< Amosi 3 >

1 Inu Aisraeli, imvani mawu awa amene Yehova wayankhula kutsutsana nanu, kutsutsana ndi banja lonse limene analitulutsa mu Igupto:
Hear this word that Jehovah hath spoken against you, children of Israel, against the whole family that I brought up from the land of Egypt, saying,
2 “Inu nokha ndi amene ndinakusankhani pakati pa mabanja onse a dziko lapansi; nʼchifukwa chake ndidzakulangani chifukwa cha machimo anu onse.”
You only have I known of all the families of the earth; therefore will I visit upon you all your iniquities.
3 Kodi anthu awiri nʼkuyendera limodzi asanapangane?
Shall two walk together except they be agreed?
4 Kodi mkango umabangula mʼnkhalango usanagwire nyama? Kodi msona wamkango umalira mʼphanga mwake pamene sunagwire kanthu?
Will a lion roar in the forest when he hath no prey? Will a young lion cry out of his den if he have taken nothing?
5 Kodi mbalame nʼkutera pa msampha pamene palibe nyambo yake? Kodi msampha umafwamphuka usanakole kanthu?
Can a bird fall in a snare upon the earth when no gin [is laid] for him? Will the snare spring up from the earth when nothing at all hath been taken?
6 Kodi pamene lipenga la nkhondo lalira mu mzinda, anthu sanjenjemera? Pamene tsoka lafika mu mzinda, kodi si Yehova amene wachititsa zimenezo?
Shall a trumpet be blown in the city, and the people not be afraid? Shall there be evil in a city, and Jehovah not have done [it]?
7 Zoonadi Ambuye Yehova sachita kanthu asanawulule zimene akufuna kuchita kwa atumiki ake, aneneri.
But the Lord Jehovah will do nothing, but he revealeth his secret unto his servants the prophets.
8 Mkango wabangula, ndani amene sachita mantha? Ambuye Yehova wayankhula, ndani amene sanganenere?
The lion hath roared, — who will not fear? The Lord Jehovah hath spoken, — who can but prophesy?
9 Lengezani zimenezi ku nyumba zaufumu za ku Asidodi ndiponso ku nyumba zaufumu za ku Igupto: “Sonkhanani ku mapiri a ku Samariya; onani chisokonezo pakati pake ndiponso kuponderezana pakati pa anthu ake.”
Publish in the palaces at Ashdod, and in the palaces in the land of Egypt, and say, Assemble yourselves upon the mountains of Samaria, and behold the great uproar in the midst thereof, and the oppressions that are within her:
10 “Iwo sadziwa kuchita zolungama, ndipo amadzaza malo awo otetezedwa ndi zinthu zolanda ku nkhondo ndi zakuba,” akutero Yehova.
and they know not to do right, saith Jehovah, who store up violence and plunder in their palaces.
11 Nʼchifukwa chake Ambuye Yehova akunena izi: “Mdani adzalizungulira dzikoli; iye adzagwetsa malinga ako, ndi kufunkha nyumba zako zaufumu.”
Therefore thus saith the Lord Jehovah: An adversary! — even round about the land! And he shall bring down thy strength from thee, and thy palaces shall be pillaged.
12 Yehova akuti, “Monga mʼbusa amalanditsa mʼkamwa mwa mkango miyendo iwiri yokha kapena msonga yokha ya khutu, moteronso ndimo mmene adzapulumukire Aisraeli amene amakhala mu Samariya pa msonga za mabedi awo, ndi ku Damasiko pa akakhutagona awo.”
Thus saith Jehovah: Like as the shepherd rescueth out of the jaw of the lion two legs, or a piece of an ear; so shall the children of Israel be rescued that sit in Samaria in the corner of a couch, and upon the damask of a bed.
13 “Imvani izi ndipo mupereke umboni wotsutsa nyumba ya Yakobo,” akutero Ambuye, Yehova Mulungu Wamphamvuzonse.
Hear ye, and testify in the house of Jacob, saith the Lord Jehovah, the God of hosts,
14 “Pa tsiku limene ndidzalange Israeli chifukwa cha machimo ake, ndidzagumula maguwa ansembe a ku Beteli; nyanga za guwa zidzathyoka ndipo zidzagwa pansi.
that in the day that I shall visit the transgressions of Israel upon him, I will also punish the altars of Bethel; and the horns of the altar shall be cut off, and fall to the ground.
15 Ndidzagwetsa nyumba ya pa nthawi yozizira pamodzi ndi nyumba ya pa nthawi yotentha; nyumba zokongoletsedwa ndi minyanga ya njovu zidzawonongedwa ndipo nyumba zikuluzikulu zidzaphwasulidwa,” akutero Yehova.
And I will smite the winter-house with the summer-house; and the houses of ivory shall perish, and many houses shall have an end, saith Jehovah.

< Amosi 3 >