< Amosi 4 >

1 Imvani mawu awa, inu ngʼombe zazikazi za ku Basani, okhala pa Phiri la Samariya, inu akazi amene mumapondereza anthu osauka ndi kuzunza anthu osowa ndi kumanena kwa amuna anu kuti, “Tipatseni zakumwa!”
Hörer detta ordet, I feta kor, som på Samarie berg ären, och gören dem fattiga orätt, och förtrycken den elända, och sägen till edra herrar: Bär hit, låt oss dricka.
2 Ambuye Yehova, mwa kuyera mtima kwake walumbira kuti, “Nthawi idzafika ndithu pamene adzakukokani ndi ngowe, womaliza wa inu adzakokedwa ndi mbedza.
Herren Herren hafver svorit vid sina helighet, si, den tiden kommer öfver eder, att man skall bära eder bort på stänger, och edra efterkommande i fiskakettlar;
3 Mudzatulukira mʼmingʼalu ya pa khoma aliyense payekhapayekha, ndipo mudzatayidwa ku Harimoni,” akutero Yehova.
Och skolen utgå igenom refvor, hvar och en för sig, och intill Harmon bortkastade varda, säger Herren.
4 “Bwerani ku Beteli mudzachimwe; ndi ku Giligala kuti mudzapitirize kuchimwa. Bweretsani nsembe zanu mmawa uliwonse, bweretsani chakhumi chanu masiku atatu aliwonse.
Ja, kommer hit till BethEl, och bedrifver synd: och till Gilgal, att I mågen föröka synderna; och bärer fram edor offer om morgonen, och edra tiond på tredje dagen;
5 Wotchani buledi wokhala ndi yisiti ngati nsembe yachiyamiko ndi kumanyadira poyera za zopereka zanu zaufulu. Inu Aisraeli, zinyadireni nsembezo, pakuti izi ndi zimene mumakonda kuchita,” akutero Ambuye Yehova.
Och röker af surdeg till tackoffer, och prediker om friviljogt offer, och förkunner det; ty I hafven det gerna så, I Israels barn, säger Herren Herren.
6 “Ndine amene ndinakusendetsani milomo mʼmizinda yanu yonse, ndipo munasowa chakudya mʼmizinda yanu. Komatu inu simunabwerere kwa Ine,” akutero Yehova.
Derföre hafver jag ock i alla edra städer gifvit eder lediga tänder, och brist på bröd I all edor rum; likväl omvänden I eder intet till mig, säger Herren.
7 “Ndinenso amene ndinamanga mvula patangotsala miyezi itatu kuti mukolole. Ndinagwetsa mvula pa mzinda wina, koma pa mzinda wina ayi, mvula inkagwa pa munda wina; koma sinagwe pa munda wina ndipo mbewu zinawuma.
Och jag hafver tillbakahållit regn öfver eder, medan ännu tre månader voro intill skördetiden; och jag lät regna uppå den ena staden, och uppå en annan stad lät jag intet regna; en åker vardt beregnad, och den andra åkren, som intet beregnad vardt, förtorkades.
8 Anthu ankayenda mzinda ndi mzinda kufuna madzi, koma sanapeze madzi okwanira kumwa. Komabe inu simunabwerere kwa Ine,” akutero Yehova.
Och två eller tre städer drogo intill en stad, på det de måtte dricka vatten, och kunde icke få sina nödtorft; likväl omvänden I eder intet till mig, säger Herren.
9 “Nthawi zambiri ndinakantha mbewu zanu ndiponso minda ya mpesa, ndinayikantha ndi chinsikwi ndiponso ndi chiwawu. Dzombe linawononga mikuyu yanu ndi mitengo ya olivi. Komabe inu simunabwerere kwa Ine,” akutero Yehova.
Jag plågade eder med torko, och med brandkorn; så åto ock gräsmatkar upp allt det i edra lustgårdar, vingårdar, på fikonaträ och oljoträ växte; likväl omvänden I eder intet till mig, säger Herren.
10 “Ine ndinabweretsa miliri pakati panu monga ndinachitira ku Igupto. Ndinapha anyamata anu ndi lupanga, ndinapereka akavalo anu kwa adani. Ndinakununkhitsani fungo la mitembo lochokera mʼmisasa yanu ya nkhondo. Komatu inu simunabwerere kwa Ine,” akutero Yehova.
Jag sände pestilentie ibland eder, lika som uti Egypten; jag drap edra unga män med svärd, och lät bortföra edra hästar fångna; jag lät stanket af edrom lägrom gå upp i edra näso; likväl omvänden I eder icke till mig, säger Herren.
11 “Ndinawononga ena mwa inu monga ndinawonongera Sodomu ndi Gomora. Inu munali ngati chikuni choyaka chimene chafumulidwa pa moto. Komabe inu simunabwerere kwa Ine,” akutero Yehova.
Jag omstörte somliga af eder, lika som Gud omstörte Sodom och Gomorra, så att I voren som en brand, den utur eldenom ryckt varder; likväl vänden I eder intet till mig, säger Herren.
12 “Choncho izi ndi zimene ndidzakuchitire iwe Israeli, chifukwa ndidzakuchitira zimenezi, konzekera kukumana ndi Mulungu wako, iwe Israeli.”
Derföre vill jag så göra med dig, Israel; efter jag nu så vill göra med dig, så skicka dig Israel, Och gack emot din Gud.
13 Iye amene amawumba mapiri, amalenga mphepo, ndipo amawululira munthu za mʼmaganizo ake, Iye amene amasandutsa usana kuti ukhale mdima, ndipo amayenda pa zitunda za dziko lapansi, dzina lake ndi Yehova Mulungu Wamphamvuzonse.
Ty si, han är den som gör bergen, skapar vädret, och kungör menniskone hvad hon tala skall; han gör morgonrodnan ( och ) mörkret; han går på jordenes höjder; han heter Herren Gud Zebaoth.

< Amosi 4 >