< Amosi 3 >

1 Inu Aisraeli, imvani mawu awa amene Yehova wayankhula kutsutsana nanu, kutsutsana ndi banja lonse limene analitulutsa mu Igupto:
Poslušajte to besedo, ki jo je Gospod govoril zoper vas, oh Izraelovi otroci, zoper celotno družino, ki sem jo privedel iz egiptovske dežele, rekoč:
2 “Inu nokha ndi amene ndinakusankhani pakati pa mabanja onse a dziko lapansi; nʼchifukwa chake ndidzakulangani chifukwa cha machimo anu onse.”
»Samo vas sem poznal izmed vseh zemeljskih družin, zato vas bom kaznoval zaradi vseh vaših krivičnosti.
3 Kodi anthu awiri nʼkuyendera limodzi asanapangane?
Mar lahko dva hodita skupaj, razen če se strinjata?
4 Kodi mkango umabangula mʼnkhalango usanagwire nyama? Kodi msona wamkango umalira mʼphanga mwake pamene sunagwire kanthu?
Ali bo lev rjovel v gozdu, kadar nima plena? Ali bo mlad lev vpil iz svojega brloga, če ni ničesar dobil?
5 Kodi mbalame nʼkutera pa msampha pamene palibe nyambo yake? Kodi msampha umafwamphuka usanakole kanthu?
Ali lahko ptica pade v zanko na tla, kjer zanjo ni nobene pasti? Mar nekdo pobere zanko s tal in ni sploh ničesar ujel?
6 Kodi pamene lipenga la nkhondo lalira mu mzinda, anthu sanjenjemera? Pamene tsoka lafika mu mzinda, kodi si Yehova amene wachititsa zimenezo?
Mar bo šofar zatrobil v mestu in ljudstvo ne bo prestrašeno? Mar bo zlo v mestu in Gospod tega ni storil?
7 Zoonadi Ambuye Yehova sachita kanthu asanawulule zimene akufuna kuchita kwa atumiki ake, aneneri.
Zagotovo Gospod Bog ne bo storil ničesar, da ne bi svojo skrivnost razodeval svojim služabnikom prerokom.
8 Mkango wabangula, ndani amene sachita mantha? Ambuye Yehova wayankhula, ndani amene sanganenere?
Lev je zarjovel, kdo se ne bo bal? Gospod Bog je spregovoril, kdo ne bi prerokoval?
9 Lengezani zimenezi ku nyumba zaufumu za ku Asidodi ndiponso ku nyumba zaufumu za ku Igupto: “Sonkhanani ku mapiri a ku Samariya; onani chisokonezo pakati pake ndiponso kuponderezana pakati pa anthu ake.”
Razglasi v palačah pri Ašdódu in v palačah egiptovske dežele in reci: ›Zberite se na gorah Samarije in glejte velike nemire v njeni sredi in zatirane v njeni sredi.‹
10 “Iwo sadziwa kuchita zolungama, ndipo amadzaza malo awo otetezedwa ndi zinthu zolanda ku nkhondo ndi zakuba,” akutero Yehova.
Kajti ne znajo delati pravilno, « govori Gospod, »tisti, ki kopičijo nasilje in rop v svojih palačah.«
11 Nʼchifukwa chake Ambuye Yehova akunena izi: “Mdani adzalizungulira dzikoli; iye adzagwetsa malinga ako, ndi kufunkha nyumba zako zaufumu.”
Zato tako govori Gospod Bog: »Nasprotnik bo celo naokoli dežele in tvojo moč bo privedel dol od tebe in tvoje palače bodo oplenjene.«
12 Yehova akuti, “Monga mʼbusa amalanditsa mʼkamwa mwa mkango miyendo iwiri yokha kapena msonga yokha ya khutu, moteronso ndimo mmene adzapulumukire Aisraeli amene amakhala mu Samariya pa msonga za mabedi awo, ndi ku Damasiko pa akakhutagona awo.”
Tako govori Gospod: »Kakor pastir iz levjih ust izvleče dve nogi ali košček ušesa, tako bodo izvlečeni Izraelovi otroci, ki prebivajo v Samariji, v kotu postelje in na ležišču v Damasku.
13 “Imvani izi ndipo mupereke umboni wotsutsa nyumba ya Yakobo,” akutero Ambuye, Yehova Mulungu Wamphamvuzonse.
Prisluhnite in pričujte v Jakobovi hiši, « govori Gospod Bog, Bog nad bojevniki,
14 “Pa tsiku limene ndidzalange Israeli chifukwa cha machimo ake, ndidzagumula maguwa ansembe a ku Beteli; nyanga za guwa zidzathyoka ndipo zidzagwa pansi.
»da na dan, ko bom na njem obiskal Izraelove prestopke, bom obiskal tudi oltarje Betela in oltarni rogovi bodo odsekani in padli na tla.
15 Ndidzagwetsa nyumba ya pa nthawi yozizira pamodzi ndi nyumba ya pa nthawi yotentha; nyumba zokongoletsedwa ndi minyanga ya njovu zidzawonongedwa ndipo nyumba zikuluzikulu zidzaphwasulidwa,” akutero Yehova.
Zimsko hišo bom udaril s poletno hišo [vred] in slonokoščene hiše bodo izginile in velike hiše bodo uničene, « govori Gospod.

< Amosi 3 >