< Amosi 3 >

1 Inu Aisraeli, imvani mawu awa amene Yehova wayankhula kutsutsana nanu, kutsutsana ndi banja lonse limene analitulutsa mu Igupto:
Écoutez cette parole, que l'Éternel a prononcée contre vous, enfants d'Israël, contre toute la famille que j'ai fait monter du pays d'Égypte.
2 “Inu nokha ndi amene ndinakusankhani pakati pa mabanja onse a dziko lapansi; nʼchifukwa chake ndidzakulangani chifukwa cha machimo anu onse.”
Il a dit: Je n'ai connu que vous d'entre toutes les familles de la terre; c'est pourquoi je vous châtierai pour toutes vos iniquités.
3 Kodi anthu awiri nʼkuyendera limodzi asanapangane?
Deux hommes marchent-ils ensemble, sans en être convenus?
4 Kodi mkango umabangula mʼnkhalango usanagwire nyama? Kodi msona wamkango umalira mʼphanga mwake pamene sunagwire kanthu?
Le lion rugit-il dans la forêt, sans qu'il ait une proie? Le lionceau jette-t-il son cri de sa tanière, sans qu'il ait rien pris?
5 Kodi mbalame nʼkutera pa msampha pamene palibe nyambo yake? Kodi msampha umafwamphuka usanakole kanthu?
L'oiseau tombe-t-il dans le filet qui est à terre, sans qu'il y ait un piège? Le filet se lève-t-il du sol, sans qu'il y ait rien de pris?
6 Kodi pamene lipenga la nkhondo lalira mu mzinda, anthu sanjenjemera? Pamene tsoka lafika mu mzinda, kodi si Yehova amene wachititsa zimenezo?
Si la trompette sonne dans une ville, le peuple ne sera-t-il pas alarmé? Et s'il arrive un malheur dans une ville, n'est-ce pas l'Éternel qui l'a fait?
7 Zoonadi Ambuye Yehova sachita kanthu asanawulule zimene akufuna kuchita kwa atumiki ake, aneneri.
Car le Seigneur, l'Éternel, ne fait rien, qu'il n'ait révélé son secret à ses serviteurs les prophètes.
8 Mkango wabangula, ndani amene sachita mantha? Ambuye Yehova wayankhula, ndani amene sanganenere?
Le lion rugit: qui ne craindra? Le Seigneur, l'Éternel, parle: qui ne prophétisera?
9 Lengezani zimenezi ku nyumba zaufumu za ku Asidodi ndiponso ku nyumba zaufumu za ku Igupto: “Sonkhanani ku mapiri a ku Samariya; onani chisokonezo pakati pake ndiponso kuponderezana pakati pa anthu ake.”
Faites entendre votre voix sur les palais d'Asdod et sur les palais du pays d'Égypte, et dites: Assemblez-vous sur les montagnes de Samarie, et voyez quels désordres au milieu d'elle et quelles oppressions dans son sein!
10 “Iwo sadziwa kuchita zolungama, ndipo amadzaza malo awo otetezedwa ndi zinthu zolanda ku nkhondo ndi zakuba,” akutero Yehova.
Ils ne savent pas faire ce qui est droit, dit l'Éternel, ils amassent la violence et la rapine dans leurs palais.
11 Nʼchifukwa chake Ambuye Yehova akunena izi: “Mdani adzalizungulira dzikoli; iye adzagwetsa malinga ako, ndi kufunkha nyumba zako zaufumu.”
C'est pourquoi, ainsi a dit le Seigneur, l'Éternel: L'ennemi vient, il entoure le pays; il abattra ta force et tes palais seront pillés.
12 Yehova akuti, “Monga mʼbusa amalanditsa mʼkamwa mwa mkango miyendo iwiri yokha kapena msonga yokha ya khutu, moteronso ndimo mmene adzapulumukire Aisraeli amene amakhala mu Samariya pa msonga za mabedi awo, ndi ku Damasiko pa akakhutagona awo.”
Ainsi a dit l'Éternel: Comme un berger sauve de la gueule du lion deux jambes ou un bout d'oreille; ainsi seront sauvés les enfants d'Israël qui sont assis dans Samarie, à l'angle d'une couche et sur le damas d'un lit.
13 “Imvani izi ndipo mupereke umboni wotsutsa nyumba ya Yakobo,” akutero Ambuye, Yehova Mulungu Wamphamvuzonse.
Écoutez et soyez mes témoins contre la maison de Jacob, dit le Seigneur, l'Éternel, le Dieu des armées:
14 “Pa tsiku limene ndidzalange Israeli chifukwa cha machimo ake, ndidzagumula maguwa ansembe a ku Beteli; nyanga za guwa zidzathyoka ndipo zidzagwa pansi.
Qu'au jour où je punirai Israël pour ses crimes, j'exercerai aussi la punition sur les autels de Béthel; les cornes de l'autel seront brisées et tomberont à terre.
15 Ndidzagwetsa nyumba ya pa nthawi yozizira pamodzi ndi nyumba ya pa nthawi yotentha; nyumba zokongoletsedwa ndi minyanga ya njovu zidzawonongedwa ndipo nyumba zikuluzikulu zidzaphwasulidwa,” akutero Yehova.
Et j'abattrai la maison d'hiver avec la maison d'été, les maisons d'ivoire périront, et de nombreuses maisons prendront fin, dit l'Éternel.

< Amosi 3 >