< Amosi 3 >

1 Inu Aisraeli, imvani mawu awa amene Yehova wayankhula kutsutsana nanu, kutsutsana ndi banja lonse limene analitulutsa mu Igupto:
“You people of Israel, I brought all your ancestors out of Egypt; so listen to what I am saying about you.
2 “Inu nokha ndi amene ndinakusankhani pakati pa mabanja onse a dziko lapansi; nʼchifukwa chake ndidzakulangani chifukwa cha machimo anu onse.”
From all the people-groups on the earth, I [chose and] took care of only you. That is the reason that I will punish you for the sins that you have committed.”
3 Kodi anthu awiri nʼkuyendera limodzi asanapangane?
Two [people] certainly cannot [RHQ] walk together if they have not [already] agreed [about what place they will start walking from].
4 Kodi mkango umabangula mʼnkhalango usanagwire nyama? Kodi msona wamkango umalira mʼphanga mwake pamene sunagwire kanthu?
A lion certainly does not [RHQ] roar in the bushes/forest if it has not killed another animal. It does not [RHQ] growl in its den if it is not eating [the flesh of an animal that it has caught].
5 Kodi mbalame nʼkutera pa msampha pamene palibe nyambo yake? Kodi msampha umafwamphuka usanakole kanthu?
No one can [RHQ] catch a bird if [he does] not [set] a trap for it. A trap does not spring shut unless some [animal] has not sprung the trap.
6 Kodi pamene lipenga la nkhondo lalira mu mzinda, anthu sanjenjemera? Pamene tsoka lafika mu mzinda, kodi si Yehova amene wachititsa zimenezo?
[Similarly, all] the people in a city certainly [RHQ] become afraid when [they hear someone] blowing a trumpet [to signal that enemies are attacking]. And when a city experiences disaster, Yahweh is the one who has caused it [RHQ].
7 Zoonadi Ambuye Yehova sachita kanthu asanawulule zimene akufuna kuchita kwa atumiki ake, aneneri.
And whatever Yahweh plans to do, he tells his prophets about it.
8 Mkango wabangula, ndani amene sachita mantha? Ambuye Yehova wayankhula, ndani amene sanganenere?
Everyone certainly becomes terrified [RHQ] when they hear a lion roar, and if Yahweh the Lord has given messages [to prophets like me], we certainly must [RHQ] proclaim those messages, [even if they cause people to become terrified].
9 Lengezani zimenezi ku nyumba zaufumu za ku Asidodi ndiponso ku nyumba zaufumu za ku Igupto: “Sonkhanani ku mapiri a ku Samariya; onani chisokonezo pakati pake ndiponso kuponderezana pakati pa anthu ake.”
[I said this to the leaders of Samaria] (OR, [Yahweh said this to me]): Send this message to the leaders [MET] in Ashdod [city] and to Egypt: “Come to the hills of Samaria and see [the way that their (leaders/wealthy people)] are causing people in that city to be terrified, and [the way that they] are causing the people to suffer!”
10 “Iwo sadziwa kuchita zolungama, ndipo amadzaza malo awo otetezedwa ndi zinthu zolanda ku nkhondo ndi zakuba,” akutero Yehova.
Yahweh says that the people there do not know how to do things that are right. Their homes are filled with [valuable things] that they have stolen or [taken] violently [from others].
11 Nʼchifukwa chake Ambuye Yehova akunena izi: “Mdani adzalizungulira dzikoli; iye adzagwetsa malinga ako, ndi kufunkha nyumba zako zaufumu.”
So Yahweh [our] God says that [soon] their enemies will come and tear down their (defenses/high city walls) and take away those valuable things.
12 Yehova akuti, “Monga mʼbusa amalanditsa mʼkamwa mwa mkango miyendo iwiri yokha kapena msonga yokha ya khutu, moteronso ndimo mmene adzapulumukire Aisraeli amene amakhala mu Samariya pa msonga za mabedi awo, ndi ku Damasiko pa akakhutagona awo.”
Yahweh has declared this: “When a lion attacks a sheep, [sometimes] a shepherd will be able to snatch from the lion’s mouth only two legs or an ear of the sheep. Similarly, [only] a few people from Samaria will escape, and [they will be able to rescue only] a part of a couch and a part of a bed.”
13 “Imvani izi ndipo mupereke umboni wotsutsa nyumba ya Yakobo,” akutero Ambuye, Yehova Mulungu Wamphamvuzonse.
The Commander of the armies of angels said this: “Proclaim [this message] about the descendants [MTY] of Jacob:
14 “Pa tsiku limene ndidzalange Israeli chifukwa cha machimo ake, ndidzagumula maguwa ansembe a ku Beteli; nyanga za guwa zidzathyoka ndipo zidzagwa pansi.
When I, Yahweh, punish [the people of] Israel because of the sins that they have committed, I will cause the altars at Bethel [town] to be destroyed; even the projections at the corners of the altars will be cut off and fall to the ground.
15 Ndidzagwetsa nyumba ya pa nthawi yozizira pamodzi ndi nyumba ya pa nthawi yotentha; nyumba zokongoletsedwa ndi minyanga ya njovu zidzawonongedwa ndipo nyumba zikuluzikulu zidzaphwasulidwa,” akutero Yehova.
I will cause the houses [that they live in during] the (winter/rainy season) and those [in which they live during] the (summer/dry season) to be torn down. [Beautiful] big houses and houses [that are decorated] with ivory will be destroyed. [That will surely happen because I], Yahweh, have said it!”

< Amosi 3 >