< Amosi 4 >

1 Imvani mawu awa, inu ngʼombe zazikazi za ku Basani, okhala pa Phiri la Samariya, inu akazi amene mumapondereza anthu osauka ndi kuzunza anthu osowa ndi kumanena kwa amuna anu kuti, “Tipatseni zakumwa!”
Slyšte slovo toto, ó krávy Bázanské, kteréž jste na horách Samařských, kteréž nátisk činíte chudým, a potíráte nuzné, kteréž říkáte pánům jejich: Přineste, ať pijeme.
2 Ambuye Yehova, mwa kuyera mtima kwake walumbira kuti, “Nthawi idzafika ndithu pamene adzakukokani ndi ngowe, womaliza wa inu adzakokedwa ndi mbedza.
Přisáhl Panovník Hospodin skrze svatost svou, že aj, dnové jdou na vás, v nichž vezme vás na háky, a potomky vaše na udice rybářské.
3 Mudzatulukira mʼmingʼalu ya pa khoma aliyense payekhapayekha, ndipo mudzatayidwa ku Harimoni,” akutero Yehova.
I vyjdete mezerami, každá tak, jakž stojí, a budete rozhazovati, což na palácích, dí Hospodin.
4 “Bwerani ku Beteli mudzachimwe; ndi ku Giligala kuti mudzapitirize kuchimwa. Bweretsani nsembe zanu mmawa uliwonse, bweretsani chakhumi chanu masiku atatu aliwonse.
Jdětež do Bethel, a buďtež poběhlci Galgala, rozmnožujte převrácenost, a přinášejte každého jitra oběti své, třetího roku desátky své.
5 Wotchani buledi wokhala ndi yisiti ngati nsembe yachiyamiko ndi kumanyadira poyera za zopereka zanu zaufulu. Inu Aisraeli, zinyadireni nsembezo, pakuti izi ndi zimene mumakonda kuchita,” akutero Ambuye Yehova.
A pálíce obět chvály z kvašených věcí, provolejte i oběti dobrovolné, a rozhlaste, poněvadž se vám tak líbí, ó synové Izraelští, dí Panovník Hospodin.
6 “Ndine amene ndinakusendetsani milomo mʼmizinda yanu yonse, ndipo munasowa chakudya mʼmizinda yanu. Komatu inu simunabwerere kwa Ine,” akutero Yehova.
A ačkoli já dal jsem vám čistotu zubů po všech městech vašich, totiž nedostatek chleba na všech místech vašich, a však jste se ke mně neobrátili, dí Hospodin.
7 “Ndinenso amene ndinamanga mvula patangotsala miyezi itatu kuti mukolole. Ndinagwetsa mvula pa mzinda wina, koma pa mzinda wina ayi, mvula inkagwa pa munda wina; koma sinagwe pa munda wina ndipo mbewu zinawuma.
Já také zadržel jsem vám déšť, když ještě tři měsícové byli do žně, a dštil jsem na jedno město, a na druhé město jsem nedštil; jeden díl deštěm svlažen byl, a ten díl, na kterýž nepršelo, uschl.
8 Anthu ankayenda mzinda ndi mzinda kufuna madzi, koma sanapeze madzi okwanira kumwa. Komabe inu simunabwerere kwa Ine,” akutero Yehova.
A toulali se dvě i tři města k jednomu městu, aby se napili vody, aniž se napiti mohli, a však jste se neobrátili ke mně, dí Hospodin.
9 “Nthawi zambiri ndinakantha mbewu zanu ndiponso minda ya mpesa, ndinayikantha ndi chinsikwi ndiponso ndi chiwawu. Dzombe linawononga mikuyu yanu ndi mitengo ya olivi. Komabe inu simunabwerere kwa Ine,” akutero Yehova.
Bil jsem vás suchem a rzí; hojnost, kterouž přinášely zahrady vaše a vinice vaše, i fíkoví vaše, i olivoví vaše, pojedly housenky, a však jste se neobrátili ke mně, dí Hospodin.
10 “Ine ndinabweretsa miliri pakati panu monga ndinachitira ku Igupto. Ndinapha anyamata anu ndi lupanga, ndinapereka akavalo anu kwa adani. Ndinakununkhitsani fungo la mitembo lochokera mʼmisasa yanu ya nkhondo. Komatu inu simunabwerere kwa Ine,” akutero Yehova.
Poslal jsem na vás mor tak jako na Egypt, zbil jsem mečem mládence vaše, v zajetí jsem vydal koně vaše, a učinil jsem, že vstupoval smrad vojsk vašich i v chřípě vaše, a však jste se neobrátili ke mně, dí Hospodin.
11 “Ndinawononga ena mwa inu monga ndinawonongera Sodomu ndi Gomora. Inu munali ngati chikuni choyaka chimene chafumulidwa pa moto. Komabe inu simunabwerere kwa Ine,” akutero Yehova.
Podvrátil jsem vás, jako podvrátil Bůh Sodomu a Gomoru, tak že jste byli jako hlavně vychvácená z ohně, vždy však neobrátili jste se ke mně, dí Hospodin.
12 “Choncho izi ndi zimene ndidzakuchitire iwe Israeli, chifukwa ndidzakuchitira zimenezi, konzekera kukumana ndi Mulungu wako, iwe Israeli.”
A protož takť učiním, ó Izraeli, a poněvadž takť učiniti míním, připraviž se vstříc Bohu svému, ó Izraeli.
13 Iye amene amawumba mapiri, amalenga mphepo, ndipo amawululira munthu za mʼmaganizo ake, Iye amene amasandutsa usana kuti ukhale mdima, ndipo amayenda pa zitunda za dziko lapansi, dzina lake ndi Yehova Mulungu Wamphamvuzonse.
Nebo aj, on jest sformovatel hor a stvořitel větrů, a oznamuje člověku, jaké by bylo jeho myšlení; činí z záře jitřní tmu, a šlapá po vysokostech země. Hospodin Bůh zástupů jest jméno jeho.

< Amosi 4 >