< Amosi 4 >
1 Imvani mawu awa, inu ngʼombe zazikazi za ku Basani, okhala pa Phiri la Samariya, inu akazi amene mumapondereza anthu osauka ndi kuzunza anthu osowa ndi kumanena kwa amuna anu kuti, “Tipatseni zakumwa!”
to hear: hear [the] word [the] this heifer [the] Bashan which in/on/with mountain: mount Samaria [the] to oppress poor [the] to crush needy [the] to say to/for lord their to come (in): bring [emph?] and to drink
2 Ambuye Yehova, mwa kuyera mtima kwake walumbira kuti, “Nthawi idzafika ndithu pamene adzakukokani ndi ngowe, womaliza wa inu adzakokedwa ndi mbedza.
to swear Lord YHWH/God in/on/with holiness his for behold day to come (in): come upon you and to lift: raise [obj] you in/on/with hook and end your in/on/with thorn fishhook
3 Mudzatulukira mʼmingʼalu ya pa khoma aliyense payekhapayekha, ndipo mudzatayidwa ku Harimoni,” akutero Yehova.
and breach to come out: come woman: another before her and to throw [the] Harmon [to] utterance LORD
4 “Bwerani ku Beteli mudzachimwe; ndi ku Giligala kuti mudzapitirize kuchimwa. Bweretsani nsembe zanu mmawa uliwonse, bweretsani chakhumi chanu masiku atatu aliwonse.
to come (in): come Bethel Bethel and to transgress [the] Gilgal to multiply to/for to transgress and to come (in): bring to/for morning sacrifice your to/for three day tithe your
5 Wotchani buledi wokhala ndi yisiti ngati nsembe yachiyamiko ndi kumanyadira poyera za zopereka zanu zaufulu. Inu Aisraeli, zinyadireni nsembezo, pakuti izi ndi zimene mumakonda kuchita,” akutero Ambuye Yehova.
and to offer: offer from leaven thanksgiving and to call: call out voluntariness to hear: proclaim for so to love: lover son: descendant/people Israel utterance Lord YHWH/God
6 “Ndine amene ndinakusendetsani milomo mʼmizinda yanu yonse, ndipo munasowa chakudya mʼmizinda yanu. Komatu inu simunabwerere kwa Ine,” akutero Yehova.
and also I to give: give to/for you bluntness tooth in/on/with all city your and lack food: bread in/on/with all place your and not to return: return till me utterance LORD
7 “Ndinenso amene ndinamanga mvula patangotsala miyezi itatu kuti mukolole. Ndinagwetsa mvula pa mzinda wina, koma pa mzinda wina ayi, mvula inkagwa pa munda wina; koma sinagwe pa munda wina ndipo mbewu zinawuma.
and also I to withhold from you [obj] [the] rain in/on/with still three month to/for harvest and to rain upon city one and upon city one not to rain portion one to rain and portion which not to rain upon her to wither
8 Anthu ankayenda mzinda ndi mzinda kufuna madzi, koma sanapeze madzi okwanira kumwa. Komabe inu simunabwerere kwa Ine,” akutero Yehova.
and to shake two three city to(wards) city one to/for to drink water and not to satisfy and not to return: return till me utterance LORD
9 “Nthawi zambiri ndinakantha mbewu zanu ndiponso minda ya mpesa, ndinayikantha ndi chinsikwi ndiponso ndi chiwawu. Dzombe linawononga mikuyu yanu ndi mitengo ya olivi. Komabe inu simunabwerere kwa Ine,” akutero Yehova.
to smite [obj] you in/on/with blight and in/on/with mildew to multiply garden your and vineyard your and fig your and olive your to eat [the] locust and not to return: return till me utterance LORD
10 “Ine ndinabweretsa miliri pakati panu monga ndinachitira ku Igupto. Ndinapha anyamata anu ndi lupanga, ndinapereka akavalo anu kwa adani. Ndinakununkhitsani fungo la mitembo lochokera mʼmisasa yanu ya nkhondo. Komatu inu simunabwerere kwa Ine,” akutero Yehova.
to send: depart in/on/with you pestilence in/on/with way: conduct Egypt to kill in/on/with sword youth your with captivity horse your and to ascend: rise stench camp your and in/on/with face: nose your and not to return: return till me utterance LORD
11 “Ndinawononga ena mwa inu monga ndinawonongera Sodomu ndi Gomora. Inu munali ngati chikuni choyaka chimene chafumulidwa pa moto. Komabe inu simunabwerere kwa Ine,” akutero Yehova.
to overturn in/on/with you like/as overthrow God [obj] Sodom and [obj] Gomorrah and to be like/as firebrand to rescue (from fire *L(abh)*) and not to return: return till me utterance LORD
12 “Choncho izi ndi zimene ndidzakuchitire iwe Israeli, chifukwa ndidzakuchitira zimenezi, konzekera kukumana ndi Mulungu wako, iwe Israeli.”
to/for so thus to make: do to/for you Israel consequence for this to make: do to/for you to establish: prepare to/for to encounter: meet God your Israel
13 Iye amene amawumba mapiri, amalenga mphepo, ndipo amawululira munthu za mʼmaganizo ake, Iye amene amasandutsa usana kuti ukhale mdima, ndipo amayenda pa zitunda za dziko lapansi, dzina lake ndi Yehova Mulungu Wamphamvuzonse.
for behold to form: formed mountain: mount and to create spirit: breath and to tell to/for man what? thought his to make dawn darkness and to tread upon high place land: country/planet LORD God Hosts name his