwa kuchuluka kwa zolakwa zanu ndi kukula kwa machimo anu. Inu mumapondereza anthu olungama ndi kulandira ziphuphu ndipo anthu osauka simuwaweruza mwachilungamo mʼmabwalo anu amilandu.
因為我知道你們罪惡多端,過犯重大:欺壓義人,接受賄賂,在城門口冤枉窮人;
13 Nʼchifukwa chake pa nthawi yotere munthu wanzeru sayankhulapo kanthu, popeza ndi nthawi yoyipa.
因此明智人在此時緘默不言,因為這是邪惡的時代。
14 Muyike mtima wanu pa zabwino osati pa zoyipa, kuti mukhale ndi moyo. Mukatero Yehova Mulungu Wamphamvuzonse adzakhala nanu, monga mmene mumanenera kuti ali nanu.
你們應尋求善,不可尋求惡:這樣你們才能生存;上主萬軍的天主也必與你們同在,正如你們所說的。
15 Mudane ndi zoyipa, mukonde zabwino; mukhazikitse chiweruzo cholungama mʼmabwalo anu amilandu. Mwina mwake Yehova Mulungu Wamphamvuzonse adzachitira chifundo anthu otsala a mʼbanja la Yosefe.
你們應惡惡好善,在城門口主張正義,或許萬軍的天主會憐憫若瑟的遺民。」
16 Choncho izi ndi zimene Ambuye, Yehova Mulungu Wamphamvuzonse, akunena: “Mʼmisewu monse mudzakhala kulira mofuwula, ndi kulira chifukwa cha kuwawa kwa masautso kudzakhala paliponse. Adzayitana alimi kuti adzalire, ndipo anthu odziwa maliridwe anthetemya adzalira mofuwula.
為此,萬軍的天主,吾主上主這樣說:「人必在一切廣場上哀悼,人必在各街道上說:哀哉! 哀哉! 並且召農人們來弔信,叫會哭的人來痛哭。
17 Mʼminda yonse ya mpesa mudzakhala kulira kokhakokha, pakuti Ine ndidzadutsa pakati panu,” akutero Yehova.
在所有的葡萄園中,人必哀哭,因為我要在你們中間經過」──上主說。
18 Tsoka kwa inu amene mumalakalaka tsiku la Yehova! Chifukwa chiyani mumalakalaka tsiku la Yehova? Tsikulo kudzakhala mdima osati kuwala.
「那仰望上主日子來臨的人是有福的! 上主的日子為你們有我們什麼好處﹖那是黑暗和無光明之日,
19 Lidzakhala ngati tsiku limene munthu pothawa mkango amakumana ndi chimbalangondo, ngati pamene munthu walowa mʼnyumba, natsamira dzanja lake pa khoma ndipo njoka nʼkuluma.
好似人逃避了獅子,又遇到了狗熊;進到房屋裏,手扶在牆上,卻被蛇咬傷。
20 Kodi tsiku la Yehova silidzakhala mdima osati kuwala, mdima wandiweyani, popanda powala pena paliponse?
上主的日子豈不是黑暗而沒有光明嗎﹖那日實在幽暗而漆黑!
21 “Ndimadana nawo masiku anu achikondwerero ndipo ndimawanyoza; sindikondwera nayo misonkhano yanu.
我痛恨厭惡你們的慶節;你們的盛會,我也不喜悅;
22 Ngakhale mupereke nsembe zopsereza ndi nsembe zachakudya, Ine sindidzazilandira. Ngakhale mupereke nsembe zabwino zachiyanjano, Ine sindidzaziyangʼana nʼkomwe.
既使你們給我奉獻全燔祭和素祭,我仍不悅納;既使你們獻上肥牲作和平祭,我也不垂顧。
23 Musandisokose nazo nyimbo zanu! Sindidzamvetsera kulira kwa azeze anu.
讓你們喧嚷的歌聲遠離我;你們的琴聲,我也不願再聽;
24 Koma chiweruzo cholungama chiyende ngati madzi, chilungamo ngati mtsinje wosaphwa!
如願公道如水常流,正義像川流不息的江河!
25 “Kodi pa zaka makumi anayi zimene munakhala mʼchipululu muja munkandibweretsera nsembe ndi zopereka, inu nyumba ya Israeli?
以色列家! 你們在曠野中四十年,何嘗給我奉獻過q和素祭﹖
26 Inu mwanyamula kachisi wa mfumu yanu, ndi nyenyezi ija Kaiwani, mulungu wanu, mafano amene munadzipangira.
你們應抬著自己所造的偶像,即你們的君王撒雇特和你們的星神克汪,
27 Nʼchifukwa chake Ine ndidzakupititsani ku ukapolo, kutali kupitirira ku Damasiko,” akutero Yehova, amene dzina lake ndi Mulungu Wamphamvuzonse.
因為 必使你們充軍到大馬士革之外,」名叫「萬軍的天主」的上主說。

< Amosi 5 >