< Amosi 4 >

1 Imvani mawu awa, inu ngʼombe zazikazi za ku Basani, okhala pa Phiri la Samariya, inu akazi amene mumapondereza anthu osauka ndi kuzunza anthu osowa ndi kumanena kwa amuna anu kuti, “Tipatseni zakumwa!”
Ecoutez cette parole, vaches grasses qui êtes sur la montagne de Samarie, qui opprimez les indigènes et qui écrasez les pauvres, qui dites à vos maîtres: Apportez, et nous boirons.
2 Ambuye Yehova, mwa kuyera mtima kwake walumbira kuti, “Nthawi idzafika ndithu pamene adzakukokani ndi ngowe, womaliza wa inu adzakokedwa ndi mbedza.
Le Seigneur Dieu a juré par sa sainteté, disant: Voici que des jours viendront sur vous, et on vous enlèvera avec des perches, et on jettera vos restes dans des chaudières bouillantes.
3 Mudzatulukira mʼmingʼalu ya pa khoma aliyense payekhapayekha, ndipo mudzatayidwa ku Harimoni,” akutero Yehova.
Et vous sortirez par des ouvertures, l’une devant l’autre, et vous serez jetées en Armon, dit le Seigneur.
4 “Bwerani ku Beteli mudzachimwe; ndi ku Giligala kuti mudzapitirize kuchimwa. Bweretsani nsembe zanu mmawa uliwonse, bweretsani chakhumi chanu masiku atatu aliwonse.
Venez à Béthel, et agissez avec impiété; allez à Galgala et multipliez vos prévarications; et amenez dès le matin vos victimes, et tous les trois jours apportez vos dîmes.
5 Wotchani buledi wokhala ndi yisiti ngati nsembe yachiyamiko ndi kumanyadira poyera za zopereka zanu zaufulu. Inu Aisraeli, zinyadireni nsembezo, pakuti izi ndi zimene mumakonda kuchita,” akutero Ambuye Yehova.
Et offrez avec du levain des sacrifices de louange; et proclamez et annoncez des oblations volontaires; car c’est ainsi que vous l’avez voulu, fils d’Israël, dit le Seigneur Dieu.
6 “Ndine amene ndinakusendetsani milomo mʼmizinda yanu yonse, ndipo munasowa chakudya mʼmizinda yanu. Komatu inu simunabwerere kwa Ine,” akutero Yehova.
De là moi aussi, je vous ai donné un engourdissement de dents dans toutes vos villes, et un manque de pains dans tout votre pays, et vous n’êtes pas revenus à moi, dit le Seigneur.
7 “Ndinenso amene ndinamanga mvula patangotsala miyezi itatu kuti mukolole. Ndinagwetsa mvula pa mzinda wina, koma pa mzinda wina ayi, mvula inkagwa pa munda wina; koma sinagwe pa munda wina ndipo mbewu zinawuma.
Moi aussi, je vous ai refusé la pluie, lorsqu’il restait encore trois mois jusqu’à la moisson; et j’ai fait pleuvoir sur une cité, et sur une autre cité je n’ai pas fait pleuvoir; une partie n’a pas reçu de pluie, et une partie sur laquelle je n’ai pas fait pleuvoir a été desséchée.
8 Anthu ankayenda mzinda ndi mzinda kufuna madzi, koma sanapeze madzi okwanira kumwa. Komabe inu simunabwerere kwa Ine,” akutero Yehova.
Et deux et trois cités sont venues vers une seule cité afin d’y boire de l’eau, et elles n’ont pas été désaltérées; et vous n’êtes pas revenus à moi, dit le Seigneur.
9 “Nthawi zambiri ndinakantha mbewu zanu ndiponso minda ya mpesa, ndinayikantha ndi chinsikwi ndiponso ndi chiwawu. Dzombe linawononga mikuyu yanu ndi mitengo ya olivi. Komabe inu simunabwerere kwa Ine,” akutero Yehova.
Je vous ai frappés d’un vent brûlant et de la nielle, et la chenille a dévoré la multitude de vos jardins et de vos vignes, et vos plants d’oliviers et vos plants de figuiers; et vous n’êtes pas revenus à moi, dit le Seigneur.
10 “Ine ndinabweretsa miliri pakati panu monga ndinachitira ku Igupto. Ndinapha anyamata anu ndi lupanga, ndinapereka akavalo anu kwa adani. Ndinakununkhitsani fungo la mitembo lochokera mʼmisasa yanu ya nkhondo. Komatu inu simunabwerere kwa Ine,” akutero Yehova.
J’ai envoyé contre vous la mort sur la voie de l’Egypte; j’ai frappé par le glaive vos jeunes hommes; j’ai étendu la captivité jusque sur vos chevaux; j’ai fait monter l’infection de vos camps à vos narines; et vous n’êtes pas revenus à moi, dit le Seigneur.
11 “Ndinawononga ena mwa inu monga ndinawonongera Sodomu ndi Gomora. Inu munali ngati chikuni choyaka chimene chafumulidwa pa moto. Komabe inu simunabwerere kwa Ine,” akutero Yehova.
Je vous ai détruits, comme le Seigneur a détruit Sodome et Gomorrhe; vous êtes devenus comme un tison arraché à un incendie; et vous n’êtes pas revenus à moi, dit le Seigneur.
12 “Choncho izi ndi zimene ndidzakuchitire iwe Israeli, chifukwa ndidzakuchitira zimenezi, konzekera kukumana ndi Mulungu wako, iwe Israeli.”
C’est pourquoi je te traiterai ainsi, ô Israël; et après que je t’aurai traité ainsi, prépare-toi à aller à la rencontre de ton Dieu, ô Israël.
13 Iye amene amawumba mapiri, amalenga mphepo, ndipo amawululira munthu za mʼmaganizo ake, Iye amene amasandutsa usana kuti ukhale mdima, ndipo amayenda pa zitunda za dziko lapansi, dzina lake ndi Yehova Mulungu Wamphamvuzonse.
Parce que voici celui qui forme les montagnes et qui crée les vents, et qui annonce à l’homme sa parole, qui produit la nuée du matin, et qui marche sur les hauteurs de la terre; son nom est le Seigneur Dieu des armées.

< Amosi 4 >