< Amosi 4 >
1 Imvani mawu awa, inu ngʼombe zazikazi za ku Basani, okhala pa Phiri la Samariya, inu akazi amene mumapondereza anthu osauka ndi kuzunza anthu osowa ndi kumanena kwa amuna anu kuti, “Tipatseni zakumwa!”
Hear ye this word, ye heifers of Bashan, that are in the mountain of Samaria, who oppress the poor, who crush the needy, —who say to their lords, Bring in, and let us drink!
2 Ambuye Yehova, mwa kuyera mtima kwake walumbira kuti, “Nthawi idzafika ndithu pamene adzakukokani ndi ngowe, womaliza wa inu adzakokedwa ndi mbedza.
Sworn hath My Lord, Yahweh, by his own holiness, That lo! days, are coming upon you, —when he will take you away with hooks, and your followers with fishhooks;
3 Mudzatulukira mʼmingʼalu ya pa khoma aliyense payekhapayekha, ndipo mudzatayidwa ku Harimoni,” akutero Yehova.
And, through fissures, shall ye go out, every woman, straight before her, —and ye shall be thrust forth towards the castle, Declareth Yahweh.
4 “Bwerani ku Beteli mudzachimwe; ndi ku Giligala kuti mudzapitirize kuchimwa. Bweretsani nsembe zanu mmawa uliwonse, bweretsani chakhumi chanu masiku atatu aliwonse.
Enter ye Bethel, and transgress, At Gilgal, cause transgression, to abound, —Yea, carry in, every morning, your sacrifices, every three days, your tithes;
5 Wotchani buledi wokhala ndi yisiti ngati nsembe yachiyamiko ndi kumanyadira poyera za zopereka zanu zaufulu. Inu Aisraeli, zinyadireni nsembezo, pakuti izi ndi zimene mumakonda kuchita,” akutero Ambuye Yehova.
Yea, burn thou incense, of that which is leavened, as a thank-offering, and proclaim ye freewill-offerings, let them be known, —for, so, ye love [to have it], ye sons of Israel, Declareth My Lord, Yahweh.
6 “Ndine amene ndinakusendetsani milomo mʼmizinda yanu yonse, ndipo munasowa chakudya mʼmizinda yanu. Komatu inu simunabwerere kwa Ine,” akutero Yehova.
Moreover also, I, have given you cleanness of teeth throughout all your cities, and want of bread throughout all your dwelling-places, —Yet have ye not returned unto me, Declareth Yahweh.
7 “Ndinenso amene ndinamanga mvula patangotsala miyezi itatu kuti mukolole. Ndinagwetsa mvula pa mzinda wina, koma pa mzinda wina ayi, mvula inkagwa pa munda wina; koma sinagwe pa munda wina ndipo mbewu zinawuma.
Moreover also, I, have withholden from you the abundant rain, when yet there were only three mouths to the harvest, Or I might rain upon one city, and, on another city, might not rain, —One portion, would be rained upon, and, the portion whereupon it should not rain, would be dried up;
8 Anthu ankayenda mzinda ndi mzinda kufuna madzi, koma sanapeze madzi okwanira kumwa. Komabe inu simunabwerere kwa Ine,” akutero Yehova.
Then would two or three cities totter to one city to drink water, without being satisfied, —Yet have ye not returned unto me, Declareth Yahweh.
9 “Nthawi zambiri ndinakantha mbewu zanu ndiponso minda ya mpesa, ndinayikantha ndi chinsikwi ndiponso ndi chiwawu. Dzombe linawononga mikuyu yanu ndi mitengo ya olivi. Komabe inu simunabwerere kwa Ine,” akutero Yehova.
I have smitten you with blight and with mildew, When your gardens and your vineyards and your fig-trees and your olive-trees have increased, the creeping locust would devour them, —Yet have ye not returned unto me, Declareth Yahweh.
10 “Ine ndinabweretsa miliri pakati panu monga ndinachitira ku Igupto. Ndinapha anyamata anu ndi lupanga, ndinapereka akavalo anu kwa adani. Ndinakununkhitsani fungo la mitembo lochokera mʼmisasa yanu ya nkhondo. Komatu inu simunabwerere kwa Ine,” akutero Yehova.
I have sent among you pestilence, in the manner of Egypt, I have slain, with the sword, your young men, and therewith have been taken captive your horses, And I have caused to ascend—the stench of your camps, even into your own nostrils, Yet ye have not returned unto me, Declareth Yahweh.
11 “Ndinawononga ena mwa inu monga ndinawonongera Sodomu ndi Gomora. Inu munali ngati chikuni choyaka chimene chafumulidwa pa moto. Komabe inu simunabwerere kwa Ine,” akutero Yehova.
I have made an overthrew among you, like the divine overthrow of Sodom and Gomorrah, and ye have become like a brand snatched out of the burning, —Yet hate ye not returned unto me, Declareth Yahweh.
12 “Choncho izi ndi zimene ndidzakuchitire iwe Israeli, chifukwa ndidzakuchitira zimenezi, konzekera kukumana ndi Mulungu wako, iwe Israeli.”
Therefore, thus, will I do unto thee, O Israel, —Because this thing I will do unto thee, Prepare to meet thy God, O Israel.
13 Iye amene amawumba mapiri, amalenga mphepo, ndipo amawululira munthu za mʼmaganizo ake, Iye amene amasandutsa usana kuti ukhale mdima, ndipo amayenda pa zitunda za dziko lapansi, dzina lake ndi Yehova Mulungu Wamphamvuzonse.
For lo! He that fashioned the mountains, and created the wind, and who telleth the son of earth what is his thought, who turneth dawn into darkness, and marcheth upon the high places of the earth, Yahweh, God of hosts, is his name!